ኢዩኤል 3 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢዩኤል 3:1-21

የተፈረደባቸው ሕዝቦች

1“በዚያ ዘመን፣ በዚያ ጊዜ፣

የይሁዳንና የኢየሩሳሌምን ምርኮ ስመልስ፣

2አሕዛብን ሁሉ እሰበስባለሁ፤

ወደ ኢዮሣፍጥም3፥2 ኢዮሣፍጥ፣ የስሙ ትርጕም እግዚአብሔር ይፈርዳል ማለት ነው፤ 12 ላይም እንዲሁ፤ ሸለቆ አወርዳቸዋለሁ፤

ስለ ርስቴ፣ ስለ ሕዝቤ፣ ስለ እስራኤል፣

በዚያ ልፈርድባቸው እገባለሁ፤

ምድሬን ከፋፍለዋል፤

ሕዝቤንም በሕዝቦች መካከል በታትነዋልና።

3በሕዝቤ ላይ ዕጣ ተጣጣሉ፤

ወንዶች ልጆችን በዝሙት ዐዳሪዎች ለወጡ፤

ወይን ጠጅ ለመጠጣትም፣

ሴቶች ልጆችን ሸጡ።

4“ጢሮስና ሲዶና እንዲሁም እናንተ የፍልስጥኤም ግዛቶች ሁሉ ሆይ፤ እንግዲህ በእኔ ላይ ምን አላችሁ? ስላደረግሁት ነገር ብድር ልትመልሱልኝ ነውን? የምትመልሱልኝ ከሆነ፣ በፍጥነትና በችኰላ እናንተ ያደረጋችሁትን በራሳችሁ ላይ መልሼ አደርግባችኋለሁ። 5ብሬንና ወርቄን ወስዳችኋል፤ የተመረጠውንም ንብረቴን ተሸክማችሁ ወደ ቤተ መቅደሳችሁ አስገብታችኋልና። 6ከገዛ ምድራቸው ልታርቋቸው፣ የይሁዳንና የኢየሩሳሌምን ሰዎች ለግሪኮች ሸጣችኋቸው።

7“እነሆ፤ እነርሱን ከሸጣችሁባቸው ቦታዎች አነሣሣቸዋለሁ፤ እናንተም ያደረጋችሁትን በገዛ ራሳችሁ ላይ እመልስባችኋለሁ። 8ወንዶችንና ሴቶች ልጆቻችሁን ለይሁዳ ሰዎች ሸጣለሁ፤ እነርሱም መልሰው በሩቅ ላሉት ለሳባ ሰዎች ይሸጧቸዋል፤” እግዚአብሔር ይህን ተናግሯልና።

9በሕዝቦች መካከል ይህን ዐውጁ፤

ለጦርነት ተዘጋጁ፤

ተዋጊዎችን አነሣሡ፤

ጦረኞችም ሁሉ ቀርበው ያጥቁ።

10ማረሻችሁ ሰይፍ፣

ማጭዳችሁም ጦር እንዲሆን ቀጥቅጡት፤

ደካማውም ሰው፣

“እኔ ብርቱ ነኝ” ይበል።

11እናንት በዙሪያ ያላችሁ ሕዝቦች ሁላችሁ፤

ፈጥናችሁ ኑ፤ በዚያም ተሰብሰቡ።

እግዚአብሔር ሆይ፤ ተዋጊዎችህን ወደዚያ አውርድ!

12“ሕዝቦች ይነሡ፤

ወደ ኢዮሣፍጥም ሸለቆ ፈጥነው ይውረዱ፤

ዙሪያውን ባሉት ሕዝቦች ሁሉ ላይ ልፈርድ፣

በዚያ እቀመጣለሁና።

13ማጭዱን ስደዱ፤

መከሩ ደርሷልና፤

ኑ ወይኑን ርገጡ፤

የወይን መጭመቂያው ሞልቶ፣

ከጕድጓዶቹም ተርፎ ፈስሷልና፤

ክፋታቸው እንደዚህ ታላቅ ነው።”

