Mithali 11 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Mithali 11:1-31

111:1 Law 19:36; Ay 6:2; Mit 16:11; Eze 45:10Bwana huchukia sana mizani za udanganyifu,

bali vipimo sahihi ni furaha yake.

211:2 Dan 4:30; Mit 16:18; 18:12Kiburi kinapokuja, ndipo huja aibu,

bali unyenyekevu huja na hekima.

311:3 Mit 13:6Uadilifu wa wenye haki huwaongoza,

bali wasio waaminifu huharibiwa na hila yao.

411:4 Ay 20:20; Eze 7:19; Sef 1:18Utajiri haufaidi kitu katika siku ya ghadhabu,

bali haki huokoa kutoka mautini.

511:5 1Fal 8:36; Mit 5:21-23; 13:6; 21:7Haki ya wasio na lawama, huwatengenezea njia iliyonyooka,

bali waovu huangushwa kwa uovu wao wenyewe.

611:6 Es 7:9; 1Tim 4:8; Mhu 10:8Haki ya wanyofu huwaokoa,

bali wasio waaminifu hunaswa na tamaa mbaya.

711:7 Ay 8:13; Mit 10:28Wakati mtu mwovu anapokufa, matumaini yake hutoweka;

yote aliyoyatazamia kutokana na nguvu zake huwa si kitu.

811:8 Mit 21:8Mtu mwenye haki huokolewa kutoka taabu,

naye mtu mwovu huingia humo badala yake.

911:9 Mit 12:6; Yer 45:5; Ay 8:13Kwa kinywa chake mtu asiyemwamini Mungu

humwangamiza jirani yake,

bali kwa maarifa mwenye haki huokolewa.

1011:10 2Fal 11:20; Mit 28:12; Es 8:15Wakati mwenye haki anapofanikiwa, mji hufurahi;

mwovu atowekapo, kuna kelele za furaha.

1111:11 Mit 14:34; 29:8Kutokana na baraka ya mtu mnyofu mji hukwezwa,

bali kwa kinywa cha mwovu mji huharibiwa.

1211:12 Mit 14:21; Ay 6:24Mtu asiye na akili humdharau jirani yake,

bali mtu mwenye ufahamu huuzuia ulimi wake.

1311:13 Law 19:16; 1Tim 5:13; Mit 20:19; 10:14Masengenyo husaliti tumaini,

bali mtu mwaminifu hutunza siri.

1411:14 Mit 20:18; 24:6; 2Sam 15:34; 1Fal 12:1; Mit 20:18; 2Sam 15:34; Mit 15:22; 24:6; 1Fal 12:1Pasipo ushauri wa hekima taifa huanguka,

bali washauri wengi hufanya ushindi uwe wa hakika.

1511:15 Mit 6:1; 17:18; 22:26-27Yeye amdhaminiye mgeni hakika atateseka,

bali yeyote akataaye kuunga mkono dhamana ni salama.

1611:16 Mit 31:31Mwanamke mwenye moyo wa huruma hupata heshima,

bali wanaume wakorofi hupata mali tu.

1711:17 Mt 25:34Mwenye huruma hujinufaisha mwenyewe,

bali mkatili hujiletea taabu mwenyewe.

1811:18 Hos 10:12; Kut 1:20; Ay 4:8Mtu mwovu hupata ujira wa udanganyifu,

bali yeye apandaye haki huvuna tuzo ya uhakika.

1911:19 Kum 30:15; Mit 10:2; 1Sam 2:6; Za 89:48; Mit 1:18-19; Mhu 7:2; Yer 43:1Mtu mwenye haki kweli kweli hupata uzima,

bali yeye afuatiliaye ubaya huendea kifo chake.

2011:20 1Nya 29:17; Za 52:7Bwana huwachukia sana watu wenye moyo wa upotovu,

bali hupendezwa na wale ambao njia zao hazina lawama.

2111:21 Mit 16:5; Za 112:2Uwe na hakika na hili: Waovu hawataepuka kuadhibiwa,

bali wenye haki watakuwa huru.

22Kama pete ya dhahabu katika pua ya nguruwe

ndivyo alivyo mwanamke mzuri ambaye hana busara.

2311:23 Rum 2:8, 9Shauku ya mwenye haki huishia tu kwenye mema,

bali tumaini la mwovu huishia tu kwenye ghadhabu.

2411:24 Za 112:9Kuna mtu atoaye kwa ukarimu, hata hivyo hupata zaidi,

mwingine huzuia, lakini huwa maskini.

2511:25 Mit 22:9; 2Kor 9:6-9; Mt 5:7Mtu mkarimu atastawi;

yeye awaburudishaye wengine

ataburudishwa mwenyewe.

2611:26 Amo 8:5; Ay 29:13Watu humlaani mtu awanyimae watu nafaka,

bali baraka itamkalia kichwani kama taji

yeye aliye radhi kuiuza.

2711:27 Es 7:10; Za 7:15-16Yeye atafutaye mema hupata ukarimu,

bali ubaya huja kwake yeye autafutaye.

2811:28 Yer 9:23; 17:8; Mk 10:25; Za 52:8Yeyote ategemeaye utajiri wake ataanguka,

bali mwenye haki atastawi kama jani bichi.

2911:29 Mhu 5:16; Mit 14:19Yeye aletaye taabu kwa jamaa yake atarithi tu upepo,

naye mpumbavu atakuwa mtumishi wa wenye hekima.

3011:30 Mwa 2:9; Yak 5:20Tunda la mwenye haki ni mti wa uzima,

naye mwenye hekima huvuta roho za watu.

3111:31 Yer 25:29; 49:12; 1Pet 4:18Kama wenye haki watapokea ujira wao duniani,

si zaidi sana yule asiyemcha Mungu na mwenye dhambi?

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 11:1-31

1Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa,

koma amakondwera ndi muyeso woyenera.

2Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi,

koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.

3Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera,

koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.

4Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu,

koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.

5Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo,

koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.

6Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa,

koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.

7Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso.

Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.

8Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto,

koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.

9Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake,

koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.

10Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera,

ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.

11Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima,

koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.

12Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru,

koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.

13Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi;

koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.

14Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa;

koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.

15Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto,

koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.

16Mkazi wodekha amalandira ulemu,

koma amuna ankhanza amangopata chuma.

17Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino

koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.

18Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu,

koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.

19Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo,

koma wothamangira zoyipa adzafa.

20Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota

koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.

21Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa,

koma anthu olungama adzapulumuka.

22Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba,

ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.

23Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha,

koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.

24Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe;

wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.

25Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera;

iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.

26Anthu amatemberera womana anzake chakudya,

koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.

27Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo,

koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.

28Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota,

koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.

29Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto,

ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.

30Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo,

ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.

31Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi,

kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!