Zabbuli 94 – LCB & CCL

Luganda Contemporary Bible

Zabbuli 94:1-23

Zabbuli 94

194:1 a Nak 1:2; Bar 12:19 b Zab 80:1Ayi Mukama, ggwe Katonda awalana eggwanga,

ggwe Katonda awalana eggwanga, labika omasemase.

294:2 a Lub 18:25 b Zab 31:23Golokoka, Ayi ggwe Omulamuzi w’ensi,

osasule ab’amalala nga bwe kibagwanidde.

3Ayi Mukama, omukozi w’ebibi alikomya ddi?

Omukozi w’ebibi alituusa ddi ng’asanyuka?

494:4 a Zab 31:18 b Zab 52:1Bafukumula ebigambo eby’okwewaanawaana;

abakola ebibi bonna beepankapanka.

594:5 Is 3:15Babetenta abantu bo, Ayi Mukama,

babonyaabonya ezzadde lyo.

6Batta nnamwandu n’omutambuze;

ne batemula ataliiko kitaawe.

794:7 Yob 22:14; Zab 10:11Ne boogera nti, “Katonda talaba;

Katonda wa Yakobo tafaayo.”

894:8 Zab 92:6Mwerinde mmwe abantu abatategeera.

Mmwe abasirusiru muligeziwala ddi?

994:9 Kuv 4:11; Nge 20:12Oyo eyatonda okutu tawulira?

Oyo eyakola eriiso talaba?

1094:10 Yob 35:11; Is 28:26Oyo akangavvula amawanga, taakubonereze?

Oyo ayigiriza abantu talina ky’amanyi?

1194:11 1Ko 3:20*Mukama amanyi ebirowoozo by’abantu;

amanyi nga mukka bukka.

1294:12 a Yob 5:17; Beb 12:5 b Ma 8:3Ayi Mukama, alina omukisa oyo gw’ogunjula,

gw’oyigiriza eby’omu mateeka go;

1394:13 Zab 55:23omuwummuzaako mu kabi kaalimu,

okutuusa abakola ebibi lwe balisimirwa ekinnya.

1494:14 1Sa 12:22; Zab 37:28; Bar 11:2Kubanga Mukama talireka bantu be;

talyabulira zzadde lye.

1594:15 Zab 97:2Aliramula mu butuukirivu,

n’abo abalina emitima emigolokofu bwe banaakolanga.

1694:16 a Kbl 10:35; Zab 17:13 b Zab 59:2Ani alinnwanyisizaako abakola ebibi?

Ani alinnwanirira eri abakola ebibi?

1794:17 Zab 124:2Singa Mukama teyali mubeezi wange,

omwoyo gwange gwandiserengese emagombe.

1894:18 Zab 38:16Bwe naleekaana nti, “Nseerera!”

Okwagala kwo okutaggwaawo, Ayi Mukama, ne kumpanirira.

19Ebyeraliikiriza omutima gwange bwe byayitirira obungi,

okusaasira kwo ne kuzzaamu omwoyo gwange amaanyi.

2094:20 Zab 58:2Oyinza okukolagana n’obufuzi obukyamu,

obukaabya abantu n’amateeka gaabwe?

2194:21 a Zab 56:6 b Zab 106:38; Nge 17:15, 26Abakola ebibi beegatta ne balumbagana abatuukirivu;

atasobezza ne bamusalira ogw’okufa.

2294:22 Zab 18:2; 59:9Naye Mukama afuuse ekiddukiro kyange eky’amaanyi;

ye Katonda wange, era Olwazi lwange mwe neekweka.

2394:23 Zab 7:16Mukama alibabonereza olw’ebibi byabwe,

n’abazikiriza olw’ebyonoono byabwe;

Mukama Katonda waffe alibamalirawo ddala.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 94:1-23

Salimo 94

1Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango,

Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.

2Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi;

bwezerani kwa odzikuza zowayenera.

3Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova,

mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?

4Amakhuthula mawu onyada;

onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.

5Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova;

amapondereza cholowa chanu.

6Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko;

amapha ana amasiye.

7Iwo amati, “Yehova sakuona;

Mulungu wa Yakobo salabadirako.”

8Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu;

zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?

9Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva?

Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?

10Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga?

Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?

11Yehova amadziwa maganizo a munthu;

Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.

12Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza,

munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;

13mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto,

mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.

14Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake;

Iye sadzasiya cholowa chake.

15Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo,

ndipo onse olungama mtima adzachitsata.

16Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa?

Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?

17Yehova akanapanda kundithandiza,

bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.

18Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,”

chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.

19Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga,

chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.

20Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu

umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?

21Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama

ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.

22Koma Yehova wakhala linga langa,

ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.

23Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo

ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo;

Yehova Mulungu wathu adzawawononga.