Psalm 124
A song of ascents. Of David.
1If the Lord had not been on our side—
let Israel say—
2if the Lord had not been on our side
when people attacked us,
3they would have swallowed us alive
when their anger flared against us;
4the flood would have engulfed us,
the torrent would have swept over us,
5the raging waters
would have swept us away.
6Praise be to the Lord,
who has not let us be torn by their teeth.
7We have escaped like a bird
from the fowler’s snare;
the snare has been broken,
and we have escaped.
8Our help is in the name of the Lord,
the Maker of heaven and earth.
Salimo 124
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
1Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
anene tsono Israeli,
2akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
potiwukira anthuwo,
3iwo atatipsera mtima,
akanatimeza amoyo;
4chigumula chikanatimiza,
mtsinje ukanatikokolola,
5madzi a mkokomo
akanatikokolola.
6Atamandike Yehova,
amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
7Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame
yokodwa mu msampha wa mlenje;
msampha wathyoka,
ndipo ife tapulumuka.
8Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova
wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.