Псалми 137 – NSP & CCL

New Serbian Translation

Псалми 137:1-9

Псалам 137

1Седели смо тамо, поред река Вавилона

и плакали кад би се сетили Сиона.

2О тамошње смо врбе

повешали харфе своје,

3јер су наши тлачитељи од нас захтевали песму;

мучитељи наши да се веселимо:

„Певајте нам песму о Сиону!“

4Како да певамо Господњу песму

у туђинској земљи?

5О, Јерусалиме, ако бих тебе заборавио,

заборављена била и десница моја!

6Језик ми се за непце слепио

ако те се не сетио,

ако се не радовао Јерусалиму

више него и најбољем своме!

7О, Господе, сети се Едомаца

што су на дан пада Јерусалима говорили:

„Разваљујте! Разваљујте га до темеља!“

8О, ћерко вавилонска,

што ћеш бити разорена!

Благо оном који ти узврати истом мером,

онако како си чинила нама.

9Благо оном ко ти нејач зграби

и о стену смрска!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 137:1-9

Salimo 137

1Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira

pamene tinakumbukira Ziyoni.

2Kumeneko, pa mitengo ya misondozi

tinapachika apangwe athu,

3pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo.

Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo;

iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”

4Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova

mʼdziko lachilendo?

5Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu,

dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.

6Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga

ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu,

ngati sindiyesa iwe

chimwemwe changa chachikulu.

7Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita

pa tsiku limene Yerusalemu anagonja.

Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi

mpaka pa maziko ake!”

8Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa,

wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera

pa zimene watichitira.

9Amene adzagwira makanda ako

ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.