Waebrania 3 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Waebrania 3:1-19

Yesu Ni Mkuu Kuliko Mose

13:1 Ebr 2:11; Rum 8:28; 2:17; 1Tim 6:12; Ebr 4:14; 10:23Kwa hiyo ndugu watakatifu, mnaoshiriki mwito wa mbinguni, mtafakarini Yesu, mtume na Kuhani Mkuu wa ukiri wetu. 23:2 Hes 12:7; Ebr 3:5Alikuwa mwaminifu kwa yeye aliyemweka, kama vile Mose alivyokuwa mwaminifu katika nyumba yote ya Mungu. 33:3 Kum 34:12; Zek 6:12; Mt 16:18Yesu ameonekana anastahili heshima kubwa kuliko Mose, kama vile mjenzi wa nyumba alivyo wa heshima kubwa kuliko nyumba yenyewe. 43:4 Efe 2:10; 3:9; Ebr 1:2; Mwa 1:1Kwa kuwa kila nyumba hujengwa na mtu fulani, lakini Mungu ni mjenzi wa kila kitu. 53:5 Kut 14:31; Ebr 3:2; Hes 12:7; Kum 3:24; 8:15; 18:9; Yos 1:2; 8:31Basi Mose kama mtumishi alikuwa mwaminifu katika nyumba yote ya Mungu, akishuhudia kwa yale ambayo yangetamkwa baadaye. 63:6 Ebr 1:2; 6:11, 18, 19; 7:19; 11:1; 1Kor 3:16; 1Tim 3:15; Rum 11:22; 5:2; Hes 4:14Lakini Kristo ni mwaminifu kama Mwana katika nyumba ya Mungu. Sisi ndio nyumba yake, kama tutashikilia sana ujasiri wetu na tumaini tunalojivunia.

Onyo Dhidi Ya Kutokuamini

73:7 Mdo 28:25; Ebr 9:8; 10:15Kwa hiyo, kama Roho Mtakatifu asemavyo:

“Leo, kama mkiisikia sauti yake,

83:8 Ebr 3:15; 4:7msiifanye mioyo yenu migumu,

kama mlivyofanya katika uasi,

wakati ule wa kujaribiwa jangwani,

93:9 Hes 14:33; Kum 1:3; Mdo 7:36ambapo baba zenu walinijaribu na kunipima

ingawa kwa miaka arobaini

walikuwa wameyaona matendo yangu.

10Hiyo ndiyo sababu nilikasirikia kizazi kile,

nami nikasema, ‘Siku zote mioyo yao imepotoka,

nao hawajazijua njia zangu.’

113:11 Kum 1:34, 35; Ebr 4:3, 5; Za 95:7-11Hivyo nikatangaza kwa kiapo katika hasira yangu,

‘Kamwe hawataingia rahani mwangu.’ ”

123:12 Mt 16:16Ndugu zangu, angalieni, asiwepo miongoni mwenu mtu mwenye moyo mwovu usioamini, unaojitenga na Mungu aliye hai. 133:13 Ebr 10:24, 25; Yer 17:9; Efe 4:22Lakini mtiane moyo mtu na mwenzake kila siku, maadamu iitwapo Leo, ili asiwepo hata mmoja wenu mwenye kufanywa mgumu kwa udanganyifu wa dhambi. 143:14 Efe 3:12; Ebr 3:6Kwa kuwa tumekuwa washiriki wa Kristo, kama tukishikamana tu kwa uthabiti na tumaini letu la kwanza hadi mwisho. 153:15 Za 95:7, 8; Ebr 4:7; 3:7, 8Kama ilivyonenwa:

“Leo, kama mkiisikia sauti yake,

msiifanye mioyo yenu migumu

kama mlivyofanya wakati wa kuasi.”

16Basi ni nani waliosikia lakini bado wakaasi? Je, si wale wote waliotoka Misri wakiongozwa na Mose? 17Lakini ni nani aliowakasirikia miaka arobaini? Je, si wale waliofanya dhambi ambao miili yao ilianguka jangwani? 18Ni nani hao ambao Mungu aliapa kuwa kamwe hawataingia rahani mwake isipokuwa ni wale waliokataa kutii? 19Hivyo tunaona kwamba hawakuweza kuingia kwa sababu ya kutokuamini kwao.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 3:1-19

Yesu ndi Wamkulu Kuposa Mose

1Nʼchifukwa chake abale oyera mtima, amenenso munayitanidwa ndi kumwamba, lingalirani za Yesu amene ndi Mtumwi ndi Mkulu wa ansembe wa chikhulupiriro chimene timavomereza. 2Iye anali wokhulupirika kwa Mulungu amene anamupatsa udindowo, monga momwe Mose anali wokhulupirika mʼnyumba yonse ya Mulungu. 3Yesu anapezeka woyenera kulandira ulemu waukulu kuposa Mose, monga momwemonso womanga nyumba amalandira ulemu waukulu kuposa nyumbayo. 4Pakuti nyumba iliyonse imamangidwa ndi munthu wina, koma amene anapanga zonse ndi Mulungu. 5Mose anali wokhulupirika monga mtumiki mʼnyumba yonse ya Mulungu, kuchitira umboni zimene zidzayankhulidwe mʼtsogolo. 6Koma Khristu ndi wokhulupirika monga mwana pa nyumba ya Mulungu. Ndipo ndife nyumba yake ngati tipitirire kulimbika mtima ndi kunyadira zomwe tikuyembekerazo.

Chenjezo pa Kusakhulupirira

7Tsono monga Mzimu Woyera akuti,

“Lero mukamva mawu ake,

8musawumitse mitima yanu

ngati munachitira pamene munawukira,

pa nthawi yoyesedwa mʼchipululu.

9Pamene makolo anu anandiputa ndi kundiyesa,

ndipo kwa zaka makumi anayi anaona zimene Ine ndinachita.

10Nʼchifukwa chake ndinawukwiyira mʼbadowo,

ndipo Ine ndinati, ‘Nthawi zonse mitima yawo imasochera,

ndipo iwo sadziwa njira zanga.’

11Kotero Ine ndinalumbira nditakwiya kuti,

‘Iwo sadzalowa mu mpumulo wanga.’ ”

12Abale samalani, kuti pasapezeke wina aliyense mwa inu wokhala ndi mtima woyipa ndi wosakhulupirira, womulekanitsa ndi Mulungu wamoyo. 13Koma muzilimbikitsana tsiku ndi tsiku, ikanalipo nthawi imene imatchedwa kuti “Lero” kuti aliyense wa inu mtima wake usawumitsidwe ndi chinyengo cha tchimo. 14Pakuti timakhala anzake a Khristu, ngati tigwiritsitsa mpaka potsiriza chitsimikizo chimene tinali nacho pachiyambi. 15Monga kunanenedwa kuti,

“Lero ngati mumva mawu ake,

musawumitse mitima yanu

ngati momwe munachitira pamene munawukira.”

16Nanga amene anamva ndi kuwukira anali ndani? Kodi si onse amene Mose anawatulutsa mu Igupto? 17Nanga amene Mulungu anawakwiyira zaka makumi anayi anali ndani? Kodi si anthu amene anachimwa, amene mitembo yawo inatsala mʼchipululu muja? 18Nanga Mulungu ankanena za ndani kuti sadzalowa mu mpumulo wake? Pajatu ankanena za anthu amene sanamvere aja. 19Tsono ife tikuona kuti sanalowe chifukwa cha kusakhulupirika kwawo.