Obadiya 1 – LCB & CCL

Luganda Contemporary Bible

Obadiya 1:1-21

11 a Is 63:1-6; Yer 49:7-22; Ez 25:12-14; Am 1:11-12 b Is 18:2 c Yer 6:4-5Kuno kwe kwolesebwa kwa Obadiya.

Mukama Ayinzabyonna kwe yamuwa ku bikwata ku nsi ya Edomu.

Tuwulidde obubaka obuva eri Katonda,

Katonda yaweereza omubaka eri amawanga n’obubaka buno nti,

“Mugolokoke tulumbe Edomu tumulwanyise.”

2“Laba, ndibafuula aba wansi ennyo mu mawanga,

era olinyoomererwa ddala.

33 a Is 16:6 b Is 14:13-15; Kub 18:7Mwelimbye n’amalala agali mu mitima gyammwe,

mmwe abasula mu mpuku ez’omu njazi,

era ne muzimba amaka gammwe waggulu ku njazi.

Mmwe aboogera nti,

‘Ani alituwanulayo n’atussa wansi?’

44 a Kbk 2:9 b Is 14:13 c Yob 20:6Wadde nga mwewanika waggulu ng’empungu

era ne muzimba ebisu byammwe wakati w’emmunyeenye,

ndibawanulayo ne mbasuula wansi,”

bw’ayogera Mukama.

55 Ma 24:21“Singa ababbi babajjira,

n’abanyazi ne babalumba ekiro,

akabi nga kaba kabatuuseeko.

Tebandibabbyeko byonna bye baagala?

Oba singa abanozi b’emizabbibu bakujjiridde,

tebandireseeko obuzabbibu butono nnyo?

6Esawu alinyagulurwa,

eby’obugagga bye ebikusike birinyagibwa.

77 a Yer 30:14 b Zab 41:9Abaalagaana naawe balikusindiikiriza ku nsalo,

Mikwano gyo balikulimbalimba ne bakuwangula;

abo abalya emmere yo balikutega omutego,

balikutega omutego kyokka toliguvumbula.

88 Yob 5:12; Is 29:14“Ku lunaku olwo,

sirizikiriza bagezi b’e Edomu,

abantu ab’amagezi ababeera mu nsozi za Esawu?” bw’ayogera Mukama.

99 Lub 36:11, 34“Abalwanyi bo abazira ggwe, Temani, balitya,

era na buli muntu mu nsozi za Esawu

alittibwa.

1010 a Yo 3:19 b Zab 137:7; Am 1:11-12 c Ez 35:9Olw’ebikolwa eby’obukambwe ebyo bye wakola muganda wo Yakobo,

oliswazibwa.

Olizikirizibwa n’otaddayo kuwulirwa.

1111 Nak 3:10Ku lunaku lwe wayimirira ku bbali n’otofaayo,

nga banyaga obugagga bwa Isirayiri,

ne bannaggwanga ne bayingira mu miryango gye,

ne bakuba obululu okulaba atwala Yerusaalemi,

wali omu ku bo.

1212 a Ez 35:15 b Nge 17:5 c Mi 4:11Tosaanye kusekerera muganda wo

mu biseera bye eby’okulaba ennaku,

wadde okusanyuka ku lunaku

olw’okuzikirira kw’abantu ba Yuda,

newaakubadde okwewaana ennyo

ku lunaku lwe baatawaanyizibwa ennyo.

1313 Ez 35:5Temukumba nga muyita mu miryango gy’abantu bange

ku lunaku kwe baalabira obuyinike,

wadde okubasekerera

ku lunaku kwe baabonaabonera,

newaakubadde okutwala obugagga bwabwe

ku lunaku lwe baatuukibwako akabi.

14Temulindira mu masaŋŋanzira

okutta abo abadduka,

wadde okuwaayo abawonyeewo

mu biro eby’okulabiramu ennaku.

1515 a Ez 30:3 b Yer 50:29; Kbk 2:8“Olunaku luli kumpi kwe ndisalira

amawanga gonna omusango.

Nga bwe mwakola abalala, nammwe bwe mulikolebwa.

Ebikolwa byammwe biribaddira.

