시편 63 – KLB & CCL

Korean Living Bible

시편 63:1-11

하나님과 교제하는 기쁨

(다윗이 유다 광야에 있을 때 지은 시)

1하나님이시여,

주는 나의 하나님이십니다.

그래서 내가 간절히 주를 찾습니다.

물이 없어 메마르고 못 쓰게 된

이 땅에서

내 영혼이 주를 애타게 그리워하며

내 육체가 주를 사모합니다.

2내가 성소에서 주를 바라보고

주의 능력과 영광을 보았습니다.

3주의 한결같은 사랑이

생명보다 나으므로

내가 주를 찬양하겠습니다.

4내가 일평생 주께 감사하며

주의 이름으로

손을 들고 기도하겠습니다.

5내가 좋은 것으로

배불리 먹고 만족할 것이며

큰 기쁨으로

주를 찬양할 것입니다.

6내가 자리에 누울 때

주를 기억하며

밤새도록 주를 생각합니다.

7주께서 항상

나의 도움이 되셨으므로

내가 주의 날개 그늘에서

기뻐 노래합니다.

8내가 주를 가까이 따르므로

주의 오른손이 나를 붙드십니다.

9나를 죽이려 하는 자들은

땅 깊은 곳에 들어갈 것이며

10그들은 칼날에 죽음을 당하여

이리의 밥이 될 것이다.

11그러나 63:11 원문에는 ‘왕은’나는 하나님 안에서

즐거워하리라.

하나님의 이름으로

맹세하는 자들은

그를 자랑할 것이나

거짓말하는 자들은

말문이 막힐 것이다.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 63:1-11

Salimo 63

Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda.

1Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga,

moona mtima ine ndimakufunafunani;

moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu,

thupi langa likulakalaka inu,

mʼdziko lowuma ndi lotopetsa

kumene kulibe madzi.

2Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika

ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.

3Chifukwa chikondi chanu

ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.

4Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga,

ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.

5Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona.

Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.

6Pa bedi panga ndimakumbukira inu;

ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.

7Chifukwa ndinu thandizo langa,

ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.

8Moyo wanga umakangamira Inu;

dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.

9Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa;

adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.

10Iwo adzaperekedwa ku lupanga

ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.

11Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu;

onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo,

koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.