예레미야 47 – KLB & CCL

Korean Living Bible

예레미야 47:1-7

블레셋에 대한 심판

1이집트군이 가사를 공격하기 전에 여호와께서 나에게 블레셋 사람들 에 관해서

2다음과 같은 말씀을 주셨다. “보라, 북쪽에서 물이 일어나 홍수처럼 밀어닥쳐 블레셋 땅과 그 가운데 있는 모든 것과 그 성들과 거기에 사는 자들을 모조리 휩쓸어 버릴 것이다. 그때 사람들이 부르짖을 것이며 그 땅의 모든 주민들이 통곡할 것이다.

3달리는 말발굽 소리와 적 전차의 요란한 소리와 전차 바퀴의 덜거덩거리는 소리에 아버지가 손에 맥이 풀려 자식을 돌보지 못할 것이다.

4블레셋 사람들을 모조리 죽이고 두로와 시돈을 도와줄 모든 생존자들까지 파멸시킬 날이 왔다. 나 여호와가 47:4 히 ‘갑돌섬’크레테섬 출신의 남아 있는 모든 블레셋 사람들을 아주 없애 버리겠다.

5가사가 대머리가 되었고 아스글론이 멸망을 당했다. 47:5 또는 ‘그들의 골짜기에 남아 있는 자들아’남아 있는 아낙의 후손들아, 너희가 언제까지 너희 살을 베며 슬퍼하겠느냐?

6너희는 ‘여호와의 칼아, 네가 언제까지 쉬지 않겠느냐? 네 집에 들어가서 가만히 쉬어라’ 하고 말한다.

7그러나 나 여호와가 그렇게 하라고 명령하였으니 어떻게 그것이 쉬겠느냐? 아스글론과 해변가에 사는 자들을 치라고 내가 명령하였다.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 47:1-7

Uthenga Wonena za Afilisti

1Uthenga umene Yehova anamupatsa mneneri Yeremiya wonena za Afilisti, Farao asanathire nkhondo Gaza ndi uwu:

2Yehova akuti,

“Taonani mmene madzi akubwerera kuchokera kumpoto;

adzasanduka mtsinje wosefukira ndi a mkokomo.

Adzasefukira mʼdziko monse ndi kumiza chilichonse mʼmenemo,

mizinda ndi onse okhala mʼmenemo.

Anthu adzafuwula;

anthu onse okhala mʼdzikomo adzalira

3akadzamva mgugu wa ngʼombe zazimuna zothamanga,

phokoso la magaleta ake

ndi kulira kwa mikombero yake.

Makolo sadzatembenuka kuti athandize ana awo;

manja awo adzangoti khoba.

4Pakuti tsiku lafika

lowononga Afilisti onse

ndi kupha onse otsala,

onse amene akanatha kuthandiza Turo ndi Sidoni.

Yehova ali pafupi kuwononga Afilisti,

otsala ochokera ku zilumba za ku Kafitori.

5Anthu a ku Gaza ameta mipala;

anthu a ku Asikeloni akhala chete.

Inu otsala a ku chigwa,

mudzakhala mukudzichekacheka mpaka liti?

6“Mukulira kuti, ‘Aa, lupanga la Yehova,

kodi udzapumula liti?

Bwerera mʼmalo ako;

ukhale momwemo ndipo ukhale chete.’

7Koma lupangalo lidzapumula bwanji

pamene Yehova walilamulira

kuti lithire nkhondo

Asikeloni ndi anthu a mʼmbali mwa nyanja?”