Yeremia 30 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Yeremia 30:1-24

Kurudishwa Kwa Israeli

1Hili ndilo neno lililomjia Yeremia kutoka kwa Bwana: 230:2 Isa 30:8; Yer 36:2“Hili ndilo asemalo Bwana, Mungu wa Israeli: ‘Andika katika kitabu maneno yote niliyonena na wewe. 330:3 Yer 29:14; 16:15; Amo 9:14; Yer 24:6Siku zinakuja,’ asema Bwana, ‘nitakapowaleta watu wangu Israeli na Yuda kutoka uhamishoni, na kuwarudisha katika nchi niliyowapa baba zao ili kuimiliki,’ asema Bwana.”

4Haya ndiyo maneno Bwana aliyoyanena kuhusu Israeli na Yuda: 530:5 Yer 6:25“Hili ndilo asemalo Bwana:

“ ‘Vilio vya woga vinasikika:

hofu kuu, wala si amani.

630:6 Yer 4:31; Isa 29:22Ulizeni na mkaone:

Je, mwanaume aweza kuzaa watoto?

Kwa nini basi ninaona kila mwanaume mwenye nguvu

ameweka mikono yake tumboni

kama mwanamke aliye na utungu wa kuzaa,

kila uso ukigeuka rangi kabisa?

730:7 Isa 2:12; Amo 5:18; Yoe 2:11; Isa 22:5; Sef 1:15; Yer 23:3Tazama jinsi ile siku itakavyokuwa ya kutisha!

Hakutakuwa na nyingine mfano wake.

Utakuwa wakati wa dhiki kwa Yakobo,

lakini ataokolewa kutoka hiyo.

830:8 Isa 9:4; Yer 25:14; Eze 34:27; Yer 27:7; Za 107:14“ ‘Katika siku ile,’ asema Bwana Mwenye Nguvu Zote,

‘nitaivunja nira kutoka shingoni mwao

na kuvipasua vifungo vyao;

wageni hawatawafanya tena watumwa.

930:9 Isa 55:3-4; 1Sam 13:14; Hos 1:11; 3:5; Yer 33:15; Eze 34:23-24Badala yake, watamtumikia Bwana, Mungu wao

na Daudi mfalme wao,

nitakayemwinua kwa ajili yao.

1030:10 Isa 41:10-13; 43:5; Yer 29:14; Isa 35:9; Yer 17:25; Isa 29:22; Eze 34:25-28“ ‘Hivyo usiogope, ee Yakobo mtumishi wangu,

usifadhaike, ee Israeli,’

asema Bwana.

‘Hakika, nitakuokoa kutoka mbali,

wazao wako kutoka nchi ya uhamisho wao.

Yakobo atakuwa tena na amani na usalama,

wala hakuna atakayemtia hofu.

1130:11 Law 26:44; Yer 4:27; 10:24; Hos 11:9; Amo 9:8; Yer 5:18; Isa 29:22; Eze 34:25-28Mimi niko pamoja nawe, nami nitakuokoa,’

asema Bwana.

‘Ingawa nitayaangamiza kabisa mataifa yote

ambamo miongoni mwao nimewatawanya,

sitawaangamiza ninyi kabisa.

Nitawaadhibu, lakini kwa haki.

Sitawaacha kabisa bila adhabu.’

1230:12 Yer 8:22; 15:18; Ay 6:4; Yer 10:19“Hili ndilo asemalo Bwana:

“ ‘Kidonda chako hakina dawa,

jeraha lako haliponyeki.

1330:13 Nah 3:19; Amu 6:31; Yer 14:19; 8:22; 46:11Hakuna yeyote wa kukutetea shauri lako,

hakuna dawa ya kidonda chako,

wewe hutapona.

1430:14 Yer 22:20; Ay 13:24; 30:21; Yer 25:7; Mao 1:2Wale walioungana nawe wote wamekusahau,

hawajali chochote kukuhusu wewe.

Nimekupiga kama vile adui angelifanya,

na kukuadhibu kama vile mtu mkatili angelifanya,

kwa sababu hatia yako ni kubwa mno

na dhambi zako ni nyingi sana.

