Yeremia 22 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Yeremia 22:1-30

Hukumu Dhidi Ya Wafalme Waovu

1Hili ndilo asemalo Bwana: “Shuka kwenye jumba la kifalme la mfalme wa Yuda, utangaze ujumbe huu huko: 222:2 Lk 1:32; Amo 7:16‘Sikia neno la Bwana, ee mfalme wa Yuda, wewe uketiye kwenye kiti cha enzi cha Daudi: wewe, maafisa wako na watu wako mnaopitia malango haya. 322:3 Law 25:17; Hos 12:6; Yer 21:12; Za 72:4; Isa 1:17; Amo 5:24; Eze 33:14; Mik 6:8Hili ndilo Bwana asemalo: Tenda haki na adili. Mwokoe mkononi mwa mdhalimu yeye aliyetekwa nyara. Usimtendee mabaya wala ukatili mgeni, yatima au mjane, wala usimwage damu isiyo na hatia mahali hapa. 422:4 Yer 17:25Kwa kuwa ukiwa mwangalifu kushika maagizo haya, ndipo wafalme watakaokalia kiti cha enzi cha Daudi watakapoingia kupitia malango ya jumba hili la kifalme, wakiwa wamepanda magari na farasi, huku wakifuatana na maafisa wao na watu wao. 522:5 Yer 17:25; Mwa 22:16; Ebr 6:13Lakini kama hutayatii maagizo haya, asema Bwana, ninaapa kwa nafsi yangu kwamba jumba hili litakuwa gofu.’ ”

622:6 Mik 3:12; Mwa 31:21; Wim 4:1; Isa 33:9; 1Fal 7:2Kwa kuwa hili ndilo Bwana asemalo kuhusu jumba la kifalme la mfalme wa Yuda:

“Ingawa uko kama Gileadi kwangu,

kama kilele cha Lebanoni,

hakika nitakufanya uwe kama jangwa,

kama miji ambayo haijakaliwa na watu.

722:7 Yer 6:4; Isa 10:34; Za 74:5; Isa 21:14; Yer 4:7; Zek 11:1; 2Nya 36:16Nitawatuma waharabu dhidi yako,

kila mtu akiwa na silaha zake,

nao watazikata boriti zako nzuri za mierezi

na kuzitupa motoni.

822:8 Kum 29:24-26; 1Fal 9:8-9; Yer 16:10-11“Watu kutoka mataifa mengi watapitia karibu na mji huu na kuulizana, ‘Kwa nini Bwana amefanya jambo la namna hii juu ya mji huu mkubwa?’ 922:9 2Fal 22:17; Yer 16:11; Eze 39:23; 1Fal 9:9Nalo jibu litakuwa: ‘Kwa sababu wameliacha agano la Bwana, Mungu wao, na wameabudu na kuitumikia miungu mingine.’ ”

1022:10 Mhu 4:2; Eze 24; 16; Yer 24:9; 29:18; 42:18Usimlilie yeye aliyekufa, wala usimwombolezee;

badala yake, afadhali umlilie kwa uchungu

yule aliyepelekwa uhamishoni,

kwa sababu kamwe hatairudia

wala kuiona tena nchi yake alikozaliwa.

1122:11 2Fal 23:30-31; 1Nya 3:15Kwa kuwa hili ndilo asemalo Bwana kuhusu Shalumu22:11 Shalumu ndiye pia anaitwa Yehoahazi. mwana wa Yosia, aliyeingia mahali pa baba yake kuwa mfalme wa Yuda, lakini ameondoka mahali hapa: “Yeye kamwe hatarudi tena. 1222:12 2Fal 23:34Atafia huko mahali walipompeleka kuwa mateka; hataiona tena nchi hii.”

1322:13 Mik 3:10; Hab 2:9; Law 19:13; Yak 5:4; Isa 5:8“Ole wake yeye ajengaye jumba lake la kifalme kwa njia ya dhuluma,

vyumba vyake vya juu kwa udhalimu,

akiwatumikisha watu wa nchi yake pasipo malipo,

bila kuwalipa kwa utumishi wao.

