ሕዝቅኤል 27 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ሕዝቅኤል 27:1-36

ለጢሮስ የወጣ ሙሾ

1የእግዚአብሔር ቃል እንዲህ ሲል ወደ እኔ መጣ፤ 2“የሰው ልጅ ሆይ፤ ስለ ጢሮስ ሙሾ አውርድ፤ 3በባሕር መግቢያ ላይ ለምትገኘውና በብዙ ጠረፎች ከሚኖሩ ሕዝቦች ጋር ለምትነግደው ለጢሮስ እንዲህ በላት፤ ‘ጌታ እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤

“ ‘ጢሮስ ሆይ፤

“ፍጹም ውብ ነኝ” ብለሻል፤

4ዳርቻሽ በባሕር መካከል ነው፤

ሠሪዎችሽም ፍጹም ውብ አድርገውሻል።

5ሳንቃዎችሽን ሁሉ፣

ከሳኔር27፥5 ሄርሞንን ማለት ነው። በመጣ ጥድ ሠሩ፤

ደቀልንም ይሠሩልሽ ዘንድ፤

ከሊባኖስ ዝግባ አመጡ።

6ከባሳን በመጣ ወርካ፣

መቅዘፊያሽን ሠሩ፤

ከቆጵሮስ27፥6 ዕብራይስጡ ኪጢም ይለዋል። ጠረፍ በመጣ ዝግባ፣27፥6 በታርጕምም እንዲሁ ሲሆን የማሶሬቱ መጽሐፍ የድምፅ ተቀባዮች ፊደል አከፋፈል ግን የተለየ ነው።

በዝኆን ጥርስ ለብጠው ወለልሽን ሠሩ።

7የመርከቦችሽ ሸራ ጥልፍ ሥራ ያለበት የግብፅ በፍታ ነበረ፤

ይህም እንደ ዐርማ አገለገለሽ።

መጋረጃዎችሽ ከኤሊሳ ጠረፍ የመጡ፣

ባለ ሰማያዊና ሐምራዊ ቀለም ነበሩ።

8ቀዛፊዎችሽ ከሲዶናና ከአራድ የመጡ ነበሩ፤

ጢሮስ ሆይ፤ የራስሽ ጠቢባን የመርከቦችሽ መሪዎች ነበሩ።

9ልምድ ያካበቱ የጌባል27፥9 ባይብሎስ ማለት ነው። ባለሙያዎች፣

መርከብሽን ለመገጣጠም በመካከልሽ ነበሩ፤

የባሕር መርከቦችና መርከበኞቻቸው ሁሉ፣

ከአንቺ ጋር ሊገበያዩ ይመጡ ነበር።

10“ ‘የፋርስ፣ የሉድና የፉጥ ሰዎች፣

ወታደር ሆነው በሰራዊትሽ ውስጥ አገለገሉ፤

ሞገስም ይሆኑሽ ዘንድ፣

ጋሻቸውንና የራስ ቍራቸውን በግድግዳሽ ላይ ሰቀሉ።

11የአራድና የሔሌክ ሰዎች፣

ቅጥርሽን በየአቅጣጫው ጠበቁ፤

የገማድ ሰዎችም፣ በምሽግሽ ውስጥ ነበሩ።

ጋሻቸውንም በቅጥርሽ ዙሪያ ሰቀሉ፤

ውበትሽንም ፍጹም አደረጉ።

12“ ‘ከሀብትሽ ብዛት የተነሣ፣ ተርሴስ ከአንቺ ጋር የንግድ ልውውጥ ታደርግ ነበር፤ ብርና ብረት፣ ቈርቈሮና እርሳስ አምጥታ ሸቀጥሽን ትለውጥ ነበር።

13“ ‘ያዋን፣ ቶቤልና ሞሳሕ ከአንቺ ጋር ይነግዱ ነበር፤ ባሪያዎችንና የናስ ዕቃዎችን በሸቀጥሽ ይለውጡ ነበር።

14“ ‘የቤት ቴርጋማ ሰዎችም መጋዣዎችን፣ የጦር ፈረሶችንና በቅሎዎችን በሸቀጥሽ ለወጡ።

15“ ‘የድዳን27፥15 ከሰብዐ ሊቃናት ጋር ተመሳሳይ ሲሆን ዕብራይስጡ ግን ዴዳን ይለዋል። ሰዎች ከአንቺ ጋር ተገበያዩ፤ ብዙ የጠረፍ አገሮችም የንግድ ደንበኞችሽ ነበሩ፤ በዝኆን ጥርስና በዞጲ ሸቀጥሽን ይገዙ ነበር።

