መዝሙር 104 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 104:1-35

መዝሙር 104

የፍጥረት መብት

1ነፍሴ ሆይ፤ እግዚአብሔርን ባርኪ፤

እግዚአብሔር አምላኬ ሆይ፤ አንተ እጅግ ታላቅ ነህ፤

ክብርንና ግርማን ለብሰሃል።

2ብርሃንን እንደ ሸማ ተጐናጽፈሃል፤

ሰማያትንም እንደ ድንኳን መጋረጃ ዘረጋህ፤

3የእልፍኝህን አግዳሚ በውሆች ላይ አኖርህ፤

ደመናትን ሠረገላህ አደረግህ፤

በነፋስ ክንፍ ትሄዳለህ።

4መላእክትህን104፥4 መልእክተኞቹን ወይም አገልጋዮቹን መንፈስ፣

አገልጋዮችህንም የእሳት ነበልባል ታደርጋለህ።

5ለዘላለም እንዳትናወጥ፣

ምድርን በመሠረቷ ላይ አጸናሃት።

6በጥልቁ እንደ ልብስ ሸፈንሃት፤

ውሆችም ከተራሮች በላይ ቆሙ።

7በገሠጽሃቸው ጊዜ ግን ፈጥነው ሄዱ፤

የነጐድጓድህንም ድምፅ በሰሙ ጊዜ ሸሹ።

8በተራሮች ላይ ፈሰሱ፤

ወዳዘጋጀህላቸው ስፍራ፣

ወደ ሸለቆዎች ወረዱ።

9ተመልሰው ምድርን እንዳይሸፍኑ፣

ዐልፈውም እንዳይመጡ ድንበር አበጀህላቸው።

10ምንጮችን በሸለቆ ውስጥ እንዲሄዱ አደረግህ፤

በተራሮችም መካከል ይፈስሳሉ፤

11የዱር እንስሳትም ከዚያ ይጠጣሉ፤

የሜዳ አህዮችም ጥማቸውን ይቈርጣሉ።

12የሰማይ ወፎች ጎጇቸውን በወንዞቹ ዳር ይሠራሉ፤

በቅርንጫፎችም መካከል ይዘምራሉ።

13ከላይ ከእልፍኝህ ተራሮችህን ታጠጣለህ፤

ምድርም በሥራህ ፍሬ ትረካለች።

14ከምድር ምግብን ታወጣ ዘንድ፣

ለእንስሳት ሣርን፣

ለሰው ልጆች ሥራ ዕፀዋትን ታበቅላለህ፤

15የሰውን ልብ ደስ የሚያሰኝ ወይን፣

ፊቱን የሚያወዛ ዘይት፣

ልቡን የሚያበረታ እህል በዚህ ይገኛል።

16ደግሞም የእግዚአብሔር ዛፎች፣

እርሱ የተከላቸውም የሊባኖስ ዝግባዎች ጠጥተው ይረካሉ፤

17ወፎች ጎጇቸውን በዚያ ይሠራሉ፤

ሽመላ በጥዶቹ ውስጥ ማደሪያ ታገኛለች።

18ረጃጅሙ ተራራ የዋሊያ መኖሪያ፣

የዐለቱም ዋሻዎች የሽኮኮ መሸሸጊያ ናቸው።

19ጨረቃን የወቅቶች መለያ አደረግሃት፤

ፀሓይም የምትጠልቅበትን ጊዜ ታውቃለች።

20ጨለማን ታመጣለህ፤ ሌሊትም ይሆናል፤

የዱር አራዊትም ሁሉ በዚህ ጊዜ ወጥተው ይራወጣሉ።

21የአንበሳ ግልገሎች ምግብ ፍለጋ ይጮኻሉ፤

የሚበሉትንም ከእግዚአብሔር ይሻሉ።

22ፀሓይ በወጣች ጊዜም ይመለሳሉ፤

በየጐሬያቸውም ገብተው ይተኛሉ።

23ሰውም ወደ ሥራው ይሄዳል፤

እስኪመሽም በተግባሩ ላይ ይሰማራል።

24እግዚአብሔር ሆይ፤ ሥራህ እንዴት ብዙ ነው!