1422:14 Isa 5:8-9; 2Sam 7:2; Eze 23:14Asema, ‘Nitajijengea jumba kuu la kifalme,

na vyumba vya juu vyenye nafasi kubwa.’

Hivyo anaweka ndani yake madirisha makubwa,

huweka kuta za mbao za mierezi,

na kuipamba kwa rangi nyekundu.

1522:15 2Fal 23:25; Za 22:21; Kum 9:7; Yer 3:13; Sef 3:2; Isa 3:10; Za 128:2“Je, inakufanya kuwa mfalme

huko kuongeza idadi ya mierezi?

Je, baba yako hakuwa na chakula na kinywaji?

Alifanya yaliyo sawa na haki,

hivyo yeye akafanikiwa katika yote.

1622:16 Za 72:1-4, 12-13; Yn 8:19; Tit 1:16; Yak 1:22; Za 82:3; Mit 24:23Aliwatetea maskini na wahitaji,

hivyo yeye akafanikiwa katika yote.

Je, hiyo si ndiyo maana ya kunijua mimi?”

asema Bwana.

1722:17 Eze 19:6; 2Fal 24:4; Isa 56:11; Eze 18:12; Mik 2:2; Kum 28:33“Lakini macho yako na moyo wako vimeelekezwa tu

katika mapato ya udhalimu,

kwa kumwaga damu isiyo na hatia,

kwa uonevu na ukatili.”

18Kwa hiyo hili ndilo asemalo Bwana kuhusu Yehoyakimu mwana wa Yosia mfalme wa Yuda:

“Hawatamwombolezea wakisema:

‘Ole, ndugu yangu! Ole, umbu langu!’

Hawatamwombolezea wakisema:

‘Ole, bwana wangu! Ole, fahari yake!’

1922:19 2Fal 24:6; Yer 36:30Atazikwa maziko ya punda:

ataburutwa na kutupwa

nje ya malango ya Yerusalemu.”

2022:20 Hes 27:12; Isa 57:13; Za 68:15; Yer 30:14; Eze 16:33-34; Hos 8:9“Panda Lebanoni ukapige kelele,

sauti yako na isikike huko Bashani,

piga kelele toka Abarimu,

kwa kuwa wote waliojiunga nawe wameangamizwa.

2122:21 Yer 3:25; 3:13; Sef 3:2; Za 25:7; Zek 7:7; Kum 9:7; Isa 54:4; Yer 7:23-28Nilikuonya wakati ulipojisikia kwamba uko salama,

lakini ulisema, ‘Mimi sitasikiliza!’

Hii imekuwa kawaida yako tangu ujana wako;

hujanitii mimi.

2222:22 Yer 7:19; 10:21; Ay 27:21Upepo utawaondoa wachungaji wako wote,

na wale ulioungana nao wataenda uhamishoni.

Kisha utaaibika na kufedheheka

kwa sababu ya uovu wako wote.

23Wewe uishiye Lebanoni,

wewe uliyetulia kwenye majengo ya mierezi,

tazama jinsi utakavyoomboleza

maumivu makali yatakapokupata,

maumivu kama yale ya mwanamke

mwenye utungu wa kuzaa!

2422:24 2Fal 24:6-8; Yer 37:1; Hag 2:23; Mwa 38:18“Hakika kama niishivyo,” asema Bwana, “hata kama wewe, Yekonia22:24 Yekonia au Konia ni jina jingine la Yehoyakini. mwana wa Yehoyakimu mfalme wa Yuda, ungekuwa pete yangu ya muhuri katika mkono wangu wa kuume, bado ningekungʼoa hapo. 2522:25 2Fal 24:16; 2Nya 36:10; Yer 34:20Nitakutia mikononi mwa wale wanaotafuta uhai wako, wale unaowaogopa, yaani Nebukadneza mfalme wa Babeli na kwa Wakaldayo. 2622:26 1Sam 25:29; Isa 22:17; Eze 19:9-14; 1Fal 2:19; 2Fal 24:8; 2Nya 36:10Nitakutupa mbali wewe na mama aliyekuzaa mwende katika nchi nyingine, ambayo hakuna hata mmoja wenu aliyezaliwa huko, nanyi mtafia huko. 27Kamwe hamtarudi katika nchi mliyotamani kuirudia.”

