ኢሳይያስ 45 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢሳይያስ 45:1-25

1“ለቀባሁት፣ ቀኝ እጁን ለያዝሁት፣

ነገሥታትን ትጥቅ አስፈታ ዘንድ፣

ሕዝብን ሁሉ ላስገዛለት፣

ደጆች እንዳይዘጉ፣

በሮቹን በፊቱ ለምከፍትለት፣

ለቂሮስ እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤

2‘በፊትህ እሄዳለሁ፤

ተራሮችን45፥2 የሙት ባሕር ጥቅሎችና የሰብዓ ሊቃናት ትርጕም ከዚህ ጋር ይስማማል፤ በማሶሬቱ ቅጅ ግን የቃሉ ትርጕም አይታወቅም። እደለድላለሁ፤

የናስ በሮችን እሰብራለሁ፤

የብረት መወርወሪያዎችንም እቈርጣለሁ።

3በስምህ የምጠራህ የእስራኤል አምላክ፣

እኔ እግዚአብሔር መሆኔን ታውቅ ዘንድ፣

በተሰወረ ስፍራ የተከማቸውን ሀብት፣

በጨለማም ያለውን ንብረት እሰጥሃለሁ።

4ስለ ባሪያዬ ስለ ያዕቆብ፣

ስለ መረጥሁት ስለ እስራኤል፣

አንተ ባታውቀኝ እንኳ፣

በስምህ ጠርቼሃለሁ፤

የክብርም ስም ሰጥቼሃለሁ።

5እኔ እግዚአብሔር ነኝ፤ ከእኔ ሌላ ማንም የለም፤

ከእኔ በቀር አምላክ የለም።

አንተ ባታውቀኝም እንኳ፣

እኔ አበረታሃለሁ።

6ይኸውም ሰዎች ከፀሓይ መውጫ፣

እስከ መጥለቂያው፣

ከእኔ በቀር ሌላ እንደሌለ እንዲያውቁ ነው፤

እኔ እግዚአብሔር ነኝ፤ ከእኔ ሌላ ማንም የለም።

7እኔ ብርሃንን ሠራሁ፤ ጨለማንም ፈጠርሁ፤

አበለጽጋለሁ፤ አደኸያለሁ፤

ይህን ሁሉ የማደርግ እኔ እግዚአብሔር ነኝ።’

8“እናንት ሰማያት፣ ጽድቅን ከላይ አዝንቡ፤

ደመናትም ወደ ታች አንጠብጥቡ፤

ምድር ትከፈት፤

ድነት ይብቀል፤

ጽድቅም አብሮት ይደግ፤

እኔ እግዚአብሔር ፈጥሬዋለሁ።

9“ከዐፈር ሸክላዎች መካከል፣

ከሠሪው ጋር ክርክር ለሚገጥም ወዮለት፤

ጭቃ፣ ሸክላ ሠሪውን፣

‘ምን እየሠራህ ነው?’ ይለዋልን?

የምትሠራውስ ሥራ፣

‘እጅ የለህም’ ይልሃልን?

10አባቱን፣

‘የወለድኸው ምንድን ነው?’ ለሚል፣

እናቱንም፣

‘ምን ወለድሽ’? ለሚል ወዮለት።

11“የእስራኤል ቅዱስ፣ ሠሪውም የሆነ እግዚአብሔር

ስለሚመጡ ነገሮች እንዲህ ይላል፤

‘ስለ ልጆቼ ትጠይቁኛላችሁን?

ስለ እጆቼስ ሥራ ታዝዙኛላችሁን?

12ምድርን የሠራሁ እኔ ነኝ፤

ሰውንም በላይዋ ፈጥሬአለሁ፤

እጆቼ ሰማያትን ዘርግተዋል፤

የሰማይንም ሰራዊት አሰማርቻለሁ።

13ቂሮስን45፥13 ዕብራይስጡ፣ እርሱን ይላል። በጽድቅ አስነሥቻለሁ፤

መንገዱን ሁሉ አስተካክዬለታለሁ፤

ከተማዬን እንደ ገና ይሠራታል፤

ምርኮኞቼን ያለ ክፍያ ወይም ያለ ዋጋ፣

ነጻ ያወጣል፤’

ይላል የሰራዊት ጌታ እግዚአብሔር።”

14እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤

“የግብፅ ሀብትና የኢትዮጵያ ንግድ፣

ቁመተ ረዣዥሞቹ የሳባ ሰዎች፣

ወደ አንተ ይመጣሉ፤

የአንተ ይሆናሉ፤

ከኋላ ይከተሉሃል፤

በሰንሰለትም ታስረው ወደ አንተ በመምጣት፣

በፊትህ እየሰገዱ፣

‘በእውነት እግዚአብሔር ከአንተ ጋር ነው፤

ከእርሱም በቀር ሌላ አምላክ የለም’ ብለው ይለምኑሃል።”