ሁሉን በጥበብ ሠራህ፤

ምድርም በፍጥረትህ ተሞላች።

25ይህች ባሕር ሰፊና የተንጣለለች ናት፤

ታላላቅና ታናናሽ እንስሳት፣

ስፍር ቍጥር የሌላቸውም ነፍሳት በውስጧ አሉ።

26መርከቦች በላይዋ ይመላለሳሉ፤

አንተ የፈጠርኸውም ሌዋታን በውስጧ ይፈነጫል።

27ምግባቸውን በወቅቱ ትሰጣቸው ዘንድ፣

እነዚህ ሁሉ አንተን ተስፋ ያደርጋሉ።

28በሰጠሃቸውም ጊዜ፣

አንድ ላይ ያከማቻሉ፤

እጅህንም ስትዘረጋ፣

በመልካም ነገር ይጠግባሉ።

29ፊትህን ስትሰውር፣

በድንጋጤ ይሞላሉ፤

እስትንፋሳቸውንም ስትወስድባቸው ይሞታሉ፤

ወደ ዐፈራቸውም ይመለሳሉ።

30መንፈስህን ስትልክ፣

እነርሱ ይፈጠራሉ፤

የምድርንም ገጽ ታድሳለህ።

31የእግዚአብሔር ክብር ለዘላለም ጸንቶ ይኑር፤

እግዚአብሔር በሥራው ደስ ይበለው፤

32እርሱ ምድርን ሲመለከት፣ ትንቀጠቀጣለች፤

ተራሮችም እርሱ ሲዳስሳቸው ይጤሳሉ።

33በሕይወት ሳለሁ ለእግዚአብሔር እዘምራለሁ፤

ቆሜ እስከ ሄድሁ ድረስም አምላኬን እወድሳለሁ።

34እኔ በእግዚአብሔር ደስ እንደሚለኝ፣

የልቤ ሐሳብ እርሱን ደስ ያሰኘው።

35ኀጥኣን ከምድር ገጽ ይጥፉ፤

ዐመፀኞች ከእንግዲህ አይገኙ።

ነፍሴ ሆይ፤ እግዚአብሔርን ባርኪ፤

ሃሌ ሉያ።104፥35 እግዚአብሔር ይመስገን የሚሉ ትርጕሞች አሉ፤ በሰብዓ ሊቃናት ትርጕም ይህ መሥመር በመዝ 105 መጀመሪያ ላይ ይገኛል።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 104:1-35

Salimo 104

1Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.

Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri;

mwavala ulemerero ndi ufumu.

2Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala;

watambasula miyamba ngati tenti

3ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake.

Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake,

ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.

4Amapanga mphepo kukhala amithenga ake,

malawi amoto kukhala atumiki ake.

5Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake;

silingasunthike.

6Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala;

madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.

7Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa,

pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;

8Inu munamiza mapiri,

iwo anatsikira ku zigwa

kumalo kumene munawakonzera.

9Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa,

iwo sadzamizanso dziko lapansi.

10Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa;

madziwo amayenda pakati pa mapiri.

11Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo;

abulu akuthengo amapha ludzu lawo.

12Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi;

zimayimba pakati pa thambo.

13Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba;

dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.

14Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye,

ndi zomera, kuti munthu azilima

kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:

15vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu,

mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala,

ndi buledi amene amapereka mphamvu.

16Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino,

mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.

17Mbalame zimamanga zisa zawo;

kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.

18Mapiri ataliatali ndi a mbalale;

mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.

19Mwezi umasiyanitsa nyengo

ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.

20Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku,

ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.

21Mikango imabangula kufuna nyama,

ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.

22Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala;

imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.

23Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake,

kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.

24Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova!

Munazipanga zonse mwanzeru,

dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.

25Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala,

yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka,

zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.

26Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku,

ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.

27Zonsezi zimayangʼana kwa Inu

kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.

28Mukazipatsa,

zimachisonkhanitsa pamodzi;

mukatsekula dzanja lanu,

izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.

29Mukabisa nkhope yanu,

izo zimachita mantha aakulu;

mukachotsa mpweya wawo,

zimafa ndi kubwerera ku fumbi.

30Mukatumiza mzimu wanu,

izo zimalengedwa

ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.

31Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya;

Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;

32Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera,

amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.

33Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse;

ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.

34Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye,

pamene ndikusangalala mwa Yehova.

35Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi

ndipo anthu oyipa asapezekenso.

Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga.

Tamandani Yehova.