Ayubu 1 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Ayubu 1:1-22

Sehemu Ya Kwanza: Habari Za Awali

(Ayubu 1–2)

Ayubu Na Jamaa Yake

11:1 Mwa 22:21; Yak 5:11; Eze 14:14, 20; Mit 8:13; Mwa 10:23; 6:9; 22:12; Ay 23:7, 10; 2:3; Za 11:7; 107:42; Mit 21:29; Mik 7:2; Kum 4:6; 1The 5:22Katika nchi ya Usi paliishi mtu ambaye aliitwa Ayubu. Mtu huyu alikuwa hana hatia, naye alikuwa mkamilifu; alimcha Mungu na kuepukana na uovu. 21:2 Za 127:3; Rut 4:15; Ay 1:13, 18; 42:13; Za 144:12Alikuwa na wana saba na binti watatu, 31:3 Ay 29:25; Mwa 13:2; 12:16; Ay 1:8; Mwa 25:6; Ay 42:10; Za 103:10naye alikuwa na kondoo elfu saba, ngamia elfu tatu, jozi mia tano za maksai, na punda mia tano, tena alikuwa na idadi kubwa ya watumishi. Alikuwa mtu mkuu sana miongoni mwa watu wa Mashariki.

41:4 Ay 1:13, 18Wanawe walikuwa na desturi ya kufanya karamu katika nyumba zao kwa zamu, nao wangewaalika umbu zao watatu ili kula na kunywa pamoja nao. 51:5 Mwa 8:20; Ay 42:8; 1Fal 21:10-13; Za 74:10; Neh 12:30; Ay 8:4; Za 10:3Wakati kipindi cha karamu kilimalizika, Ayubu angetuma waitwe na kuwafanyia utakaso. Angetoa dhabihu ya sadaka ya kuteketezwa kwa ajili ya kila mmoja wao asubuhi na mapema, akifikiri, “Pengine wanangu wametenda dhambi na kumlaani Mungu mioyoni mwao.” Hii ilikuwa ndiyo desturi ya kawaida ya Ayubu.

Jaribu La Kwanza La Ayubu

61:6 1Fal 22:19; Ay 38:7; 2:1; Dan 7:10; Mwa 6:2; 2Sam 24:1; 2Nya 18:21; Za 109:6; Lk 22:31Siku moja wana wa Mungu1:6 Wana wa Mungu hapa ina maana malaika au viumbe vya mbinguni. walikwenda kujionyesha mbele za Bwana. Shetani1:6 Shetani hapa ina maana ya mshtaki wa watakatifu. naye akaja pamoja nao. 71:7 Mwa 3:1; 1Pet 5:8; Mt 12:43Bwana akamwambia Shetani, “Umetoka wapi?”

Shetani akamjibu Bwana, “Natoka kuzunguka pote duniani, nikitembea huku na huko humo.”

81:8 Ay 42:7-8; Kut 20:20; Yos 1:7; Za 25:16; 26:12; 112:1; 128:4Ndipo Bwana akamwambia Shetani, “Je, umemwangalia huyo mtumishi wangu Ayubu? Hakuna mtu mwingine duniani aliye kama yeye, asiye na hatia, ni mnyofu, mwenye kumcha Mungu, na kuepukana na uovu.”

91:9 1Tim 6:5Shetani akamjibu Bwana, “Je, Ayubu anamcha Mungu bure? 101:10 Za 34:7; 128:1-2; Ay 8:7; 1Sam 25:16; Ay 2:4; 29:6; 42:12, 17Je, wewe hukumjengea boma pande zote yeye na wa nyumbani mwake pamoja na kila kitu alicho nacho? Kazi za mikono yake umezibariki na hivyo makundi yake ya kondoo na mbuzi pamoja na ya wanyama yameenea katika nchi nzima. 111:11 Ay 19:21; Law 24:11; Ufu 12:9-10; Lk 22:31; Isa 3:8; 65:3; Ay 2:5Lakini nyoosha mkono wako na kupiga kila kitu alicho nacho, naye kwa hakika atakulaani mbele za uso wako.”

121:12 Ay 2:6; 1Kor 10:13Bwana akamwambia Shetani, “Vema sana, kwa hiyo, kila kitu alicho nacho kiko mikononi mwako, lakini juu ya huyo mtu mwenyewe usimguse hata kwa kidole.”

Ndipo Shetani akatoka mbele za Bwana.

131:13 Ay 1:2, 4; Mhu 9:12; Lk 12:19, 20Siku moja watoto wa Ayubu walipokuwa wakifanya karamu wakila na kunywa divai katika nyumba ya ndugu yao mkubwa, 141:14 Mwa 36:24akaja mjumbe kwa Ayubu na kusema, “Maksai walikuwa wakilima na punda walikuwa wakilisha karibu nao, 151:15 Mwa 10:7; Ay 6:19; 9:26Waseba wakawashambulia na kuchukua mifugo. Kisha wakawaua watumishi kwa upanga, nami ndimi peke yangu niliyenusurika kukuletea habari!”

161:16 1Fal 18:38; 2Fal 1:12; Ay 20:26; Mwa 18:17; Law 10:2; Hes 11:1-3Alipokuwa bado ananena, mjumbe mwingine akaja na kusema, “Moto wa Mungu ulishuka kutoka mbinguni na kuteketeza kondoo na watumishi, nami ndimi peke yangu niliyenusurika kukuletea habari!”

