Psaltaren 47 – NUB & CCL

Swedish Contemporary Bible

Psaltaren 47:1-10

Psalm 47

Herren är kung

1För körledaren. Av Korachs ättlingar. En psalm.

2Klappa händer, alla folk!

Höj jubelrop till Gud och gläd er!

3Herren, den Högste, är fruktansvärd,

han är en stor kung över hela jorden.

4Han lade nationer under oss,

folk under våra fötter.

5Han utvalde åt oss vår arvedel,

Jakobs stolthet, som han älskade. Séla

6Gud har stigit upp under jubelrop,

Herren vid trumpeters ljud.

7Lovsjung Gud, lovsjung!

Lovsjung vår kung, lovsjung!

8Gud är kung över hela jorden,

lovsjung honom med en psalm47:8 Här finns ordet maskil, vars betydelse inte är känd (se not till 32:1)..

9Gud är kung över folken,

han sitter på sin helighets tron.

10Folkens förnäma samlas

som Abrahams Guds folk.

Jordens mäktiga tillhör Gud,

han är upphöjd över allt.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 47:1-9

Salimo 47

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora.

1Ombani mʼmanja, inu anthu onse;

fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.

2Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba;

Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!

3Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu;

anayika anthu pansi pa mapazi athu.

4Iye anatisankhira cholowa chathu,

chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda.

Sela

5Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe,

Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.

6Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando;

imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.

7Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi;

imbirani Iye salimo la matamando.

8Mulungu akulamulira mitundu ya anthu;

Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.

9Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana

monga anthu a Mulungu wa Abrahamu,

pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu;

Iye wakwezedwa kwakukulu.