16“ ‘ምርትሽ ብዙ እንደ መሆኑ፣ ሶርያ27፥16 በአብዛኛዎቹ የዕብራይስጥ የጥንት ቅጆችም እንዲሁ ሲሆን፣ አንዳንድ የጥንት የዕብራይስጥ ቅጆችና ሱርስቱ ግን ኤዶም ይላሉ። ከአንቺ ጋር ትገበያይ ነበር፤ ሸቀጥሽንም በበሉር፣ በሐምራዊ ጨርቅ፣ በወርቀ ዘቦ፣ በጥሩ በፍታ፣ በዛጐልና በቀይ ዕንይለውጡ ነበር።

17“ ‘ይሁዳና እስራኤል እንኳ ከአንቺ ጋር ተገበያይተዋል፤ የሚኒትን ስንዴ፣ ጣፋጭ ቂጣ፣27፥17 በዕብራይስጥ የዚህ ቃል ትርጕም አይታወቅም። ማር፣ ዘይትና በለሳን በማምጣት በሸቀጥሽ ይለውጡ ነበር።

18“ ‘ከሀብት ከንብረትሽ ብዛት የተነሣ፣ ደማስቆ የኬልቦንን የወይን ጠጅና፣ የዛሐርን የበግ ጠጕር በማቅረብ ከአንቺ ጋር ተገበያይታለች።

19“ ‘ዌንዳንና ያዋን ከኦሴል መጥተው ከአንቺ ጋር የንግድ ልውውጥ ያደርጉ ነበር፤ ቀልጦ የተሠራ ብረትን፣ ብርጕድንና ቀረፋን በሸቀጥሽ ይለውጡ ነበር።

20“ ‘ድዳን ግላስ በማቅረብ ከአንቺ ጋር ትነግድ ነበር።

21“ ‘የዐረብና የቄዳር መሳፍንት ሁሉ ደንበኞችሽ ነበሩ፤ ጠቦትና አውራ በግ፣ ፍየልም አምጥተው ከአንቺ ጋር ይገበያዩ ነበር።

22“ ‘የሳባና የራዕማ ነጋዴዎች ከአንቺ ጋር ይገበያዩ ነበር፤ ምርጥ የሆነውን የሽቱ ቅመም ዐይነት ሁሉ፣ የከበረ ድንጋይና ወርቅ በማቅረብ በሸቀጥሽ ይለውጡ ነበር።

23“ ‘ካራን፣ ካኔ፣ ዔድን፣ የሳባ ነጋዴዎች፣ አሦርና ኪልማድ ከአንቺ ጋር የንግድ ልውውጥ ያደርጉ ነበር። 24እነዚህም በገበያሽ ውስጥ ያማረ ልብስ፣ ሰማያዊ ካባ፣ ወርቀ ዘቦ እንዲሁም በኅብረ ቀለም ያሸበረቀና በጥብቅ የተታታ ስጋጃ በማቅረብ ከአንቺ ጋር ይነግዱ ነበር።