14ብዙ ሕዝብ፣ በጣም ብዙ ሕዝብ፣

ፍርድ በሚሰጥበት ሸለቆ ተሰብስቧል፤

ፍርድ በሚሰጥበት ሸለቆ፣

የእግዚአብሔር ቀን ቀርቧልና።

15ፀሓይና ጨረቃ ይጨልማሉ፤

ከዋክብትም ከእንግዲህ አያበሩም።

16እግዚአብሔር ከጽዮን ጮኾ ይናገራል፤

ከኢየሩሳሌም ያንጐደጕዳል፤

ሰማይና ምድርም ይናወጣሉ፤

እግዚአብሔር ግን ለሕዝቡ መሸሸጊያ፣

ለእስራኤልም ልጆች መጠጊያ ይሆናል።

በረከት ለእግዚአብሔር ሕዝብ

17“ከዚያም እኔ አምላካችሁ እግዚአብሔር

በቅዱሱ ተራራዬ በጽዮን እንደምኖር ታውቃላችሁ፤

ኢየሩሳሌም የተቀደሰች ትሆናለች፤

ከእንግዲህም ወዲያ ባዕዳን አይወርሯትም።

18“በዚያ ጊዜ ተራሮች፣ አዲስ የወይን ጠጅ ያንጠባጥባሉ፤

ኰረብቶችም ወተት ያፈስሳሉ፤

በይሁዳ ያሉ ሸለቆዎች3፥18 ወይም የሸጢም ሸለቆ ሁሉ ውሃ ያጐርፋሉ፤

ከእግዚአብሔር ቤት ምንጭ ይፈልቃል፤

የሰጢምን ሸለቆ ያጠጣል።

19ግብፅ ባድማ፣

ኤዶምም ምድረ በዳ ትሆናለች፤

በምድራቸው ንጹሕ ደም በማፍሰስ፣

በይሁዳ ሕዝብ ላይ ግፍ ፈጽመዋልና።

20ይሁዳ ለዘላለም፣

ኢየሩሳሌምም ለትውልድ ሁሉ መኖሪያ ትሆናለች፤

21ደማቸውን እበቀላለሁ፤

በደለኛውንም ንጹሕ አላደርግም።”

እግዚአብሔር በጽዮን ይኖራል!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoweli 3:1-21

Kuweruzidwa kwa Mitundu ya Anthu

1“Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo,

nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,

2ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse

ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati.

Kumeneko ndidzawaweruza

chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli,

pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu

ndikugawa dziko langa.

3Anagawana anthu anga pochita maere

ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere;

anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo

kuti iwo amwe.

4“Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu. 5Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano. 6Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.

7“Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu. 8Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.

9Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina:

Konzekerani nkhondo!

Dzutsani ankhondo amphamvu!

Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.

10Sulani makasu anu kuti akhale malupanga

ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo.

Munthu wofowoka anene kuti,

“Ndine wamphamvu!”

11Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse,

ndipo musonkhane kumeneko.

Tumizani ankhondo anu Yehova!

12“Mitundu ya anthu idzuke;

ipite ku Chigwa cha Yehosafati,

pakuti kumeneko Ine ndidzakhala

ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.

13Tengani chikwakwa chodulira tirigu,

pakuti mbewu zakhwima.

Bwerani dzapondeni mphesa,

pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza

ndipo mitsuko ikusefukira;

kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”

14Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu,

mʼchigwa cha chiweruzo!

Pakuti tsiku la Yehova layandikira

mʼchigwa cha chiweruzo.

15Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa,

ndipo nyenyezi sizidzawalanso.

16Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni

ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu;

dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka.

Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake,

linga la anthu a ku Israeli.

Madalitso a Anthu a Mulungu

17“Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu,

ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika.

Yerusalemu adzakhala wopatulika;

alendo sadzamuthiranso nkhondo.

18“Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano,

ndipo zitunda zidzayenderera mkaka;

mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi.

Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova

ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.

19Koma Igupto adzasanduka bwinja,

Edomu adzasanduka chipululu,

chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda

mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.

20Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya

ndi Yerusalemu ku mibadomibado.

21Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke

ndidzakhululuka.”

Yehova amakhala mu Ziyoni!