1530:15 Yer 10:19; Mit 1:31Kwa nini unalia kwa ajili ya jeraha lako,

yale maumivu yako yasiyoponyeka?

Kwa sababu ya uovu wako mkubwa na dhambi zako nyingi

nimekufanyia mambo haya.

1630:16 Kum 23:22; Yoe 3:4-8; Isa 29:8; Yer 10:25; Isa 14:2; Yer 49:2; 50:10“ ‘Lakini watu wote wakuangamizao wataangamizwa;

adui zako wote watakwenda uhamishoni.

Wale wote wakutekao nyara watatekwa nyara;

wote wakufanyao mateka nitawafanya mateka.

1730:17 Isa 6:12; Yer 33:24; Kut 15:26; Za 142:4Lakini nitakurudishia afya yako

na kuyaponya majeraha yako,’

asema Bwana,

‘kwa sababu umeitwa mwenye kutupwa,

Sayuni ambaye hakuna yeyote anayekujali.’

1830:18 Kum 30:3; Yer 32:44; Za 103:13; Eze 39:25; 36:10; Yer 31:23; Hes 24:5“Hili ndilo asemalo Bwana:

“ ‘Nitarudisha baraka za mahema ya Yakobo,

na kuhurumia maskani yake.

Mji utajengwa tena juu ya magofu yake,

nalo jumba la kifalme litasimama mahali pake halisi.

1930:19 Neh 8:12; Mwa 15:5; Isa 51:3, 11; 60:9; Yer 31:4; Isa 35:10; 44:23; Zek 2:4Nyimbo za kushukuru zitatoka kwao

na sauti ya furaha.

Nitaiongeza idadi yao

wala hawatapungua,

nitawapa heshima

na hawatadharauliwa.

2030:20 Isa 54:13-14; Zek 8:5; Yer 31:17; Kut 23:22Watoto wao watakuwa kama walivyokuwa

siku za zamani,

nayo jumuiya yao itaimarishwa mbele yangu;

nitawaadhibu wale wote wawaoneao.

2130:21 Yer 23:5-6; Hes 16:5; Kum 17:15Mmoja wao atakuwa kiongozi wao;

mtawala wao atainuka miongoni mwao.

Nitamleta karibu nami,

naye atanikaribia mimi,

kwa maana ni nani yule atakayejitolea

kuwa karibu nami?’

asema Bwana.

2230:22 Isa 19:25; Hos 2:23; Law 26:12‘Kwa hiyo ninyi mtakuwa watu wangu,

nami nitakuwa Mungu wenu.’ ”

2330:23 Yer 23:19; 25:32Tazama, tufani ya Bwana

italipuka kwa ghadhabu,

upepo wa kisulisuli uendao kasi

utashuka juu ya vichwa vya waovu.

2430:24 Yer 4:8; Mao 1:12; Yer 4:28; 23:19-20Hasira kali ya Bwana haitarudi nyuma

mpaka atakapotimiza makusudi yote ya moyo wake.

Siku zijazo

mtayaelewa haya.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 30:1-24

Kubwezeretsedwa kwa Israeli

1Yehova anawuza Yeremiya kuti, 2“Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Lemba mʼbuku mawu onse amene ndakuwuza. 3Nthawi ikubwera pamene ndidzachotse anthu anga, Israeli ndi Yuda kuchokera ku ukapolo ndi kuwabwezera dziko limene ndinapatsa makolo awo,’ akutero Yehova.”

4Nawa mawu amene Yehova anayankhula ndi anthu a ku Israeli ndi Yuda: 5“Yehova akuti:

“Ndamva kulira chifukwa cha nkhawa,

ndamva kulira kwa mantha popeza palibe mtendere.

6Tsono khalani pansi ndi kudzifunsa kuti:

Kodi munthu wamwamuna angathe kubereka mwana?

Nanga nʼchifukwa chiyani ndikuona munthu aliyense wamwamuna

atagwira manja ake pa mimba pake ngati mayi pa nthawi yake yochira?

Chifukwa chiyani nkhope iliyonse ili yakugwa?

7Mayo ine! Tsiku limeneli ndi lalikulu kwambiri!