25“ ‘የተርሴስ መርከቦች፣

ሸቀጥሽን አጓጓዙልሽ፤

በባሕር መካከልም፣

በከባድ ጭነት ተሞልተሽ ነበር።

26ቀዛፊዎችሽ፣

ወደ ጥልቁ ባሕር ይወስዱሻል፤

የምሥራቁ ነፋስ ግን፣

በባሕሩ መካከል ይሰባብርሻል።

27የመርከብ አደጋ በሚደርስበሽ ቀን፣

ሀብትሽ፣ ሸቀጥሽና የንግድ ዕቃሽ፣

መርከብ ነጂዎችሽ፣ መርከበኞችሽና መርከብ ሠሪዎችሽ፣

ነጋዴዎችሽና ወታደሮችሽ ሁሉ፣

በመርከብ ላይ ያሉትም ሁሉ፣

ወደ ባሕሩ ወለል ይዘቅጣሉ።

28መርከበኞችሽ ሲጮኹ፣

የባሕሩ ጠረፍ ይናወጣል።

29ቀዛፊዎች ሁሉ፣

መርከባቸውን ጥለው ይሄዳሉ፤

መርከብ ነጂዎችና መርከበኞችም ሁሉ፣

ወርደው ባሕሩ ዳር ይቆማሉ፤

30ድምፃቸውን ከፍ አድርገው፣

በምሬት ያለቅሱልሻል፤

በራሳቸውም ላይ ዐቧራ ነስንሰው፣

በዐመድ ላይ ይንከባለላሉ።

31ስለ አንቺ ጠጕራቸውን ይላጫሉ፤

ማቅም ይለብሳሉ፤

በነፍስ ምሬት፣

በመራራም ሐዘን ያለቅሱልሻል።

32ስለ አንቺ በዋይታ ያለቅሳሉ፤

እንዲህም እያሉ ሙሾ ያወርዳሉ፤

“ባሕር ውጦት የቀረ፣

እንደ ጢሮስ ማን አለ?”

33ሸቀጥሽ ከባሕር በወጣ ጊዜ፤

ብዙ ሕዝቦችን ታጠግቢ ነበር፣

በታላቅ ሀብትሽና ሸቀጥሽ፣

የምድርን ነገሥታት ታበለጥጊ ነበር።

34አሁን ግን በጥልቅ ውሃ ውስጥ፣

በባሕር ተንኰታኵተሻል፤

ጭነትሽና ተሳፋሪዎችሽ ሁሉ፣

ከአንቺ ጋር ሰጥመዋል።

35በጠረፍ አገር የሚኖሩ ሁሉ፣

በአንቺ ሁኔታ ተደናገጡ፤

ንጉሦቻቸው በፍርሀት ራዱ፤

ፊታቸውም ተለዋወጠ።

36በሌሎች ሕዝቦች መካከል ያሉ ነጋዴዎች ምንኛ አፏጩብሽ!

መጨረሻሽ አስደንጋጭ ሆነ፤

ለዘላለምም አትገኚም።’ ”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 27:1-36

Nyimbo Yodandaulira Turo

1Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira Turo. 3Uza Turo, mzinda wokhala pa dooko la nyanja, wochita malonda ndi anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja kuti: Ambuye Yehova akuti,

“Iwe Turo, umanena kuti,

‘Ndine wokongola kwambiri.’

4Malire ako anali mʼkati mwenimweni mwa nyanja;

amisiri ako anakukongoletsa kwambiri.

5Anakupanga ndi matabwa

a payini ochokera ku Seniri;

anatenga mikungudza ya ku Lebanoni

kupangira mlongoti wako.

6Ndi mitengo ya thundu ya ku Basani

anapanga zopalasira zako;

ndi matabwa a mitengo ya payini yochokera ku zilumba za Kitimu.

Pakuti anapanga thandala lako pakati pa matabwawo panali minyanga ya njovu.

7Nsalu yabafuta yopeta yochokera ku Igupto inali thanga yako,

ndipo inakhala ngati mbendera.

Nsalu zophimba matenti ako zinali za mtundu wamtambo ndi pepo

zochokera ku zilumba za Elisa.

8Anthu a ku Sidoni ndi Arivadi ndi amene anali opalasa ako.

Anthu aluso ako, iwe Turo, anali mwa iwe ndiwo amene ankakuyendetsa.

9Akuluakulu ndi eni luso a ku Gebala anali mʼkati mwako,

ngati okonza zibowo zako.

Sitima za pa nyanja zonse, ndi oyendetsa ake

ankabwera pamodzi ndi katundu kudzachita nawe malonda.

10“Anthu a ku Perisiya, a ku Ludi ndi Puti

anali asilikali mʼgulu lako la nkhondo.

Iwo ankapachika zishango ndi zipewa zawo zankhondo pa makoma ako,

kubweretsa kwa iwe ulemerero.

11Anthu a ku Arivadi ndi Heleki

ankalondera mbali zonse za mpanda wako;

anthu a ku Gamadi

anali mu nsanja zako,

Iwo ankapachika zishango zawo pa makoma ako onse.

Amenewo ndiwo anakukongoletsa kwambiri.

12“Dziko la Tarisisi linachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako wamtundumtundu. Iwo ankapereka siliva, chitsulo, chitini ndi mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.