2822:28 Za 31:12; Hos 8:8; Yer 17:4; 48:38; 2Fal 24:6; Yer 19:10Je, huyu mtu Yekonia ni chungu kilichodharauliwa,

chungu kilichovunjika,

chombo kisichotakiwa na mtu yeyote?

Kwa nini yeye na watoto wake watupwe nje kwa nguvu,

na kutupwa kwenye nchi wasioijua?

2922:29 Yer 6:19Ee nchi, nchi, nchi,

sikia neno la Bwana!

3022:30 1Nya 3:16-18; Mt 1:12; Yer 10:21; 38:23; 52:10; Ay 18:19; Za 94:20Hili ndilo Bwana asemalo:

“Mwandike huyu mtu kama asiye na mtoto,

mtu ambaye hatafanikiwa maisha yake yote,

kwa maana hakuna mtoto wake atakayefanikiwa,

wala kukaa kwenye kiti cha enzi cha Daudi

wala kuendelea kutawala katika Yuda.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 22:1-30

Chiweruzo kwa Mafumu Oyipa

1Yehova anandiwuza kuti, “Pita ku nyumba ya mfumu ya ku Yuda ndipo ukayiwuze kuti, 2‘Imva mawu a Yehova, iwe mfumu ya ku Yuda, amene umakhala pa mpando waufumu wa Davide; iwe, nduna zako pamodzi ndi anthu ako amene amalowera pa zipata izi. 3Yehova akuti, uziweruza molungama ndi mosakondera. Uzipulumutsa munthu amene walandidwa katundu mʼdzanja la womuzunza. Usazunze kapena kupondereza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye. Usaphe munthu wosalakwa pa malo pano. 4Pakuti ngati udzamvera malamulo awa, ndiye kuti mafumu onse okhala pa mpando waufumu wa Davide azidzalowabe pa zipata za nyumba yaufumu ino, atakwera magaleta ndi akavalo, iwowo pamodzi ndi nduna zawo ndi anthu awo. 5Koma ngati sumvera malamulo awa, akutero Yehova, ndikulumbira pali Ine ndemwe kuti nyumba ino yaufumu idzasanduka bwinja.’ ”

6Pakuti zimene Yehova akunena za nyumba yaufumu ya mfumu ya ku Yuda ndi izi:

“Ngakhale iwe uli ngati Giliyadi kwa Ine,

ngati msonga ya phiri la Lebanoni,

komabe ndidzakusandutsa chipululu,

ngati mizinda yopanda anthu.

7Ndidzatuma anthu oti adzakuwononge,

munthu aliyense ali ndi zida zake,

ndipo adzadula mikungudza yako yokongola

nadzayiponya pa moto.

8“Pamene anthu a mitundu ina adzadutsa pa mzinda umenewu adzafunsana kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere pa mzinda waukuluwu?’ 9Ndipo yankho lake lidzakhala lakuti, ‘Chifukwa anasiya pangano limene anapangana ndi Yehova Mulungu wawo ndipo anapembedza ndi kutumikira milungu ina.’ ”

10Musayilire mfumu Yosiya, musamuyimbire nyimbo womwalirayo;

mʼmalo mwake, mulire kwambiri chifukwa cha Yehowahazi amene wapita ku ukapolo,

chifukwa sadzabwereranso

kapena kuonanso dziko lake lobadwira.

11Pakuti zimene Yehova akunena za Yehowahazi mwana wa Yosiya, amene anatenga mpando waufumu wa Yuda mʼmalo mwa abambo ake koma nʼkuwusiya ndi izi: “Iye sadzabwereranso. 12Iyeyo adzafera ku ukapoloko. Sadzalionanso dziko lino.”