1616 Yer 25:15; 49:12Ng’abantu bange bwe baanywa ekikompe eky’ekibonerezo ku lusozi lwange olutukuvu

n’amawanga ageetooloddewo bwe galikinywa obutakoma;

balikinywa,

babe ng’abataganywangako.

1717 a Am 9:11-15 b Is 4:3Naye ku Lusozi Sayuuni baliwona,

kubanga lutukuvu,

n’ennyumba ya Yakobo

eritwala omugabo gwabwe.

1818 Zek 12:6Ennyumba ya Yakobo eriba omuliro,

n’ennyumba ya Yusufu olulimi olw’omuliro.

Ennyumba ya Esawu eriba bisusunku,

era baligyokya n’eggwaawo.

Tewaliba muntu wa nnyumba ya Esawu

n’omu alisigalawo,

kubanga Mukama akyogedde.

1919 a Is 11:14 b Yer 31:5“Abantu b’e Negebu balitwala

olusozi Esawu,

n’abantu ab’omu biwonvu balitwala

ensi y’Abafirisuuti.

Balyetwalira n’ennimiro ez’omu Efulayimu ne Samaliya,

ne Benyamini ne yeetwalira Gireyaadi.

2020 a 1Bk 17:9-10 b Yer 33:13Ekibiina ky’Abayisirayiri abaali mu buwaŋŋanguse e Kanani,

balyetwalira ensi, okutuukira ddala ku Zalefaasi;

abawaŋŋanguse abaava mu Yerusaalemi abali mu Sefalaadi,

balyetwalira ebibuga mu Negebu.

2121 Zab 22:28; Zek 14:9, 16; Kub 11:15Abanunuzi balyambuka ku Lusozi Sayuuni,

okufuga ensozi za Esawu.

Obwakabaka buliba bwa Mukama.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Obadiya 1:1-21

Masomphenya a Obadiya

1Masomphenya a Obadiya.

Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti,

Tamva uthenga wochokera kwa Yehova:

Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti,

“Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”

2“Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina;

udzanyozedwa kwambiri.

3Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa,

iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe

ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali,

iwe amene umanena mu mtima mwako kuti,

‘Ndani anganditsitse pansi?’

4Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga

ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi,

ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,”

akutero Yehova.

5“Anthu akuba akanabwera kwa iwe,

kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku,

aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe!

Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha?

Ngati anthu othyola mphesa akanafika,

kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?

6Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse,

chuma chake chobisika chidzabedwa!

7Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire;

abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa;

amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha,

koma iwe sudzazindikira zimenezi.”

8Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo,

kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu,

anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?

9Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha,

ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau

adzaphedwa pa nkhondo.

10Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo,

udzakhala wamanyazi;

adzakuwononga mpaka muyaya.

11Pamene adani

ankamulanda chuma chake

pamene alendo analowa pa zipata zake

ndi kuchita maere pa Yerusalemu,

pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.

12Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako

pa nthawi ya tsoka lake,

kapena kunyogodola Ayuda

chifukwa cha chiwonongeko chawo,

kapena kuwaseka pa nthawi ya

mavuto awo.

13Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga

pa nthawi ya masautso awo,

kapena kuwanyogodola

pa tsiku la tsoka lawo,

kapena kulanda chuma chawo

pa nthawi ya masautso awo.

14Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu

kuti uphe Ayuda othawa,

kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka

pa nthawi ya mavuto awo.”

15“Tsiku la Yehova layandikira

limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu.

Adzakuchitira zomwe unawachitira ena;

zochita zako zidzakubwerera wekha.

16Iwe unamwa pa phiri langa loyera,

koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza;

iwo adzamwa ndi kudzandira

ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.

17Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso;

phirilo lidzakhala lopatulika,

ndipo nyumba ya Yakobo

idzalandira cholowa chake.

18Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto

ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto;

nyumba ya Esau idzasanduka chiputu,

ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza.

Sipadzakhala anthu opulumuka

kuchokera mʼnyumba ya Esau.”

Yehova wayankhula.

19Anthu ochokera ku Negevi adzakhala

ku mapiri a Esau,

ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri

adzatenga dziko la Afilisti.

Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya,

ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.

20Aisraeli amene ali ku ukapolo

adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati;

a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi

adzalandira mizinda ya ku Negevi.

21Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni

ndipo adzalamulira mapiri a Esau.

Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.