ኢሳይያስ 9 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢሳይያስ 9:1-21

ሕፃን ተወለደልን

1ነገር ግን ተጨንቀው የነበሩ ከእንግዲህ ተስፋ ቢስ አይሆኑም። በቀደመው ዘመን የዛብሎንንና የንፍታሌምን ምድር አዋረደ፤ በሚመጣው ዘመን ግን ከዮርዳኖስ ማዶ፣ በባሕር መንገድ አጠገብ ያለውን የአሕዛብን ገሊላ ያከብራል፤

2በጨለማ የሚኖር ሕዝብ

ታላቅ ብርሃን አየ፤

በሞት ጥላ9፥2 ወይም፣ በጨለማ ምድር። ምድር ለኖሩትም

ብርሃን ወጣላቸው።

3ሕዝብን አበዛህ፤

ደስታቸውንም ጨመርህ፤

ሰዎች ምርትን ሲሰበስቡ፣

ምርኮንም ሲከፋፈሉ

ደስ እንደሚላቸው ሁሉ፣

እነርሱም በፊትህ ደስ ይላቸዋል።

4ምድያም ድል በተመታ ጊዜ እንደ ሆነው፣

የከበዳቸውን ቀንበር፣

በትከሻቸው ላይ የነበረውን በትር፣

የተጨቈኑበትንም ዘንግ ሰብረህላቸዋል።

5የጦረኞች ጫማ ሁሉ፣

በደም የተለወሰ ልብስም ሁሉ፣

ለእሳት ይዳረጋል፤

ይማገዳልም።

6ሕፃን ተወልዶልናል፤

ወንድ ልጅም ተሰጥቶናል፤

አለቅነትም በጫንቃው ላይ ይሆናል።

ስሙም፣ ድንቅ መካር፣9፥6 ወይም፣ ድንቅ፣ መካር።

ኀያል አምላክ፣

የዘላለም አባት፣ የሰላም ልዑል ይባላል።

7ለመንግሥቱ ስፋት፣

ለሰላሙም ብዛት ፍጻሜ የለውም፤

ከአሁን ጀምሮ እስከ ዘላለም፣

መንግሥቱን በፍትሕና በጽድቅ ይመሠርታል፤

ደግፎ በመያዝም ያጸናዋል።

በዳዊት ዙፋን ይቀመጣል፤

አገሩንም ሁሉ ይገዛል፤

የሰራዊት ጌታ እግዚአብሔር ቅናት

ይህን ያደርጋል።

የእግዚአብሔር ቍጣ በእስራኤል ላይ

8ጌታ በያዕቆብ ላይ ቃል ላከ፤

በእስራኤልም ላይ ይወድቃል።

9ሕዝቡ በሙሉ፣

ኤፍሬምና የሰማርያ ነዋሪዎች

ይህን ያውቃሉ፤

በትዕቢትና በልብ እብሪትም እንዲህ ይላሉ፤

10“ጡቦቹ ወድቀዋል፤

እኛ ግን በጥርብ ድንጋይ መልሰን እንገነባለን፤

የሾላ ዛፎቹ ተቈርጠዋል፤

እኛ ግን በዝግባ እንተካለን።”

