Mhubiri 12 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Mhubiri 12:1-14

112:1 2Sam 19:35; Mhu 11:8Mkumbuke Muumba wako

siku za ujana wako,

kabla hazijaja siku za taabu,

wala haijakaribia miaka utakaposema,

“Mimi sifurahii hiyo”:

2kabla jua na nuru,

nao mwezi na nyota havijatiwa giza,

kabla ya kurudi mawingu baada ya mvua;

312:3 Mwa 27:1; Zek 8:4; Za 71:9siku ile walinzi wa nyumba watakapotetemeka,

nao watu wenye nguvu watakapojiinamisha,

wakati wasagao watakapokoma kwa sababu ya uchache,

nao wachunguliao madirishani kutiwa giza;

412:4 Yer 25:10; Mik 7:1wakati milango ya kuingia barabarani itakapofungwa

na sauti ya kusaga kufifia;

wakati watu wataamshwa kwa sauti ya ndege,

lakini nyimbo zao zote zikififia;

512:5 Ay 10:21; 17:13; Yer 9:17; Amo 5:16wakati watu watakapoogopa kilichoinuka juu

na hatari zitakazokuwepo barabarani;

wakati mlozi utakapochanua maua

na panzi kujikokota

nawe usiwe na shauku ya kitu chochote.

Ndipo mwanadamu aiendea nyumba yake ya milele

nao waombolezaji wakizunguka barabarani.

6Mkumbuke Muumba wako: kabla haijakatika kamba ya fedha,

au bakuli la dhahabu halijavunjika;

kabla mtungi kuvunjika kwenye chemchemi,

au gurudumu kuvunjika kisimani,

712:7 Mwa 2:7; Ay 20:8; 34:15; Mhu 3:21; Za 146:4nayo mavumbi kurudi ardhini yalikotoka,

na roho kurudi kwa Mungu aliyeitoa.

8Mhubiri asema, “Ubatili! Ubatili!

Kila kitu ni ubatili!”

Hitimisho La Mambo

912:9 1Fal 4:32Mhubiri hakuwa tu na hekima, bali aliwagawia watu maarifa pia. Alitafakari na kutafiti na akaweka katika utaratibu mithali nyingi. 1012:10 Mit 22:20-21Mhubiri alitafiti ili kupata maneno sahihi na kila alichoandika kilikuwa sawa na kweli.

1112:11 Ezr 9:8; Ay 6:25Maneno ya wenye hekima ni kama mchokoro, mithali zao zilizokusanywa pamoja ni kama misumari iliyogongomewa ikawa imara, yaliyotolewa na Mchungaji mmoja. 12Tena zaidi ya hayo, mwanangu, kubali maonyo, hakuna mwisho wa kutunga vitabu vingi, nako kusoma sana huuchosha mwili.

1312:13 Mik 6:8; Kum 4:2-6; 10:12; Kut 20:20; 1Sam 12:24; Ay 23:15; Za 19:9Hii ndiyo jumla ya maneno;

yote yamekwisha sikiwa:

Mche Mungu, nawe uzishike amri zake,

maana kwa jumla ndiyo impasayo mtu.

1412:14 Mt 10:26; Ay 19:26; 34:21; Mhu 3:17; Za 19:12; Yer 16:17Kwa maana Mungu ataleta hukumuni kila kazi,

pamoja na kila neno la siri,

likiwa jema au baya.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 12:1-14

1Uzikumbukira mlengi wako

masiku a unyamata wako,

masiku oyipa asanafike,

nthawi isanafike pamene udzanena kuti,

“Izi sizikundikondweretsa.”

2Nthawi ya ukalamba wako, dzuwa ndi kuwala,

mwezi ndi nyenyezi zidzada.

Mitambo idzabweranso mvula itagwa.

3Nthawi imene manja ako adzanjenjemera,

miyendo yako idzafowoka,

pamene mano ako adzalephera kutafuna chifukwa ndi owerengeka,

ndipo maso ako adzayamba kuchita chidima.

4Makutu ako adzatsekeka,

ndipo sudzamva phokoso lakunja;

sudzamvanso kusinja kwa pa mtondo

kapena kulira kwa mbalame mmawa.

5Imeneyi ndiyo nthawi imene anthu amaopa kupita kumalo okwera,

amaopa kuyenda mʼmisewu;

Mutu umatuwa kuti mbuu,

amayenda modzikoka ngati ziwala

ndipo chilakolako chimatheratu.

Nthawi imeneyo munthu amapita ku nyumba yake yamuyaya

ndipo anthu olira maliro amayendayenda mʼmisewu.

6Kumbukira Iye chingwe cha siliva chisanaduke,

kapena mbale yagolide isanasweke;

mtsuko usanasweke ku kasupe,

kapena mkombero usanathyoke ku chitsime.

7Iyi ndi nthawi imene thupi lidzabwerera ku dothi, kumene linachokera,

mzimu udzabwerera kwa Mulungu amene anawupereka.

8“Zopanda phindu! Zopandapake!” akutero Mlaliki.

“Zonse ndi zopandapake!”

Mawu Otsiriza

9Mlaliki sanali wozindikira zinthu kokha ayi, komanso ankaphunzitsa anthu. Iye ankasinkhasinkha ndi kufufuzafufuza ndi kulemba mwadongosolo miyambi yambiri. 10Mlaliki anafufuzafufuza kuti apeze mawu oyenera, ndipo zimene analemba zinali zolondola ndiponso zoona.

11Mawu a anthu anzeru ali ngati zisonga, zokamba zawo zimene anasonkhanitsa zili ngati misomali yokhomera, yoperekedwa ndi mʼbusa mmodzi. 12Samalira mwana wanga, za kuwonjezera chilichonse pa zimenezi.

Kulemba mabuku ambiri sikutha, ndipo kuphunzira kwambiri kumatopetsa thupi.

13Basi zonse zamveka; mathero a nkhaniyi ndi awa:

uziopa Mulungu ndi kusunga malamulo ake,

pakuti umenewu ndiwo udindo

wa anthu onse.

14Pakuti Mulungu adzaweruza zochita zonse,

kuphatikizanso zinthu zonse zobisika,

kaya zabwino kapena zoyipa.