Zaburi 107 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Zaburi 107:1-43

KITABU CHA TANO

(Zaburi 107–150)

Zaburi 107

Kumsifu Mungu Kwa Wema Wake

1107:1 1Nya 16:8; 2Nya 5:13; 7:3; Mt 19:17Mshukuruni Bwana, kwa kuwa yeye ni mwema,

upendo wake wadumu milele.

2107:2 Za 106:10; Isa 35:9Waliokombolewa wa Bwana na waseme hivi,

wale aliowaokoa kutoka mkono wa adui,

3107:3 Za 106:47; Isa 49:12; Hes 1:9; Yer 29:14; Eze 39:27wale aliowakusanya kutoka nchi mbalimbali,

kutoka mashariki na magharibi,

kutoka kaskazini na kusini.

4107:4 Yos 5:6; Za 107:36Baadhi yao walitangatanga jangwani,

hawakuona njia ya kuwafikisha mji ambao wangeweza kuishi.

5107:5 Kut 16:3; 15:22; 17:2Walikuwa na njaa na kiu,

nafsi zao zikadhoofika.

6107:6 Kut 14:10; Za 50:15; Isa 41:17; Hos 5:15; Yer 29:12-14Ndipo walipomlilia Bwana katika shida yao,

naye akawaokoa kutoka taabu yao.

7107:7 Ezr 8:21, 36; Isa 38:12Akawaongoza kwa njia iliyo sawa

hadi mji ambao wangeweza kuishi.

8107:8 Za 105:1; 6:4; 75:1Basi na wamshukuru Bwana kwa upendo wake usiokoma,

na kwa matendo yake ya ajabu kwa wanadamu,

9107:9 Za 22:26; 63:5; 23:1; 34:10; Mt 5:6; Yer 31:25; Lk 1:53; Isa 55:1; 58:11kwa maana yeye humtosheleza mwenye kiu,

na kumshibisha mwenye njaa kwa vitu vyema.

10107:10 Za 107:14; 88:6; 143:3; 102:20; Isa 9:2; 42:7, 16; 49:9; 61:1; Mik 7:9; Ay 36:8Wengine walikaa gizani na katika huzuni kuu,

wafungwa wakiteseka katika minyororo,

11107:11 Za 5:10; Hes 14:11; 1Fal 22:5; 2Nya 36:16kwa sababu walikuwa wameasi

dhidi ya maneno ya Mungu

na kudharau shauri

la Aliye Juu Sana.

12107:12 Isa 63:5; Za 72:12; 2Fal 14:26Aliwatumikisha kwa kazi ngumu;

walijikwaa na hapakuwepo yeyote wa kuwasaidia.

13107:13 Za 106:8Ndipo walipomlilia Bwana katika shida yao,

naye akawaokoa kutoka taabu yao.

14107:14 Isa 9:2; 42:7; 59:9; 50:10; 60:2; 29:18; Ay 36:8; Lk 1:79; Za 86:13; 116:16; 146:7; Mdo 12:7Akawatoa katika giza na huzuni kuu

na akavunja minyororo yao.

15107:15 Za 107:8, 21, 31; 105:1; 6:4; 75:1Basi na wamshukuru Bwana kwa upendo wake usiokoma,

na kwa matendo yake ya ajabu kwa wanadamu,

16107:16 Isa 45:2kwa kuwa yeye huvunja malango ya shaba

na kukata mapingo ya chuma.

17107:17 Za 53:1; 25:7; Law 14:1; 26:16; Isa 65:6, 7; Yer 30:14, 15; Gal 6:7, 8; Mt 1:22; Mao 3:39Wengine wakawa wapumbavu kutokana na uasi wao,

wakapata mateso kwa sababu ya uovu wao.

18107:18 Ay 3:24; 6:6; 17:16; 33:22Wakachukia kabisa vyakula vyote,

wakakaribia malango ya mauti.

19107:19 Za 107:13; 5:2; 34:4Ndipo walipomlilia Bwana katika shida yao,

naye akawaokoa kutoka taabu yao.

20107:20 Kum 32:2; Mt 8:8; 2Fal 20:4; Lk 7:7; Kut 15:26; Hes 21:8; Za 30:3; 16:10; 56:13; 147:15; Ay 33:28Akalituma neno lake na kuwaponya,

akawaokoa kutoka maangamizo yao.

