መክብብ 4 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መክብብ 4:1-16

ግፍ፣ ጥረት፣ ብቸኝነት

1እንደ ገና ከፀሓይ በታች የሚደረገውን ግፍ ሁሉ አየሁ፤ አስተዋልሁም፤

የተገፉትን ሰዎች እንባ ተመለከትሁ፤

የሚያጽናናቸውም አልነበረም፤

ኀይል በሚገፏቸው ሰዎች እጅ ነበረ፤

የሚያጽናናቸውም አልነበረም።

2እኔም የቀድሞ ሙታን፣

ዛሬ በሕይወት ካሉት ሕያዋን ይልቅ፣

ደስተኞች እንደ ሆኑ ተናገርሁ።

3ነገር ግን ከሁለቱም ይልቅ፣

ገና ያልተወለደው፣

ከፀሓይ በታች የሚደረገውንም፣

ክፋት ያላየው ይሻላል።

4እንዲሁም ጥረትና የሥራ መከናወን ሁሉ ሰው በባልንጀራው ላይ ካለው ቅናት እንደሚመነጭ ተመለከትሁ፤ ይህም ደግሞ ከንቱ፣ ነፋስንም እንደ መከተል ነው።

5ሰነፍ እጁን አጣጥፎ ይቀመጣል፤

የገዛ ራሱንም ሥጋ ይበላል።

6በድካምና ነፋስን በመከተል ከሚገኝ ሁለት ዕፍኝ ይልቅ፣

በርጋታ የሚገኝ አንድ ዕፍኝ ይሻላል።

7ደግሞም ከፀሓይ በታች ከንቱ የሆነን ነገር አየሁ፤

8ልጅም ሆነ ወንድም የሌለው፣

ብቸኛ ሰው አለ፤

ጥረቱ ማለቂያ የለውም፤ ዐይኑም ባለው ሀብት ገና አልረካም፤

እርሱም፣ “ለማን ብዬ ነው የምደክመው?

ራሴን ከማስደሰትስ የምቈጠበው

ለምንድን ነው?” ብሎ ጠየቀ፤

ይህም ደግሞ ከንቱ፣ የጭንቅ ኑሮ ነው።

9ለሥራቸው መልካም ውጤት ስለሚያገኙ፣

ከአንድ፣ ሁለት መሆን ይሻላል፤

10አንዱ ቢወድቅ፣

ባልንጀራው ደግፎ ያነሣዋል።

ቢወድቅ የሚያነሣው ረዳት የሌለው ግን፣

እንዴት አሳዛኝ ነው!

11ደግሞም ሁለቱ አብረው ቢተኙ ይሞቃቸዋል፤

ነገር ግን አንዱ ብቻውን እንዴት ሊሞቀው ይችላል?

12አንድ ሰው ብቸኛውን ቢያጠቃውም፣

ሁለት ከሆኑ ይመክቱታል፤

በሦስት የተገመደ ገመድም ቶሎ አይበጠስም።

በልጦ መገኘት ከንቱ ነው

13ምክርን መቀበል ከማያውቅ ሞኝና ሽማግሌ ንጉሥ ይልቅ ጠቢብ የሆነ ድኻ ወጣት ይሻላል። 14ወጣቱ ከእስር ቤት ወደ ንጉሥነት የመጣ ወይም በግዛቱ ውስጥ በድኽነት የተወለደ ሊሆን ይችላል። 15ከፀሓይ በታች የሚኖሩና የሚመላለሱ ሁሉ፣ ንጉሡን የሚተካውን ወጣት ተከትለውት አየሁ። 16በፊቱ የነበረው ሕዝብ ሁሉ ቍጥር ስፍር አልነበረውም፤ ከእርሱ በኋላ የመጡት ግን በተተኪው አልተደሰቱም። ይህም ደግሞ ከንቱ፣ ነፋስንም እንደ መከተል ነው።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 4:1-16

Matsoka ndi Mavuto a Moyo Uno

1Ndinayangʼananso ndi kuona chipsinjo chimene chimachitika pansi pano:

ndinaona misozi ya anthu opsinjika,

ndipo iwo alibe owatonthoza;

mphamvu zinali ndi anthu owapsinjawo

ndipo iwonso analibe owatonthoza.

2Ndipo ndinanena kuti akufa,

amene anafa kale,

ndi osangalala kuposa amoyo,

amene akanalibe ndi moyo.

3Koma wopambana onsewa

ndi amene sanabadwe,

amene sanaone zoyipa

zimene chimachitika pansi pano.

4Ndipo ndinazindikira kuti ntchito zonse zolemetsa ndiponso ntchito zonse zaluso zimachitika chifukwa choti wina akuchitira nsanje mnzake. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.

5Chitsiru chimangoti manja ake lobodo

ndi kudzipha chokha ndi njala.

6Nʼkwabwino kukhala ndi dzanja limodzi lodzaza uli pa mtendere,

kuposa kukhala ndi manja awiri odzaza uli pa mavuto,

ndipo uku nʼkungodzivuta chabe.

7Ndinaonanso chinthu china chopanda phindu pansi pano:

8Panali munthu amene anali yekhayekha;

analibe mwana kapena mʼbale.

Ntchito yake yolemetsa sinkatha,

ndipo maso ake sankakhutitsidwa ndi chuma chake.

Iye anadzifunsa kuti, “Kodi ntchito yosautsayi ndikuyigwirira yani?

Nanga nʼchifukwa chiyani ndikudzimana chisangalalo?”

Izinso ndi zopandapake,

zosasangalatsa!

9Kukhala awiri nʼkwabwino kuposa kukhala wekha,

chifukwa ntchito ya anthu awiri ili ndi phindu:

10Ngati winayo agwa,

mnzakeyo adzamudzutsa.

Koma tsoka kwa munthu amene agwa

ndipo alibe wina woti amudzutse!

11Komanso ngati anthu awiri agona malo amodzi, adzafunditsana.

Koma nanga mmodzi angadzifunditse yekha?

12Munthu mmodzi angathe kugonjetsedwa,

koma anthu awiri akhoza kudziteteza.

Chingwe cha maulusi atatu sichidukirapo.

Kutukuka Nʼkopandapake

13Wachinyamata wosauka koma wanzeru aposa mfumu yokalamba koma yopusa imene simvanso malangizo. 14Wachinyamatayo angathe kuchokera ku ndende ndi kudzakhala mfumu, kapena angathe kubadwa wosauka mʼdziko la mfumuyo. 15Ndipo ndinaona kuti iwo onse amene anakhala ndi moyo ndi kuyenda pansi pano anatsatira wachinyamatayo, amene anatenga malo a mfumu. 16Mfumu ikhoza kulamulira anthu osawerengeka, komabe itamwalira, palibe amene adzayamikire zomwe mfumuyo inachita. Izinso ndi zopandapake, nʼkungozivuta chabe.