시편 1 – KLB & CCL

Korean Living Bible

시편 1:1-6

제 1 권

(1-41)

복 있는 사람

1복 있는 사람은

악한 자들의 말을 듣지 않고 죄인들을 본받지 않으며

1:1 암시됨.하나님을 조롱하는 자들과

어울리지 않고

2여호와의 율법을 즐거워하며

그 율법을 밤낮 묵상하는 자이다.

3그는 시냇가에 심은 나무가

철을 따라 과실을 맺고

그 잎이 마르지 않는 것처럼

하는 일마다 다 잘 될 것이다.

4그러나 악인들은 그렇지 않으니 그들은 바람에 나는

겨와 같을 뿐이다.

5그러므로 악인들이

심판 날에 무사하지 못하고

죄인들이 의로운 자들 가운데

서지 못할 것이다.

6의로운 사람의 길은

여호와께서 지키시나

악인의 길은 파멸에 이를 것이다.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 1:1-6

BUKU LOYAMBA

Masalimo 1–41

Salimo 1

1Wodala munthu

amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa,

kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa,

kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.

2Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova

ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.

3Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,

umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake

ndipo masamba ake safota.

Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.

4Sizitero ndi anthu oyipa!

Iwo ali ngati mungu

umene umawuluzidwa ndi mphepo.

5Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo,

kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.

6Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama,

koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.