21107:21 Za 107:15; 6:4; 75:1Basi na wamshukuru Bwana kwa upendo wake usiokoma,

na kwa matendo yake ya ajabu kwa wanadamu.

22107:22 Law 7:12; Za 9:11; 73:28; 65:8; 50:14; 118:17; Ay 8:21; Ebr 13:15Na watoe dhabihu za kushukuru,

na wasimulie matendo yake kwa nyimbo za furaha.

23107:23 Isa 42:10; Za 104:26Wengine walisafiri baharini kwa meli,

walikuwa wafanyabiashara kwenye maji makuu.

24107:24 Za 64:9; 111:2; 143:5Waliziona kazi za Bwana,

matendo yake ya ajabu kilindini.

25107:25 Za 105:31; 50:3; 93:3Kwa maana alisema na kuamsha tufani

iliyoinua mawimbi juu.

26107:26 Za 22:14; Isa 13:7; Nah 2:10; Lk 8:23; Yos 2:11Yakainuka juu mbinguni, yakashuka chini hadi vilindini,

katika hatari hii ujasiri wao uliyeyuka.

27107:27 Isa 19:14; 24:20; 28:7Walipepesuka na kuyumbayumba kama walevi,

ujanja wao ukafikia ukomo.

28107:28 Za 107:19; 4:1; Yon 1:6Ndipo walipomlilia Bwana katika shida yao,

naye akawatoa kwenye taabu yao.

29107:29 Lk 8:24; Za 93:3; 65:7; Mk 4:39-41; Yon 1:15; Isa 50:2; Mt 8:26Akatuliza dhoruba kwa mnongʼono,

mawimbi ya bahari yakatulia.

30107:30 Za 107:7Walifurahi ilipokuwa shwari,

naye akawaongoza hadi bandari waliyoitamani.

31107:31 Za 107:15; 6:4; 75:1; 106:2Basi na wamshukuru Bwana kwa upendo wake usiokoma,

na kwa matendo yake ya ajabu kwa wanadamu.

32107:32 Za 30:1; 34:3; 99:5; 1:5; 22:22; 26:12; 35:18Na wamtukuze yeye katika kusanyiko la watu,

na wamsifu katika baraza la wazee.

33107:33 1Fal 17:1; Yoe 1:20; Isa 41:15; 42:15; 50:2; 34:9, 10; Eze 30:12; Nah 1:4; Za 74:15; 104:10Yeye aligeuza mito kuwa jangwa,

chemchemi za maji zitiririkazo kuwa ardhi yenye kiu,

34107:34 Mwa 13:10nchi izaayo ikawa ya chumvi isiyofaa,

kwa sababu ya uovu wa wale walioishi humo.

35107:35 2Fal 3:17; Za 105:41; 126:4; Isa 43:19; 51:3; 35:7; Ay 38:26Aligeuza jangwa likawa madimbwi ya maji,

nayo ardhi kame kuwa chemchemi za maji zitiririkazo;

36107:36 Mdo 17:26aliwaleta wenye njaa wakaishi humo,

nao wakajenga mji wangeweza kuishi.

37107:37 2Fal 19:29; Isa 37:30Walilima mashamba na kupanda mizabibu,

nayo ikazaa matunda mengi,

38107:38 Mwa 12:2; 49:25; Kum 7:13Mungu aliwabariki, hesabu yao ikaongezeka sana,

wala hakuruhusu mifugo yao kupungua.

39107:39 2Fal 10:32; Eze 5:12; Za 44:9Kisha hesabu yao ilipungua, na walinyenyekeshwa

kwa kuonewa, maafa na huzuni.

40107:40 Ay 12:18, 21; Kum 32:10Yeye ambaye huwamwagia dharau wakuu,

aliwafanya watangetange nyikani isiyo na njia.

41107:41 1Sam 2:8; 2Sam 7:8; Za 113:7-9; Ay 21:11; 8:7Lakini yeye aliwainua wahitaji katika taabu zao,

na kuongeza jamaa zao kama makundi ya kondoo.

42107:42 Ay 22:19; 5:16; Mit 10:11; Rum 3:19; Za 97:10-12Wanyofu wataona na kufurahi,

lakini waovu wote watafunga vinywa vyao.