15አዳኙ የእስራኤል አምላክ ሆይ፤

አንተ በእውነት ራስህን የምትሰውር አምላክ ነህ።

16ጣዖት ሠሪዎች ሁሉ ያፍራሉ፤ ይቀልላሉ፤

በአንድነት ይዋረዳሉ።

17እስራኤል ግን በእግዚአብሔር

በዘላለም ድነት ይድናል፤

እናንተም ለዘላለም፣

አታፍሩም፤ አትዋረዱም።

18ሰማያትን የፈጠረ፣

እርሱ እግዚአብሔር ነው፤

ምድርን ያበጃት፣ የሠራት፣

የመሠረታት፣

የሰው መኖሪያ እንጂ፣

ባዶ እንድትሆን ያልፈጠራት፣

እግዚአብሔር እንዲህ ይላልና፤

“እኔ እግዚአብሔር ነኝ፤

ከእኔም በቀር ሌላ የለም።

19በጨለማ ምድር፣

በምስጢር አልተናገርሁም፤

ለያዕቆብም ዘር፣

‘በከንቱ ፈልጉኝ’ አላልሁም።

እኔ እግዚአብሔር እውነትን እናገራለሁ፤

ትክክለኛውንም ነገር ዐውጃለሁ።

20“በአንድነት ተሰብሰቡ፤ ቅረቡም፤

እናንት ከአሕዛብ የኰበለላችሁ፣ ኑ።

የዕንጨት ጣዖት የሚሸከሙ፣

ማዳን ወደማይችል አምላክ የሚጸልዩ፣ ዕውቀት የላቸውም።

21ጕዳያችሁን ተናገሩ፤ አቅርቡ፤

ተሰብስበውም ይማከሩ።

ይህን አስቀድሞ ማን ዐወጀ?

ከጥንትስ ማን ተናገረ?

እኔ እግዚአብሔር አይደለሁምን?

ጻድቅና አዳኝ የሆነ አምላክ፣

ከእኔ በቀር ማንም የለም፤

ከእኔ ሌላ አምላክ የለም።

22“እናንት የምድር ዳርቻ ሁሉ፣

እኔ አምላክ ነኝ፤ ከእኔም በቀር ሌላ የለምና፤

ትድኑ ዘንድ ወደ እኔ ተመለሱ።

23ጕልበት ሁሉ በእኔ ፊት ይንበረከካል፤

አንደበትም ሁሉ በእኔ ይምላል፤

ብዬ በራሴ ምያለሁ፤

የማይታጠፍ ቃል፣

ከአፌ በጽድቅ ወጥቷል።

24ስለ እኔም ሲናገሩ፣ ‘ጽድቅና ኀይል፣

በእግዚአብሔር ብቻ ነው’ ይላሉ።”

በእርሱ ላይ በቍጣ የተነሡ ሁሉ፣

ወደ እርሱ መጥተው ያፍራሉ።

25ነገር ግን የእስራኤል ዘር ሁሉ፣

በእግዚአብሔር ይጸድቃሉ፤

ሞገስንም ያገኛሉ።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 45:1-25

1Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake

Koresi amene anamugwira dzanja lamanja

kuti agonjetse mitundu ya anthu

ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo,

ndi kutsekula zitseko

kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:

2Ine ndidzayenda patsogolo pako,

ndi kusalaza mapiri;

ndidzaphwanya zitseko za mkuwa

ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.

3Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima,

katundu wa pamalo obisika,

kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova

Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.

4Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo,

chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli,

Ine ndakuyitana pokutchula dzina

ndipo ndakupatsa dzina laulemu

ngakhale iwe sukundidziwa Ine.

5Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina;

kupatula Ine palibenso Mulungu wina.

Ndidzakupatsa mphamvu,

ngakhale sukundidziwa Ine,

6kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo

anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha.

Ine ndine Yehova,

ndipo palibenso wina.

7Ndimalenga kuwala ndi mdima,

ndimabweretsa madalitso ndi tsoka;

ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.

8“Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba;

mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo.

Dziko lapansi litsekuke,

ndipo chipulumutso chiphuke kuti

chilungamo chimereponso;

Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.

9“Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake,

ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake.

Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti,

‘Kodi ukuwumba chiyani?’

Kodi ntchito yako inganene kuti,

‘Ulibe luso?’

10Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti,

‘Kodi munabereka chiyani?’

Kapena amayi ake kuti,

‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’

11“Yehova

Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena,

zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi:

Kodi iwe ukundifunsa za ana anga,

kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?

12Ndine amene ndinapanga dziko lapansi

ndikulenga munthu kuti akhalemo.

Ine ndi manja anga ndinayalika thambo;

ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.

13Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe:

ndipo ndidzawongolera njira zake zonse.

Iye adzamanganso mzinda wanga

ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo,

wopanda kupereka ndalama kapena mphotho,

akutero Yehova Wamphamvuzonse.”

14Yehova akuti,

“Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu.

Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba

adzabwera kwa inu

ndipo adzakhala anthu anu;

iwo adzidzakutsatani pambuyo panu

ali mʼmaunyolo.

Adzakugwadirani

ndi kukupemphani, ponena kuti,

‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina;

palibenso mulungu wina.’ ”

15Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika

amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.

16Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa.

Adzakhala osokonezeka maganizo.

17Koma Yehova adzapulumutsa Israeli

ndi chipulumutso chamuyaya;

simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka

mpaka kalekale.

18Yehova

analenga zinthu zakumwamba,

Iye ndiye Mulungu;

amene akulenga dziko lapansi,

ndi kulikhazikitsa,

sanalipange kuti likhale lopanda kanthu,

koma analipanga kuti anthu akhalemo.

Iyeyu akunena kuti:

Ine ndine Yehova,

ndipo palibenso wina.

19Ine sindinayankhule mwachinsinsi,

pamalo ena a mdima;

Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti,

“Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.”

Ine Yehova, ndimayankhula zoona;

ndikunena zolungama.

20Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere;

yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina.

Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo,

amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.

21Fotokozani mlandu wanu,

mupatsane nzeru nonse pamodzi.

Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale?

Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana?

Kodi si Ineyo Yehova?

Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine,

Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa,

palibenso wina kupatula Ine.

22“Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke,

inu anthu onse a pa dziko lapansi,

pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.

23Ndalumbira ndekha,

pakamwa panga patulutsa mawu owona,

mawu amene sadzasinthika konse akuti,

bondo lililonse lidzagwada pamaso panga;

anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.

24Iwo adzanene kwa Ine kuti,

‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’ ”

Onse amene anamuwukira Iye

adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.

25Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli

zidzapambana ndi kupeza ulemerero.