ኢሳይያስ 40 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢሳይያስ 40:1-31

የእግዚአብሔርን ሕዝብ የሚያጽናና ቃል

1አጽናኑ፤ ሕዝቤን አጽናኑ፤

ይላል አምላካችሁ።

2ለኢየሩሳሌም አለዝባችሁ ንገሯት፤

ዐውጁላትም፤

በባርነት ያገለገለችበት ዘመን አብቅቷል፤

የኀጢአቷም ዋጋ ተከፍሏል፤

ስለ ኀጢአቷ ሁሉ ከእግዚአብሔር እጅ

ሁለት ዕጥፍ ተቀብላለች።

3የዐዋጅ ነጋሪ ድምፅ እንዲህ ይላል፤

የእግዚአብሔርን መንገድ፣

በምድረ በዳ አዘጋጁ፤

ለአምላካችን አውራ ጐዳና፣

በበረሓ አስተካክሉ።

4ሸለቆው ሁሉ ከፍ ይላል፤

ተራራውና ኰረብታው ሁሉ ዝቅ ይላል፤

ወጣ ገባው ምድር ይስተካከላል፤

ሰርጓጕጡም ሜዳ ይሆናል።

5የእግዚአብሔርም ክብር ይገለጣል፤

ሰው ሁሉ በአንድነት ያየዋል፤

የእግዚአብሔር አፍ ይህን ተናግሯልና።”

6ድምፅም፣ “ጩኽ” አለኝ፤

እኔም፣ “ምን ብዬ ልጩኽ?” አልሁ።

“ሰው ሁሉ እንደ ሣር ነው፤

ክብሩም ሁሉ እንደ ሜዳ አበባ ነው።

7ሣሩ ይደርቃል፤ አበባውም ይረግፋል፤

የእግዚአብሔር እስትንፋስ ነፍሶበታልና፤

ሕዝቡ በርግጥ ሣር ነው።

8ሣሩ ይደርቃል፤ አበባውም ይረግፋል፤

የአምላካችን ቃል ግን ለዘላለም ጸንቶ ይኖራል።”

9አንተ ለጽዮን የምሥራችን የምትነግር፤

ከፍ ወዳለው ተራራ ውጣ፤

አንተ ለኢየሩሳሌም ብሥራት የምትነግር፣40፥9 ወይም፣ ጽዮን ሆይ፤ የምሥራቹን የምታበሥሪ፣ ወደ ረዥም ተራራ ላይ ውጪ ወይም የምሥራቹን የምታበሥሪ ኢየሩሳሌም ሆይ

ድምፅህን ከፍ አድርገህ ጩኽ።

ከፍ አድርገው፤ አትፍራ፤

ለይሁዳም ከተሞች፣

“እነሆ፤ አምላካችሁ!” በል።

10እነሆ፤ጌታ እግዚአብሔር በኀይል

ይመጣል፤

ክንዱ ስለ እርሱ ይገዛል።

እነሆ፤ ዋጋው ከእርሱ ጋር ነው፤

የሚከፍለውም ብድራት አብሮት አለ።

11መንጋውን እንደ እረኛ ያሰማራል፤

ጠቦቶቹን በክንዱ ይሰበስባል፤

በዕቅፉም ይይዛቸዋል፤

የሚያጠቡትንም በጥንቃቄ ይመራል።

12ውሆችን በዕፍኙ የሰፈረ፣

ሰማያትን በስንዝሩ የለካ፣

የምድርን ዐፈር በመስፈሪያ ሰብስቦ የያዘ፣

ተራሮችን በሚዛን፣

ኰረብቶችንም በመድሎት የመዘነ ማነው?

13የእግዚአብሔርን መንፈስ የተረዳ፣

አማካሪውስ ሆኖ ያስተማረው ማነው?

14ዕውቀት ለማግኘት እግዚአብሔር ማንን አማከረ?

ትክክለኛውንስ መንገድ ማን አስተማረው?

ዕውቀትን ያስተማረው፣

የማስተዋልንም መንገድ ያሳየው ማን ነበር?

15እነሆ፤ አሕዛብ በገንቦ ውስጥ እንዳለች ጠብታ ናቸው፤

በሚዛን ላይ እንዳለ ትቢያ ይቈጠራሉ፤

ደሴቶችንም እንደ ደቃቅ ዐፈር ይመዝናቸዋል።

16ሊባኖስ ለመሠዊያ እሳት አትበቃም፤

የእንስሶቿም ቍጥር ለሚቃጠል መሥዋዕት ያንሳል።

17አሕዛብ ሁሉ በፊቱ እንደ ኢምንት ናቸው፤

ከምንም የማይቈጠሩ መና ናቸው።

18እንግዲህ፣ እግዚአብሔርን ከማን ጋር ታወዳድሩታላችሁ?

ከየትኛውስ ምስል ጋር ታነጻጽሩታላችሁ?

19የተቀረጸውንማ ምስል ባለ እጅ ይቀርጸዋል፤

ወርቅ አንጥረኛም በወርቅ ይለብጠዋል፤

የብር ሰንሰለትም ያበጅለታል።

20እንዲህ ያለውን መባ ማቅረብ የማይችል ምስኪን ድኻ፣

የማይነቅዝ ዕንጨት ይመርጣል፤

የማይወድቅ ምስልን ለማቆምም፣

ታዋቂ ባለሙያ ይፈልጋል።

21አላወቃችሁምን?

አልሰማችሁምን?

ከጥንት አልተነገራችሁምን?

ምድር ከተመሠረተች ጀምሮ አላስተዋላችሁምን?