43107:43 Yer 9:12; Hos 14:9; Za 103:11; Dan 12:10Yeyote aliye na hekima, ayasikie mambo haya,

na atafakari upendo mkuu wa Bwana.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 107:1-43

BUKU LACHISANU

Masalimo 107–150

Salimo 107

1Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;

pakuti chikondi chake ndi chosatha.

2Owomboledwa a Yehova anene zimenezi

amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,

3iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko,

kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.

4Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu,

osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.

5Iwo anamva njala ndi ludzu,

ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.

6Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo

ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.

7Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka

kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.

8Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,

9pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu

ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.

10Ena anakhala mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu,

amʼndende ovutika mʼmaunyolo achitsulo,

11pakuti iwowo anawukira mawu a Mulungu

ndi kunyoza uphungu wa Wammwambamwamba.

12Kotero Iye anawapereka kuti agwire ntchito yakalavulagaga;

anagwa pansi ndipo panalibe woti awathandize.

13Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo

ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.

14Yehova anawatulutsa mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu

ndipo anadula maunyolo awo.

15Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,

16pakuti Iye amathyola zipata zamkuwa

ndi kudula pakati mipiringidzo yachitsulo.

17Ena anakhala zitsiru chifukwa cha njira zawo zowukira,

ndipo anamva zowawa chifukwa cha mphulupulu zawo.

18Iwo ananyansidwa ndi chakudya chilichonse

ndipo anafika pafupi ndi zipata za imfa.

19Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo

ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awowo.

20Iye anatumiza mawu ake ndi kuwachiritsa;

anawalanditsa ku manda.

21Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.

22Apereke nsembe yachiyamiko

ndi kufotokoza za ntchito zake ndi nyimbo zachimwemwe.

23Ena anayenda pa nyanja mʼsitima zapamadzi;

Iwo anali anthu amalonda pa nyanja yayikulu.

24Anaona ntchito za Yehova,

machitidwe ake odabwitsa mʼnyanja yakuya.

25Pakuti Iye anayankhula ndi kuwutsa mphepo yamkuntho

imene inabweretsa mafunde ataliatali.

26Sitima za pamadzizo zinatukulidwa mmwamba ndi kutsikira pansi pakuya;

pamene amawonongeka, kulimba mtima kwawo kunasungunuka.

27Anachita chizungulire ndi kudzandira ngati anthu oledzera;

anali pa mapeto a moyo wawo.

28Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo

ndipo Iyeyo anawapulumutsa ku masautso awo.

29Yehova analetsa namondwe,

mafunde a mʼnyanja anatontholetsedwa.

30Anali osangalala pamene kunakhala bata,

ndipo Iye anawatsogolera ku dooko limene amalifuna.

31Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.

32Akuze Iye mu msonkhano wa anthu

ndi kumutamanda pabwalo la akuluakulu.

33Iye anasandutsa mitsinje kukhala chipululu,

akasupe otuluka madzi kukhala nthaka yowuma,

34ndiponso nthaka yachonde kukhala nthaka yamchere,

chifukwa cha kuyipa kwa amene amakhala kumeneko.

35Anasandutsa chipululu kukhala mayiwe a madzi

ndi nthaka yowuma kukhala akasupe a madzi oyenda;

36kumeneko Iye anabweretsa anthu anjala kuti azikhalako,

ndipo iwo anamanga mzinda woti akhazikikeko.

37Anafesa mbewu mʼminda ndi kudzala mipesa

ndipo anakolola zipatso zochuluka;

38Yehova anawadalitsa, ndipo chiwerengero chawo chinachuluka kwambiri,

ndipo Iye sanalole kuti ziweto zawo zithe.

39Kenaka chiwerengero chawo chinachepa ndipo iwo anatsitsidwa

chifukwa cha mazunzo, mavuto ndi chisoni;

40Iye amene amakhuthulira mʼnyozo pa olemekezeka

anawachititsa kuyendayenda mʼmalo owumawo wopanda njira.

41Koma Iyeyo anakweza anthu osowa kuchoka ku masautso awo

ngati magulu a nkhosa.

42Anthu olungama mtima amaona ndi kusangalala,

koma anthu onse oyipa amatseka pakamwa pawo.

43Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi

ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.