13“Tsoka kwa munthu womanga nyumba yake mopanda chilungamo,

womanga zipinda zake zosanja monyenga,

pogwiritsa ntchito abale ake mwathangata,

osawapatsa malipiro a ntchito yawo.

14Munthuyo amati, ‘Ndidzadzimangira nyumba yayikulu

ya zipinda zikuluzikulu zamʼmwamba.’

Kotero ndidzapanga mazenera akuluakulu,

ndi kukhomamo matabwa a mkungudza

ndi kukongoletsa ndi makaka ofiira.

15“Kodi kukhala ndi nyumba ya mkungudza wambiri

zingachititse iwe kukhala mfumu?

Ganiza za abambo ako. Suja anali ndi zonse zakudya ndi zakumwa.

Abambo ako ankaweruza molungama ndi mosakondera,

ndipo zonse zinkawayendera bwino.

16Iye ankateteza anthu osauka ndi osowa,

ndipo zonse zinkamuyendera bwino.

Kodi zimenezi sindiye tanthauzo la kudziwa Ine?”

akutero Yehova.

17“Koma maso ako ndi mtima sizili penanso,

koma zili pa phindu lachinyengo,

pa zopha anthu osalakwa

ndi pa kuzunza ndi pakulamulira mwankhanza.”

18Nʼchifukwa chake Yehova ponena za Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda akuti,

“Anthu sadzamulira maliro kapena kunena kuti,

‘Kalanga ine, mʼbale wanga! Kalanga ine mlongo wanga!

Anthu ake sadzamulira maliro kuti,

Kalanga ine, mbuye wathu! Taonani ulemerero wake wapita!’

19Adzayikidwa ngati bulu,

kuchita kumuguguza ndi kukamutaya

kunja kwa zipata za Yerusalemu.”

20“Tsono inu anthu a ku Yerusalemu, pitani ku mapiri a Lebanoni kuti mukalire mofuwula kumeneko,

mawu anu akamveke mpaka ku Basani.

Mulire mofuwula muli ku Abarimu

chifukwa abwenzi ako onse awonongeka.

21Ndinakuchenjezani pamene munali pa mtendere.

Koma inu munati, ‘Sindidzamvera.’

Umu ndi mmene mwakhala mukuchitira kuyambira mukali aangʼono.

Simunandimvere Ine.

22Mphepo idzakuchotserani abusa anu onse,

ndipo abwenzi anu adzatengedwa ku ukapolo.

Pamenepo mudzachita manyazi ndi kunyozedwa

chifukwa cha zoyipa zanu zonse.

23Inu amene mumakhala mʼnyumba ya ku Lebanoni,

amene munamanga nyumba zanu pakati pa mikungudza,

mudzabuwula kwambiri pamene zowawa zidzakugwerani,

zonga za mkazi pa nthawi yake yochira!

24“Pali Ine wamoyo, akutero Yehova, ngakhale iwe, Yehoyakini mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda, ukanakhala ngati mphete ya ku dzanja langa lamanja, ndikanakuvula nʼkukutaya. 25Ndidzakupereka kwa amene akufuna kukupha, amene iwe umawaopa. Ndidzakupereka kwa Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni ndi anthu ake. 26Iwe pamodzi ndi amayi ako amene anakubereka ndidzakupititsani ku dziko lachilendo. Ngakhale inu simunabadwire kumeneko, komabe mudzafera komweko. 27Simudzabwereranso ku dziko limene mudzafuna kubwerera.”

28Kodi Yehoyakini wakhala ngati mbiya yonyozeka,

yosweka imene anthu sakuyifunanso?

Kodi nʼchifukwa chake iye pamodzi ndi ana ake,

achotsedwa nʼkutayidwa ku dziko limene iwo sakulidziwa?

29Iwe dziko, dziko, dziko,

Imva mawu a Yehova!

30Yehova akuti,

“Munthu ameneyu mumutenge ngati wopanda ana,

munthu amene sadzakhala wochita bwino pamoyo wake wonse,

pakuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa zidzukulu zake zomwe zidzachita bwino.

Palibe amene adzathe kukhala pa mpando waufumu wa Davide

ndi kulamulira Yuda.”