Sipadzakhala lina lofanana nalo.

Idzakhala nthawi ya masautso kwa Yakobo,

koma adzapulumuka ku masautsowo.”

8Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pa tsiku limenelo,

ndidzathyola goli la ukapolo mʼkhosi mwawo

ndipo ndidzadula zingwe zowamanga;

Aisraeli sadzakhalanso akapolo a alendo.

9Mʼmalo mwake, adzatumikira Yehova Mulungu wawo

ndiponso Davide mfumu yawo,

amene ndidzawasankhira.

10“ ‘Tsono usachite mantha, iwe mtumiki wanga Yakobo;

usade nkhawa, iwe Israeli,’

akutero Yehova.

‘Ndithu ndidzakupulumutsa kuchokera ku dziko lakutali,

zidzukulu zako kuchokera ku dziko la ukapolo wawo.

Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala modekha pa mtendere,

ndipo palibe amene adzamuchititsa mantha.

11Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani,’

akutero Yehova.

‘Ngakhale ndidzawononga kotheratu mitundu yonse ya anthu

kumene ndinakubalalitsirani,

koma inu sindidzakuwonongani kotheratu.

Sindidzakulekani kuti mukhale osalangidwa.

Koma ndidzakulangani mwachilungamo.’ ”

12Yehova akuti,

“Chilonda chanu nʼchosachizika,

bala lanu ndi lonyeka.

13Palibe amene angathe kukutetezani pa mlandu wanu,

palibe chiyembekezo choti inu nʼkuchira,

palibe mankhwala ochiritsa inu.

14Abwenzi anu onse akuyiwalani;

sasamalanso za inu.

Ndakukanthani ngati mmene mdani akanachitira.

Ndipo ndakulangani mwa nkhanza,

chifukwa machimo anu ndi ambiri,

ndipo kulakwa kwanu ndi kwakukulu.

15Chifukwa chiyani mukulira nacho chilonda chanu?

Bala lanu silingapole ayi.

Ine ndakuchitani zimenezi chifukwa machimo anu ndi ambiri

ndipo kulakwa kwanu nʼkwakukulu.

16“Tsono onse amene anakuwonongani, nawonso adzawonongedwa;

adani anu onse adzapita ku ukapolo.

Iwo amene anafunkha zinthu zanu, zinthu zawo zidzafunkhidwanso;

onse amene anakusakazani nawonso adzasakazidwa.

17Ndidzachiza matenda anu

ndi kupoletsa zilonda zanu,

akutero Yehova,

‘chifukwa mukutchedwa anthu otayika.

Amati, ndi anthu a ku Ziyoni awa amene alibe wowasamala.’ ”

18Yehova akuti,

“Ndidzabwera nalo banja la Yakobo ku dziko lawo

ndipo ndidzachitira chifundo malo ake okhalamo;

mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso pa bwinja pake,

nyumba yaufumu idzamangidwanso pa malo pake penipeni.

19Anthuwo adzayimba nyimbo zoyamika Yehova

ndipo kudzamveka phokoso lachisangalalo.

Ndidzawachulukitsa,

ndipo chiwerengero chawo sichidzatsika;

ndidzawapatsa ulemerero,

ndipo sadzanyozedwanso.

20Ana awo adzakhalanso monga mmene analili kale,

ndipo gulu lawo ndidzalikhazikitsa pamaso panga;

ndidzalanga onse owazunza.

21Mtsogoleri wawo adzakhala mmodzi mwa iwo.

Wodzawalamulira adzachokera pakati pawo.

Choncho ndidzawakokera kufupi ndi Ine ndipo iye adzandiyandikira.

Ndani angalimbe mtima payekha kuyandikana nane

popanda kuyitanidwa?”

akutero Yehova.

22“Choncho inu mudzakhala anthu anga,

ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu.”

23Taonani ukali wa Yehova wowomba

ngati mphepo ya mkuntho.

Mphepo ya namondwe

ikuwomba pa mitu ya anthu oyipa.

24Mkwiyo woopsa wa Yehova sudzachoka

mpaka atakwaniritsa zolinga

za mu mtima mwake.

Mudzamvetsa zimenezi

masiku akubwerawo.