Canções de louvor
1Nesse dia, dirás:
“Eu te louvo, Senhor!
É verdade que estiveste irado contra mim,
mas agora confortas-me.
2Vejam bem, Deus veio salvar-me!
Tenho razão para confiar e nada recear,
porque o Senhor é a minha força.
É ele quem me leva a cantar!
Ele é a minha salvação!”
3Oh! Que alegria poder beber da fonte da salvação!
4Nesse dia maravilhoso dirão:
“Louvem o Senhor!
Louvem o seu nome!
Contem ao mundo como as suas obras são maravilhosas!
Como o seu poder é grande!
5Cantem ao Senhor, porque fez coisas maravilhosas!
Que isso se saiba em toda a Terra!
6Que os habitantes de Sião cantem bem alto os seus louvores,
e que o façam com alegria!
Porque grande e poderoso é o Santo de Israel,
que vive no vosso meio!”
Nyimbo za Mayamiko
1Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati:
“Ndikukuyamikani, Inu Yehova;
chifukwa ngakhale munandipsera mtima,
mkwiyo wanu wachoka,
ndipo mwanditonthoza.
2Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga;
ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;
Iye wakhala chipulumutso changa.”
3Mudzakondwera popeza Yehova
ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
4Tsiku limenelo mudzati:
“Yamikani Yehova, tamandani dzina lake;
mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu,
ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
5Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu;
zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
6Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni;
pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”