Job 25 – NIV & CCL

New International Version

Job 25:1-6

Bildad

1Then Bildad the Shuhite replied:

2“Dominion and awe belong to God;

he establishes order in the heights of heaven.

3Can his forces be numbered?

On whom does his light not rise?

4How then can a mortal be righteous before God?

How can one born of woman be pure?

5If even the moon is not bright

and the stars are not pure in his eyes,

6how much less a mortal, who is but a maggot—

a human being, who is only a worm!”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 25:1-6

Mawu a Bilidadi

1Apo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,

2“Ulamuliro ndi kuopsa ndi za Mulungu,

Iye amakhazikitsa bata mu ufumu wake kumwambako.

3Kodi magulu ake ankhondo nʼkuwerengeka?

Kodi kuwala kwake sikuwalira ndani?

4Kodi munthu angakhale bwanji wolungama pamaso pa Mulungu?

Kodi munthu wobadwa mwa mayi angakhale wangwiro?

5Ngati mwezi sutha kuwala kwenikweni,

ndipo nyenyezi sizitha kuwala pamaso pake,

6nanji tsono munthu amene ali ngati mphutsi,

mwana wa munthu amene ali ngati nyongolotsi!”