ኢዮብ 32 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢዮብ 32:1-22

ኤሊሁ

1ኢዮብ በበኩሉ ራሱን እንደ ጻድቅ ቈጥሮ ስለ ነበር፣ እነዚህ ሦስት ሰዎች ለእርሱ መልስ መስጠታቸውን ተዉ። 2ከራም ወገን የሆነው፣ የቡዛዊው የባርክኤል ልጅ ኤሊሁ ግን ኢዮብ ከእግዚአብሔር ይልቅ ራሱን ጻድቅ ስላደረገ እጅግ ተቈጣው። 3ሦስቱ የኢዮብ ጓደኞች በኢዮብ ላይ መፍረድ32፥3 የማሶሬቱ ቅጅ ከዚህ ጋር ይስማማል፤ ጥንታዊው የዕብራውያን ጸሐፍት ትውፊት ግን ኢዮብንም ሆነ እግዚአብሔርን ኰነኑ ይላል። እንጂ፣ ነገሩን ሊያሳምኑት ስላልቻሉ፣ በእነርሱም ላይ ተቈጣ። 4ኤሊሁ፣ ሌሎቹ በዕድሜ ይበልጡት ስለ ነበር ከእነርሱ ቀድሞ ለኢዮብ ሳይናገር ቈየ። 5ነገር ግን እነዚህ ሦስቱ የሚሉትን ባጡ ጊዜ ቍጣው ነደደ።

6ስለዚህ የቡዛዊው የባርክኤል ልጅ ኤሊሁ እንዲህ አለ፤

“እኔ በዕድሜ ታናሽ ነኝ፤

እናንተ ግን አዛውንቶች ናችሁ፤

ከዚህም የተነሣ የማውቀውን ለመናገር አልደፈርሁም፤

ፈርቼ ዝም አልሁ።

7‘ዕድሜ ይናገራል፤

ረዥም ዘመን ጥበብን ያስተምራል’ ብዬ ነበር።

8ነገር ግን በሰው ያለው መንፈስ፣

ሁሉን የሚችል አምላክ እስትንፋስ፣

ማስተዋልን ይሰጣል።

9ጠቢባን የሚሆኑት በዕድሜ የገፉ32፥9 ወይም፣ ብዙ ወይም፣ ታላቅ ብቻ አይደሉም፤

የሚያስተውሉም ሽማግሌዎች ብቻ አይደሉም።

10“ስለዚህ፣ ‘ስሙኝ፣

እኔም የማውቀውን ልንገራችሁ’ እላለሁ።

11እናንተ በምትነጋገሩበት ጊዜ ታገሥሁ፤

ቃላት እየመረጣችሁ ስትናገሩ፣

በጥሞና ሰማኋችሁ፤

12በሙሉ ልብ አደመጥኋችሁ፤

ነገር ግን ከእናንተ የኢዮብን ቃል ያስተባበለ ማንም የለም፤

ለንግግሩም አጸፋ የመለሰ አልተገኘም።

13‘እኛ ጥበብ አግኝተናል፤

ሰው ሳይሆን እግዚአብሔር ይርታው’ አትበሉ።

14ኢዮብ ግን ቃሉን በእኔ ላይ አልሰነዘረም፤

እኔም እንደ እናንተ አነጋገር መልስ አልሰጠውም።

15“እነርሱ ተስፋ ቈርጠው የሚሉት የላቸውም፤

የሚናገሩትም ጠፍቷቸዋል።

16እንግዲህ እነርሱ መልስ ስላጡ፣

ጸጥ ብለውም ስለ ቆሙ፣ በትዕግሥት ልጠብቅን?

17እኔም የምለው ይኖረኛል፤

የማውቀውንም እገልጣለሁ።

18የምናገረው ሞልቶኛልና፤

በውስጤ ያለውም መንፈስ ገፋፍቶኛል።

19ውስጤ እንደ ተከደነና መተንፈሻ እንዳጣ የወይን ጠጅ፣

ሊፈነዳ እንደ ተቃረበም አዲስ የወይን ጠጅ አቁማዳ ሆኗል።

20ተናግሬ መተንፈስ አለብኝ፤

አፌንም ከፍቼ መልስ መስጠት ይገባኛል።

21ለማንም አላደላም፤

ሰውንም አላቈላምጥም።

22ማቈላመጥን ባውቅበትማ ኖሮ፣

ፈጣሪዬ ፈጥኖ ባጠፋኝ ነበር።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 32:1-22

Mawu a Elihu

1Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama. 2Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga. 3Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa. 4Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo. 5Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.

6Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati:

“Ine ndine wamngʼono,

inuyo ndinu akuluakulu,

nʼchifukwa chake ndimaopa,

ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.

7Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula;

anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’

8Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu,

mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.

9Si okalamba amene ali ndi nzeru,

si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.

10“Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni;

inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’

11Ndadikira nthawi yonseyi,

ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula,

pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,

12ineyo ndinakumvetseranidi.

Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu;

palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.

13Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru;

Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’

14Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine,

ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.

15“Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso;

mawu awathera.

16Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano,

pakuti angoyima phee wopanda yankho?

17Inenso ndiyankhulapo tsopano;

nanenso ndinena zimene ndikudziwa.

18Pakuti ndili nawo mawu ambiri,

ndipo mtima wanga ukundikakamiza;

19mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo,

ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.

20Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike;

ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.

21Sindidzakondera munthu wina aliyense,

kapena kuyankhula zoshashalika,

22pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika,

Mlengi wanga akanandilanga msanga.”