11ነገር ግን እግዚአብሔር የረአሶንን ጠላቶች ያጠናክራል፤

በእነርሱም ላይ ያመጣባቸዋል፤

ባለጋራዎቻቸውንም ያነሣሣባቸዋል።

12ሶርያውያን ከምሥራቅ፣ ፍልስጥኤማውያን ከምዕራብ፤

አፋቸውን ከፍተው እስራኤልን ይቦጫጭቋታል።

ይህም ሁሉ ሆኖ፣ ቍጣው ገና አልበረደም፤

እጁ እንደ ተዘረጋ ነው።

13ሕዝቡ ግን ወደ ቀጣቸው ፊታቸውን አልመለሱም፤

የሰራዊት ጌታ እግዚአብሔርንም አልፈለጉም።

14ስለዚህ እግዚአብሔር ራስንና ጅራትን፣

የዘንባባውን ቅርንጫፍና ሸንበቆውን ከእስራኤል በአንድ ቀን ይቈርጣል።

15ሽማግሌዎችና የተከበሩ ሰዎች ራስ፣

ሐሰትን የሚያስተምሩ ነቢያት ደግሞ ጅራት ናቸው።

16ይህን ሕዝብ የሚመሩት ያስቱታል፤

የሚመራውም ሕዝብ ከመንገድ ወጥቶ ይባዝናል።

17ስለዚህ ጌታ በጐበዛዝት ደስ አይሰኝም፤

አባት ለሌላቸውና ለመበለቶች አይራራም፤ ሁሉም ፈሪሀ እግዚአብሔር ያላደረበትና ክፉ አድራጊ ነው፤

የሁሉ አፍ አስጸያፊ ቃል ይናገራልና።

ይህም ሁሉ ሆኖ፣ ቍጣው ገና አልበረደም፤

እጁም እንደ ተዘረጋ ነው።

18እንግዲህ ርኩሰት እንደ እሳት ይቀጣጠላል፤

እሾኽንና ኵርንችትን ይበላል፤

ጥቅጥቅ ያለውን ደን ያነድዳል፤

ጢሱም ተትጐልጕሎ እንደ ዐምድ ይቆማል።

19በሰራዊት ጌታ በእግዚአብሔር ቍጣ ምድር ትጋያለች፤

ሕዝቡም እሳት ውስጥ እንደሚጨመር

ማገዶ ይሆናል፤

ወንድሙንም ማዳን የሚችል ማንም የለም።

20በቀኝ በኩል ይጐርሳሉ፤

ነገር ግን ራባቸው አይታገሥም፤

በግራም በኩል ይበላሉ፤

ነገር ግን አይጠግቡም፤

እያንዳንዱም የገዛ ወገኑን9፥20 ወይም፣ ክንዱን ሥጋ ይበላል።

21ምናሴ ኤፍሬምን፣ ኤፍሬም ምናሴን ይበላል፤

በይሁዳም ላይ በአንድነት ይነሣሉ፤

ይህም ሁሉ ሆኖ፣ ቍጣው ገና አልበረደም፤

እጁም እንደ ተዘረጋ ነው።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 9:1-21

Ufumu wa Mesiya

1Anthu amene anali ndi nkhawa, sadzakhalanso otaya mtima. Masiku amakedzana Mulungu ananyozetsa dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafutali, koma kutsogolo kuno dera lonse la Galileya, limene lili dziko la anthu a mitundu ina, kuyambira ku nyanja yayikulu, mʼmbali mwa Yorodani, adzalisandutsa laulemu.

2Anthu oyenda mu mdima

awona kuwala kwakukulu;

kwa iwo okhala mʼdziko la mdima wandiweyani

kuwunika kwawafikira.

3Inu mwauchulukitsa mtundu wanu

ndipo mwawonjezera chimwemwe chawo.

Iwo akukondwa pamaso panu,

ngati mmene anthu amakondwera nthawi yokolola,

ngatinso mmene anthu amakondwera

pamene akugawana zolanda ku nkhondo.

4Monga munachitira pogonjetsa Amidiyani,

inu mwathyola goli

limene limawalemera,

ndodo zimene amamenyera mapewa awo,

ndiponso mikwapulo ya anthu owazunza.

5Nsapato iliyonse ya munthu wankhondo,

ndiponso chovala chilichonse chodonthekera magazi

zidzatenthedwa pa moto

ngati nkhuni.

6Chifukwa mwana watibadwira,

mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife,

ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake.

Ndipo adzamutcha dzina lake lakuti

Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu,

Atate Amuyaya, ndi Mfumu ya Mtendere.

7Ulamuliro ndi mtendere wake

zidzakhala zopanda malire.

Iye adzalamulira ufumu wake ali pa

mpando waufumu wa Davide,

ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza

mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo

kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya.

Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse

watsimikiza kuchita zimenezi.

Mkwiyo wa Yehova pa Israeli

8Ambuye atumiza mawu otsutsa Yakobo;

ndipo mawuwo agwera pa Israeli.

9Anthu onse okhala mu

Efereimu ndi okhala mu Samariya,

adzadziwa zimenezi.

Iwo amayankhula modzikuza kuti,

10“Ngakhale njerwa zagumuka,

koma ife tidzamanga ndi miyala yosema.

Mitanda ya mkuyu yagwetsedwa,

koma ife tidzayika mitanda ya mkungudza mʼmalo mwake.”

11Koma Yehova wadzutsa adani kuti alimbane nawo

ndipo wawafulumiza adani awo kuti amenyane nawo.

12Asiriya ochokera kummawa ndi Afilisti ochokera kumadzulo ndipo

ayasama pakamwa kuti adye a Israeli.

Komabe, mkwiyo wake sunawachokere,

mkono wake uli chitambasulire.

13Koma anthu sanabwerere kwa amene anawakantha uja,

ngakhale kufunafuna Yehova Wamphamvuzonse.

14Choncho Yehova adzadula mutu wa Israeli pamodzi ndi mchira womwe,

nthambi ya kanjedza ndi bango lomwe tsiku limodzi;

15mutuwo ndiye akuluakulu ndi olemekezeka,

mchira ndiye aneneri ophunzitsa zabodza.

16Amene amatsogolera anthuwa ndiwo amawasocheretsa,

ndipo otsogoleredwa amatayika.

17Nʼchifukwa chake Ambuye adzakondwera nawo achinyamata,

ngakhale kuwachitira chifundo ana amasiye ndi akazi amasiye,

pakuti aliyense ndi wosapembedza Mulungu ndiponso ndi wochimwa ndipo

aliyense amayankhula zopusa.

Komabe, mkwiyo wake sunawachokere,

mkono wake uli chitambasulire.

18Ndithu kuyipa kwa anthuwo kumayaka ngati moto;

moto wake umanyeketsa mkandankhuku ndi minga,

umayatsa nkhalango yowirira,

ndipo utsi wake umachita kuti toloo ngati mtambo.

19Dziko lidzatenthedwa ndi ukali wa Yehova Wamphamvuzonse,

dziko lidzatenthedwa

ndipo anthu adzakhala ngati nkhuni zosonkhera moto;

palibe munthu amene adzachitire chifundo mʼbale wake.

20Kudzanja lamanja adzapeza chakudya nʼkudya,

koma adzakhalabe ndi njala;

kudzanja lamanzere adzapeza chakudya nʼkudya,

koma sadzakhuta.

Aliyense azidzadya ana ake omwe.

21Manase adzadya Efereimu ndipo Efereimu adzadya Manase;

onsewa pamodzi adzadya Yuda.

Komabe pa zonsezi, mkwiyo wake sunawachokere,

mkono wake uli chitambasulire.