መዝሙር 140 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 140:1-13

መዝሙር 140

በክፉዎች ላይ የቀረበ ጸሎት

ለመዘምራን አለቃ፤ የዳዊት መዝሙር።

1እግዚአብሔር ሆይ፤ ከክፉ ሰዎች አድነኝ፤

ከዐመፀኞችም ሰዎች ጠብቀኝ፤

2እነርሱ በልባቸው ክፉ ነገር ያውጠነጥናሉ፤

በየዕለቱም ጦርነት ይጭራሉ።

3ምላሳቸውን እንደ እባብ ያሾላሉ፤

ከከንፈራቸውም በታች የእፉኝት መርዝ አለ። ሴላ

4እግዚአብሔር ሆይ፤ ከክፉዎች እጅ ጠብቀኝ፤

እግሮቼንም ለመጥለፍ ከሚያደቡ ዐመፀኞች ሰውረኝ።

5ትዕቢተኞች ወጥመድ በስውር አስቀመጡብኝ፤

የመረባቸውን ገመድ ዘረጉብኝ፤

በመንገዴም ላይ አሽክላ አኖሩ። ሴላ

6እግዚአብሔር ሆይ፤ “አንተ አምላኬ ነህ” እልሃለሁ፤

እግዚአብሔር ሆይ፤ የልመና ጩኸቴን ስማ።

7ብርቱ አዳኝ የሆንህ ጌታ እግዚአብሔር ሆይ፤

በጦርነት ዕለት የራስ ቍር ሆንኸኝ።

8እግዚአብሔር ሆይ፤ የክፉዎች ምኞት አይፈጸም፤

በትዕቢትም እንዳይኵራሩ፣

ዕቅዳቸው አይሳካ። ሴላ

9ዙሪያዬን የከበቡኝ ሰዎች ራስ፣

የከንፈራቸው መዘዝ ይጠምጠምበት።

10የእሳት ፍም በላያቸው ይውረድ፤

ዳግመኛም እንዳይነሡ ወደ እሳት ይጣሉ፤

ማጥ ወዳለበት ጕድጓድ ይውደቁ።

11ምላሰኛ በምድሪቱ ጸንቶ አይኑር፤

ዐመፀኛውን ሰው ክፋት አሳድዶ ያጥፋው።

12እግዚአብሔር ለድኻ ፍትሕን እንደሚያስከብር፣

ለችግረኛውም ትክክለኛ ፍርድን እንደሚሰጥ ዐውቃለሁ።

13ጻድቃን በእውነት ስምህን ያመሰግናሉ፤

ቅኖችም በፊትህ ይኖራሉ።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 140:1-13

Salimo 140

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Landitseni Yehova kwa anthu oyipa;

tetezeni kwa anthu ankhanza,

2amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa

ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.

3Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka;

pa milomo yawo pali ululu wa mamba.

Sela

4Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa;

tchinjirizeni kwa anthu ankhanza

amene amakonza zokola mapazi anga.

5Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika;

iwo atchera zingwe za maukonde awo

ndipo anditchera misampha pa njira yanga.

Sela

6Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.”

Imvani kupempha kwanga Yehova.

7Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu,

mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.

8Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova;

musalole kuti zokonza zawo zitheke,

mwina iwo adzayamba kunyada.

Sela

9Mitu ya amene andizungulira

iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.

10Makala amoto agwere pa iwo;

aponyedwe pa moto,

mʼmaenje amatope, asatulukemonso.

11Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko;

choyipa chilondole anthu ankhanza.

12Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka,

ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.

13Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu,

ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.