13“Yavani, Tubala ndi Mesaki ankachita nawe malonda; iwo ankapereka akapolo ndi ziwiya za mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.

14“Anthu a ku Beti Togarima ankapereka akavalo antchito, akavalo ankhondo ndi abulu mosinthanitsa ndi katundu wako.

15“Anthu a ku Dedani ankachita nawe malonda, ndipo anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja anali ogula malonda ako. Ankakupatsa minyanga ya njovu ndi phingo.

16“Anthu a ku Aramu ankachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa zinthu zako. Iwo ankapereka miyala ya emeradi, nsalu zapepo, nsalu zopetapeta, nsalu zabafuta, korali ndi miyala ya rubi mosinthanitsa ndi katundu wako.

17“Yuda ndi Israeli ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka tirigu ochokera ku Miniti ndi zokometsera zakudya, uchi, mafuta ndi mankhwala mosinthanitsa ndi katundu wako.

18“Anthu a ku Damasiko, chifukwa cha zinthu zako za malonda zambiri ndi katundu wako wosiyanasiyana, ankachita nawe malonda a vinyo wochokera ku Heliboni ndi ubweya wankhosa ochokera ku Zahari. 19Adani ndi Agriki ochokera ku Uzala ankagula katundu wako. Iwo ankapereka chitsulo chosalala, kasiya ndi bango lonunkhira mosinthanitsa ndi katundu wako.

20“Anthu a ku Dedani ankakugulitsa nsalu zoyika pa zishalo za akavalo.

21“Arabiya ndi mafumu onse a ku Kedara anali ogula malonda ako. Iwo ankachita nawe malonda a ana ankhosa onenepa, nkhosa zazimuna ndi mbuzi.

22“Anthu amalonda a ku Seba ndi Raama ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka zonunkhira zosiyanasiyana zabwino kwambiri, miyala yokongola ndi golide mosinthanitsa ndi katundu wako.

23“Amalonda a ku Harani, Kane, Edeni, Seba, Asuri ndi Kilimadi ankachita nawe malonda. 24Iwowa ankasinthanitsana nawe zovala zokongola, nsalu zopetapeta, zoyala pansi za mawangamawanga, atazimanga bwino ndi zingwe zolimba.

25“Sitima za pa madzi za ku Tarisisi zinali

zonyamula malonda ako.

Motero iwe uli ngati sitima yapamadzi

yodzaza ndi katundu wolemera.

26Anthu opalasa ako amakupititsa

pa nyanja yozama.

Koma mphepo yakummawa idzakuthyolathyola

pakati pa nyanja.

27Chuma chako, katundu wako, malonda ako,

okuyendetsa ako, okuwongolera ako ndi opanga sitima za pa madzi,

anthu ako amalonda ndi asilikali ako onse

ndiponso aliyense amene ali mʼmenemo

adzamira mʼnyanja

tsiku limene udzawonongeka.

28Madera a mʼmbali mwa nyanja adzagwedezeka

chifukwa cha kufuwula kwa oyendetsa sitimawo.

29Onse amene amapalasa sitima zapamadzi,

adzatuluka mʼsitima zawo;

oyendetsa ndi onse owongolera sitima zapamadzi

adzayimirira mʼmbali mwa nyanja.

30Iwo akufuwula,

kukulira iwe kwambiri;

akudzithira fumbi kumutu,

ndi kudzigubuduza pa phulusa.

31Akumeta mpala mitu yawo chifukwa cha iwe

ndipo akuvala ziguduli.

Akukulira iweyo

ndi mitima yowawa kwambiri.

32Akuyimba nyimbo

yokudandaulira nʼkumati:

‘Ndani anawonongedwapo ngati Turo

pakati pa nyanja?’

33Pamene malonda ako ankawoloka nyanja

unakhutitsa mitundu yambiri ya anthu.

Mafumu a dziko lapansi analemera ndi chuma chako

komanso ndi malonda ako.

34Koma tsopano wathyokera mʼnyanja,

pansi penipeni pa nyanja.

Katundu wako ndi onse amene anali nawe

amira pamodzi nawe.

35Onse amene amakhala mʼmbali mwa nyanja

aopsedwa ndi zimene zakuchitikira.

Mafumu awo akuchita mantha

ndipo nkhope zangoti khululu.

36Anthu amalonda a mitundu ina akukunyogodola.

Watha mochititsa mantha

ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.”