Mithali 21 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Mithali 21:1-31

121:1 Es 5:1; Yer 39:11-12Moyo wa mfalme uko katika mkono wa Bwana;

huuongoza kama mkondo wa maji, popote apendapo.

221:2 Mit 24:12; Lk 16:15; Yer 17:10; 1Sam 16:7Njia zote za mwanadamu huonekana sawa kwake,

bali Bwana huupima moyo.

321:3 Hos 6:6; Mik 6:6-8Kufanya yaliyo sawa na haki inakubalika

zaidi kwa Bwana kuliko dhabihu.

421:4 Ay 41:34; Mit 6:17Macho ya kudharau na moyo wa kiburi,

ambavyo ni taa ya waovu, vyote ni dhambi!

521:5 Mit 10:4Mipango ya mwenye bidii huelekeza kwenye faida,

kama vile kwa hakika pupa huelekeza kwenye umaskini.

621:6 Mit 10:2; 2Pet 2:3Mali iliyopatikana kwa ulimi wa uongo

ni mvuke upitao upesi na mtego wa kufisha.

721:7 Mit 11:5Jeuri ya waovu itawaburuta mbali,

kwa kuwa wanakataa kufanya yaliyo sawa.

821:8 Mit 2:15Njia ya mwenye hatia ni ya upotovu,

bali tabia ya mtu asiye na hatia ni nyofu.

921:9 Mit 21:19; 19:13; 25:24Ni afadhali kuishi pembeni mwa paa la nyumba,

kuliko kuishi nyumba moja na mke mgomvi.

1021:10 Yak 4:5Mtu mwovu hutamani sana ubaya,

jirani yake hapati huruma kutoka kwake.

1121:11 Mit 19:25Wakati mwenye mzaha ameadhibiwa,

mjinga hupata hekima;

wakati mtu mwenye hekima afundishwapo,

hupata maarifa.

1221:12 1Kor 10:10; Rum 2:8; Mit 14:11Mwenye Haki huyajua yanayotendeka katika nyumba za waovu,

naye atawaangamiza waovu.

1321:13 Ay 29:12; Zek 7:11; Mdo 7:57; Yak 2:13Mtu akiziba masikio asisikie kilio cha maskini,

yeye pia atalia, wala hatajibiwa.

1421:14 Mwa 32:20; Mit 18:16Zawadi itolewayo kwa siri hutuliza hasira

na rushwa iliyofichwa kwenye nguo hutuliza ghadhabu kali.

1521:15 Mit 21:9Wakati haki imetendeka, huleta furaha kwa wenye haki,

bali kitisho kwa watenda mabaya.

1621:16 Za 49:14; Eze 18:24Mtu anayepotea kutoka mapito ya ufahamu,

hupumzika katika kundi la waliokufa.

1721:17 Mit 23:20-21, 29-35Mtu apendaye anasa atakuwa maskini,

yeyote apendaye mvinyo na mafuta kamwe hatakuwa tajiri.

1821:18 Isa 43:3-4; Mit 11:8Waovu huwa fidia kwa ajili ya wenye haki,

nao wasio waaminifu kwa ajili ya wanyofu.

1921:19 Mit 21:9Ni afadhali kuishi jangwani

kuliko kuishi na mke mgomvi na mkorofi.

2021:20 Za 112:3; Mit 10:22; Mt 25:3Katika nyumba ya mwenye hekima

kuna akiba ya vyakula vizuri na mafuta,

lakini mtu mpumbavu

hutafuna vyote alivyo navyo.

2121:21 1Kor 15:58; Za 25:13; Mt 5:6Yeye afuatiaye haki na upendo

hupata uzima, mafanikio na heshima.

2221:22 Mit 8:14; Mhu 9:15-16Mtu mwenye hekima huushambulia mji wa wenye nguvu,

na kuangusha ngome wanazozitegemea.

2321:23 Za 34:13; Yak 3:2; Mit 12:13Yeye alindaye kinywa chake na ulimi wake

hujilinda na maafa.

2421:24 Yer 43:2Mtu mwenye kiburi na majivuno, “Mdhihaki” ndilo jina lake;

hutenda mambo kwa kiburi kilichozidi.

2521:25 Mit 13:4Kutamani sana kwa mvivu kutakuwa kifo chake,

kwa sababu mikono yake haitaki kufanya kazi.

2621:26 Law 25:35; Mt 5:42Mchana kutwa hutamani zaidi,

lakini mnyofu hutoa pasipo kuzuia.

2721:27 1Fal 14:24; Amo 5:22; Mit 15:8Dhabihu ya mtu mwovu ni chukizo,

si zaidi sana itolewapo kwa nia mbaya!

2821:28 Isa 29:21; Mit 19:5Shahidi wa uongo ataangamia,

bali maneno ya mwenye kusikia yatadumu.

2921:29 Mit 14:8Mtu mwovu ana uso wa ushupavu,

bali mtu mnyofu huzifikiria njia zake.

3021:30 Ay 12:13; Yer 9:23; 2Nya 13:12; Mdo 5:39Hakuna hekima, wala akili, wala mpango

unaoweza kufaulu dhidi ya Bwana.

3121:31 Isa 31:1; Za 3:8Farasi huandaliwa kwa ajili ya siku ya vita,

bali ushindi huwa kwa Bwana.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 21:1-31

1Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova;

Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.

2Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo,

koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.

3Za chilungamo ndi zolondola

ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.

4Maso odzikuza ndi mtima wonyada,

zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.

5Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake;

koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.

6Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa

ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.

7Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga,

pakuti iwo amakana kuchita zolungama.

8Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota,

koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.

9Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba,

kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.

10Munthu woyipa amalakalaka zoyipa;

sachitira chifundo mnansi wake wovutika.

11Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru;

koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.

12Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova,

ndipo Iye adzawononga woyipayo.

13Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira,

nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.

14Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo,

ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.

15Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala,

koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.

16Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru

adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.

17Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi,

ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.

18Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama

ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.

19Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu

kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.

20Munthu wanzeru samwaza chuma chake,

koma wopusa amachiwononga.

21Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika,

amapeza moyo ndi ulemerero.

22Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu

ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.

23Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake

sapeza mavuto.

24Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,”

iye amachita zinthu modzitama kwambiri.

25Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha

chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.

26Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri,

koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.

27Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova,

nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!

28Mboni yonama idzawonongeka,

koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.

29Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima,

koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.

30Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu,

zimene zingapambane Yehova.

31Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo,

koma ndi Yehova amene amapambanitsa.