Zaburi 144 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Zaburi 144:1-15

Zaburi 144

Mfalme Amshukuru Mungu Kwa Ushindi

Zaburi ya Daudi.

1144:1 Mwa 49:24; 2Sam 22:35Sifa ni kwa Bwana Mwamba wangu,

aifundishaye mikono yangu vita,

na vidole vyangu kupigana.

2144:2 Za 59:9; 91:2; 18:39; 27:1; 37:39; 43:2; 18:2; Amu 4:23; Mwa 15:1Yeye ni Mungu wangu wa upendo na boma langu,

ngome yangu na mwokozi wangu,

ngao yangu ninayemkimbilia,

ambaye huwatiisha mataifa chini yangu.

3144:3 Ebr 2:6Ee Bwana, mwanadamu ni nini hata umjali,

Binadamu ni nini hata umfikirie?

4144:4 Ay 7:7; 27:3; 14:2; Isa 2:22; 1Nya 29:15; Yak 4:14Mwanadamu ni kama pumzi,

siku zake ni kama kivuli kinachopita.

5144:5 Za 18:9; 57:3; 104:32; Isa 64:1; Mwa 11:5Ee Bwana, pasua mbingu zako, ushuke,

gusa milima ili itoe moshi.

6144:6 Hab 3:11; Zek 9:14; Za 59:11; 68:1; 7:12, 13; 18:14Peleka umeme uwatawanye adui,

lenga mishale yako uwashinde.

7144:7 2Sam 22:17; Za 3:7; 57:3; 69:2; 18:44Nyoosha mkono wako kutoka juu,

nikomboe na kuniokoa

kutoka maji makuu,

kutoka mikononi mwa wageni

8144:8 Za 12:2; 41:6; 26:3; Mwa 14:22; Kum 32:40ambao vinywa vyao vimejaa uongo,

na mikono yao ya kuume ni midanganyifu.

9144:9 Za 28:7; 96:1; 33:2-3; 71:22; 69:1Ee Mungu, nitakuimbia wimbo mpya,

kwa zeze yenye nyuzi kumi nitakuimbia,

10144:10 2Sam 8:14; Za 18:50; Ay 5:20kwa Yule awapaye wafalme ushindi,

ambaye humwokoa Daudi, mtumishi wake kutokana na upanga hatari.

11144:11 Za 3:7; 25:20; 18:44; 41:6-7; 12:2; 36:3; 106:26; Isa 44:20Nikomboe na uniokoe

kutoka mikononi mwa wageni

ambao vinywa vyao vimejaa uongo,

na mikono yao ya kuume ni midanganyifu.

12144:12 Za 92:12-14; 128:3; 4:4; 7:4Kisha wana wetu wakati wa ujana wao

watakuwa kama mimea iliyotunzwa vizuri,

binti zetu watakuwa kama nguzo zilizoviringwa

kurembesha jumba la kifalme.

13144:13 Mit 3:10Ghala zetu zitajazwa

aina zote za mahitaji.

Kondoo zetu watazaa kwa maelfu,

kwa makumi ya maelfu katika mashamba yetu;

14144:14 Mit 14:4; 2Fal 25:11; Isa 24:11; Yer 14:2-3; Law 26:17maksai wetu watakokota

mizigo mizito.

Hakutakuwa na kubomoka kuta,

hakuna kuchukuliwa mateka,

wala kilio cha taabu

katika barabara zetu.

15144:15 Kum 28:3; 33:29Heri watu ambao hili ni kweli;

heri wale ambao Bwana ni Mungu wao.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 144:1-15

Salimo 144

Salimo la Davide.

1Atamandike Yehova Thanthwe langa,

amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;

zala zanga kumenya nkhondo.

2Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa,

linga langa ndi mpulumutsi wanga,

chishango changa mmene ine ndimathawiramo,

amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.

3Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira,

mwana wa munthu kuti muzimuganizira?

4Munthu ali ngati mpweya;

masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.

5Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi;

khudzani mapiri kuti atulutse utsi.

6Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani;

ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.

7Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba;

landitseni ndi kundipulumutsa,

ku madzi amphamvu,

mʼmanja mwa anthu achilendo,

8amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza,

amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

9Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu;

ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,

10kwa Iye amene amapambanitsa mafumu,

amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.

11Landitseni ndi kundipulumutsa,

mʼmanja mwa anthu achilendo,

amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza,

amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

12Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo

adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino,

ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala

zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.

13Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza

ndi zokolola za mtundu uliwonse.

Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda

pa mabusa athu.

14Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera.

Sipadzakhala mingʼalu pa makoma,

sipadzakhalanso kupita ku ukapolo,

mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.

15Odala anthu amene adzalandira madalitso awa;

odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.