22እርሱ ከምድር ክበብ በላይ በዙፋን ላይ ይቀመጣል፤

ሕዝቦቿም እንደ አንበጣ ናቸው።

ሰማያትን እንደ ድባብ ይዘረጋቸዋል፤

እንደ መኖሪያ ድንኳንም ይተክላቸዋል።

23አለቆችን ኢምንት፣

የዚህን ዓለም ገዦች እንዳልነበሩ ያደርጋቸዋል።

24ተተክለው ምንም ያህል ሳይቈዩ፣

ተዘርተው ምንም ያህል ሳይሰነብቱ፣

ገና ሥር መስደድ ሳይጀምሩ

አነፈሰባቸው፤ እነርሱም ደረቁ፤

ዐውሎ ነፋስም እንደ ገለባ ጠራርጎ ወሰዳቸው።

25ቅዱሱ፣ “ከማን ጋር ታወዳድሩኛላችሁ?

የሚስተካከለኝስ ማን አለ?” ይላል።

26ዐይናችሁን አንሡ፤ ወደ ሰማይ ተመልከቱ፤

እነዚህን ሁሉ የፈጠረ ማን ነው?

የከዋክብትን ሰራዊት አንድ በአንድ የሚያወጣቸው፣

በየስማቸው የሚጠራቸው እርሱ ነው።

ከኀይሉ ታላቅነትና ከችሎታው ብርታት የተነሣ፣

አንዳቸውም አይጠፉም።

27ያዕቆብ ሆይ፤ ለምን እንዲህ ትላለህ?

እስራኤል ሆይ፤ ለምን እንዲህ ትናገራለህ?

“መንገዴ ከእግዚአብሔር ተሰውራለች፤

ፍርዴም በአምላኬ ቸል ተብላለች” ለምን ትላለህ?

28አታውቅምን?

አልሰማህምን?

እግዚአብሔር የዘላለም አምላክ፣

የምድር ዳርቻ ፈጣሪ ነው።

አይደክምም፤ አይታክትም፤

ማስተዋሉም በማንም አይመረመርም።

29ለደከመው ብርታት ይሰጣል፤

ለዛለው ጕልበት ይጨምራል።

30ወጣቶች እንኳ ይደክማሉ፤ ይታክታሉም፤

ጐበዛዝትም ተሰናክለው ይወድቃሉ።

31እግዚአብሔርን ተስፋ የሚያደርጉ ግን፣

ኀይላቸውን ያድሳሉ፤

እንደ ንስር በክንፍ ይወጣሉ፤

ይሮጣሉ፤ አይታክቱም፤

ይሄዳሉ፤ አይደክሙም።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 40:1-31

Mawu a Chitonthozo kwa Anthu a Mulungu

1Atonthozeni, atonthozeni anthu anga,

akutero Mulungu wanu.

2Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu

ndipo muwawuzitse

kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha,

tchimo lawo lakhululukidwa.

Ndawalanga mokwanira

chifukwa cha machimo awo onse.

3Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti,

“Konzani njira ya Yehova

mʼchipululu;

wongolani njira zake;

msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.

4Chigwa chilichonse achidzaze.

Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse;

Dziko lokumbikakumbika alisalaze,

malo azitundazitunda awasandutse zidikha.

5Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera,

ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona,

pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”

6Wina ananena kuti, “Lengeza.”

Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani?

“Pakuti anthu onse ali ngati udzu

ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.

7Udzu umanyala ndipo maluwa amafota

chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.”

Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.

8Udzu umanyala ndipo maluwa amafota,

koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”

9Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni,

kwera pa phiri lalitali.

Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu,

fuwula kwambiri,

kweza mawu, usachite mantha;

uza mizinda ya ku Yuda kuti,

“Mulungu wanu akubwera!”

10Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu,

ndipo dzanja lake likulamulira,

taonani akubwera ndi mphotho yake

watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.

11Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa:

Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake

ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake

ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.

12Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake,

kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake?

Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu,

kapena kuyeza kulemera kwa

mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?

13Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova

kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?

14Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya,

kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru?

Iye anapempha nzeru kwa yani

ndi njira ya kumvetsa zinthu?

15Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko.

Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo;

mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.

16Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe,

ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.

17Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake;

Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu

ndi cha chabechabe.

18Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani?

Kodi mungamufanizire ndi chiyani?

19Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga

ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide

naliveka mkanda wasiliva.

20Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere

amasankha mtengo umene sudzawola,

nafunafuna mʼmisiri waluso woti

amupangire fano limene silingasunthike.

21Kodi simukudziwa?

Kodi simunamve?

Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe?

Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?

22Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi,

Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala.

Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga,

nayikunga ngati tenti yokhalamo.

23Amatsitsa pansi mafumu amphamvu

nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.

24Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene

kapena kufesedwa chapompano,

ndi kungoyamba kuzika mizu kumene

ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa

ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.

25Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani?

Kapena kodi alipo wofanana nane?”

26Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani.

Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi?

Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo,

nayitana iliyonse ndi dzina lake.

Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri,

palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.

27Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena

ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti,

“Yehova sakudziwa mavuto anga,

Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”

28Kodi simukudziwa?

Kodi simunamve?

Yehova ndiye Mulungu wamuyaya,

ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi.

Iye sadzatopa kapena kufowoka

ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.

29Iye amalimbitsa ofowoka

ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.

30Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka,

ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;

31koma iwo amene amakhulupirira Yehova

adzalandira mphamvu zatsopano.

Adzawuluka ngati chiwombankhanga;

adzathamanga koma sadzalefuka,

adzayenda koma sadzatopa konse.