171:17 Mwa 11:28-31; Ay 9:24Alipokuwa bado ananena, mjumbe mwingine akaja na kusema, “Wakaldayo waliunda vikosi vitatu vya uvamizi na kuwaangukia ngamia wako na kuwachukua wakaondoka nao. Wakawaua watumishi kwa upanga, nami ndimi peke yangu niliyenusurika kukuletea habari.”

181:18 Ay 1:2, 4Alipokuwa bado ananena, mjumbe mwingine akaja na kusema, “Wana wako na binti zako walipokuwa wakifanya karamu, wakila na kunywa divai katika nyumba ya ndugu yao mkubwa, 191:19 Isa 21:1; Mk 7:25; Za 11:6; Isa 5:28; Yer 4:11; 13:24; 18:17; Eze 17:10; Hos 13:15ghafula upepo wenye nguvu ukavuma kutoka jangwani, nao ukaipiga nyumba hiyo pembe zake nne. Ikawaangukia hao watoto nao wamekufa, nami ndimi peke yangu niliyenusurika kukuletea habari!”

201:20 Mwa 37:29; Mk 14:63; Isa 3:24; 15:2; 22:12; Yer 7:29; 16:6; Eze 27:31; 29:18; Mik 1:16; 1Pet 5:6Ndipo Ayubu akasimama, akararua joho lake na kunyoa nywele zake. Kisha akaanguka chini katika kuabudu 211:21 Mhu 5:15; Rut 1:21; Amu 10:15; Efe 5:20; Mwa 45:5; 1Tim 6:7; 1Sam 2:7; Mhu 7:14; Yak 5:11; Amo 3:6; Efe 5:20; Mwa 45:5na kusema:

“Nilitoka tumboni mwa mama yangu uchi,

nami nitaondoka uchi,1:21 Au: nitarudi huko uchi.

Bwana alinipa, naye Bwana ameviondoa,

jina la Bwana litukuzwe.”

221:22 Mit 10:19; Rum 9:20; Ay 2:10; Za 39:1; Isa 53:7Katika mambo haya yote, Ayubu hakutenda dhambi kwa kumlaumu Mungu kwa kufanya ubaya.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 1:1-22

Mawu Oyamba

1Mʼdziko la Uzi munali munthu wina, dzina lake Yobu. Munthu ameneyu anali wosalakwa ndi wolungama mtima, ankaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa. 2Anali ndi ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu, 3ndipo anali ndi nkhosa 7,000, ngamira 3,000, ngʼombe zantchito 1,000 ndi abulu aakazi 500, ndiponso anali ndi antchito ambiri. Iye anali munthu wotchuka kwambiri pakati pa anthu onse a mʼmayiko a kummawa.

4Ana ake aamuna ankachita phwando mosinthanasinthana mʼnyumba zawo, ndipo ankayitana alongo awo atatu aja kudzadya ndi kumwa nawo. 5Masiku aphwandowo atatha, Yobu ankawayitana kuti adzawayeretse. Mmamawa iye ankapereka nsembe yopsereza kuperekera mwana aliyense, poganiza kuti, “Mwina ana anga achimwa ndi kutukwana Mulungu mʼmitima yawo.” Umu ndi mmene Yobu ankachitira nthawi zonse.

Yobu Ayesedwa Koyamba

6Ana a Mulungu atabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anafika nawo limodzi. 7Yehova anati kwa Satanayo, “Kodi iwe ukuchokera kuti?”

Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”

8Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.”

9Satana anayankha kuti, “Kodi Yobu amaopa Mulungu popanda chifukwa?” 10“Kodi Inu simumamuteteza iyeyo, nyumba yake ndi zonse zimene ali nazo? Mwadalitsa ntchito ya manja ake, kotero kuti nkhosa ndi ngʼombe zake zili ponseponse mʼdzikomo. 11Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kukantha zonse ali nazo ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”

12Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, tsono zonse zimene ali nazo ndaziyika mʼmanja mwako, koma iye yekhayo usamukhudze.”

Pamenepo Satana anachoka pamaso pa Yehova.

13Tsiku lina pamene ana aamuna ndi ana aakazi a Yobu ankachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba mwa mkulu wawo, 14wamthenga anabwera kwa Yobu ndipo anati, “Ngʼombe zanu zotipula ndipo abulu anu amadya chapafupi pomwepo, 15tsono panabwera Aseba kudzatithira nkhondo ndi kutenga zonse. Apha antchito ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”

16Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Kunagwa mphenzi ndipo yapsereza nkhosa ndi antchito anu onse, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”

17Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Akasidi anadzigawa mʼmagulu atatu ankhondo ndipo anafika pa ngamira zanu ndi kuzitenga. Apha antchito anu onse ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”

18Iyeyo akuyankhulabe, panafikanso wamthenga wina nati, “Ana anu aamuna ndi aakazi amachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba ya mkulu wawo, 19mwadzidzidzi chinayamba chimphepo champhamvu chochokera ku chipululu, nʼkudzawomba nyumba mbali zonse zinayi. Nyumbayo yawagwera ndipo afa, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”

20Atamva zimenezi, Yobu anayimirira nangʼamba mkanjo wake, ndi kumeta tsitsi lake. Kenaka anadzigwetsa pansi napembedza Mulungu, 21nati,

“Ndinatuluka maliseche mʼmimba mwa amayi anga,

namonso mʼmanda ndidzalowa wamaliseche.

Yehova ndiye anapereka ndipo Yehova watenga;

litamandike dzina la Yehova.”

22Mu zonsezi, Yobu sanachimwe kapena kunena kuti, “Mulungu walakwa.”