Koseya 14 – LCB & CCL

Luganda Contemporary Bible

Koseya 14:1-9

Okwenenya Kuleeta Omukisa

114:1 Kos 5:5Mudde eri Mukama Katonda wammwe, ggwe Isirayiri.

Ebibi byammwe bye bibaleetedde okugwa.

214:2 a Mi 7:18-19 b Beb 13:15Mudde eri Mukama

nga mwogera ebigambo bino nti,

“Tusonyiwe ebibi byaffe byonna,

otwanirize n’ekisa,

bwe tutyo tunaawaayo ebibala by’akamwa kaffe, ng’ebiweebwayo eby’ente ennume.

314:3 a Zab 33:17; Is 31:1 b Kos 8:6 c Zab 10:14; 68:5Obwasuli tebusobola kutulokola;

Tetujja kwebagala mbalaasi ez’omu ntalo.

Tetuliddayo kwogera nate nti, ‘Bakatonda baffe,’

nga twogera ku bintu bye twekoledde n’emikono gyaffe,

kubanga mu ggwe, bamulekwa mwe bajja okusaasirwa.”

414:4 a Kos 6:1 b Zef 3:17Ndibalekesaayo empisa zaabwe embi,

ne mbaagala awatali kye mbasalidde kya kusasula.

Kubanga obusungu bwange butanudde okubavaako.

514:5 a Lu 2:1 b Is 35:2 c Yob 29:19Ndifaanana ng’omusulo eri Isirayiri:

alimulisa ng’eddanga,

era alisimba emirandira ng’emivule gy’e Lebanooni.

614:6 a Zab 52:8; Yer 11:16 b Lu 4:11Amatabi ge amato galikula;

n’obulungi bwe buliba ng’omuzeyituuni,

n’akaloosa ke kaliba ng’akaloosa k’omuvule gw’e Lebanooni.

714:7 a Zab 91:1-4 b Kos 2:22 c Ez 17:23Abantu balibeera nate wansi w’ekisiikirize kye,

era alibala ng’emmere ey’empeke.

Alimulisa ng’omuzabbibu,

era alyatiikirira nga wayini ow’e Lebanooni.

814:8 nny 3Ggwe Efulayimu mugabo ki gwe nnina mu bakatonda bo?

Ndimwanukula ne mulabirira.

Nninga omuberosi omugimu, era n’ebibala byo biva mu nze.

914:9 a Zab 107:43 b Nge 10:29; Is 1:28 c Zab 111:7-8; Zef 3:5; Bik 13:10 d Is 26:7Abalina amagezi bategeera ensonga zino,

era abakabakaba balibimanya.

Amakuba ga Mukama matuufu,

n’abatuukirivu bagatambuliramu,

naye abajeemu bageesittaliramu.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 14:1-9

Kulapa Kubweretsa Madalitso

1Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako.

Machimo anu ndi amene akugwetsani!

2Bweretsani zopempha zanu

ndipo bwererani kwa Yehova.

Munene kwa Iye kuti,

“Tikhululukireni machimo athu onse

ndi kutilandira mokoma mtima,

kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.

3Asiriya sangatipulumutse;

ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo,

sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’

kwa zimene manja athu omwe anazipanga,

pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”

4Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo

ndipo ndidzawakonda mwaufulu

pakuti ndaleka kuwakwiyira.

5Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli

Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo.

Adzazika mizu yake pansi

ngati mkungudza wa ku Lebanoni;

6mphukira zake zidzakula.

Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi,

kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.

7Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake.

Iye adzakula bwino ngati tirigu.

Adzachita maluwa ngati mphesa

ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.

8Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano?

Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira.

Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira;

zipatso zako zimachokera kwa Ine.”

9Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi.

Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi.

Njira za Yehova ndi zolungama;

anthu olungama amayenda mʼmenemo,

koma anthu owukira amapunthwamo.