민수기 1 – KLB & CCL

Korean Living Bible

민수기 1:1-54

이스라엘의 첫 인구 조사

1이스라엘 백성이 이집트를 떠난 지 2년째가 되는 해 2월 일에 여호와께서 시 나이 광야 성막에서 모세에게 말씀하셨다.

2-4“너희는 이스라엘의 각 지파와 집안별 로 20세 이상 된 남자로서 전쟁에 나가 싸울 수 있는 사람이 몇 명이나 되는지 조사하여라. 너와 아론은 각 지파에서 선출된 지도자들의 도움을 받아 직접 그 인구 조사를 실시해야 한다.

5너희를 도와줄 각 지파의 지도자들은 다음과 같다:

르우벤 지파에서

스데울의 아들 엘리술,

6시므온 지파에서

수리삿대의 아들 슬루미엘,

7유다 지파에서

암미나답의 아들 나손,

8잇사갈 지파에서

수알의 아들 느다넬,

9스불론 지파에서

헬론의 아들 엘리압,

10요셉 자손 중에서는

에브라임 지파에서

암미훗의 아들 엘리사마,

므낫세 지파에서

브다술의 아들 가말리엘,

11베냐민 지파에서

기드오니의 아들 아비단,

12단 지파에서

암미삿대의 아들 아히에셀,

13아셀 지파에서

오그란의 아들 바기엘,

14갓 지파에서

드우엘의 아들 엘리아삽,

15납달리 지파에서

에난의 아들 아히라이다.”

16이들은 모두 이스라엘 백성 가운데서 선출된 각 지파의 지도자들이었다.

17-19그 날에 모세와 아론과 각 지파 지도자 들은 20세 이상의 이스라엘 모든 남자들을 소집하여 자기 소속 지파와 집안별로 등록하게 하였다. 이 모든 일은 여호와께서 모세에게 명령하신 대로 실시되었다.

20전쟁에 나가 싸울 수 있는 20세 이상 등록된 이스라엘 남자들의 수는 각 지파별로 다음과 같다:

21야곱의 맏아들 르우벤 지파에서 46,500명22-23시므온 지파에서 59,300명24-25갓 지파에서 45,650명26-27유다 지파에서 74,600명28-29잇사갈 지파에서 54,400명30-31스불론 지파에서 57,400명32-33에브라임 지파에서 40,500명34-35므낫세 지파에서 32,200명36-37베냐민 지파에서 35,400명38-39단 지파에서 62,700명40-41아셀 지파에서 41,500명42-43납달리 지파에서 53,400명

44-46모두 603,550명이었다.

47그러나 이 총인원에는 레위인이 포함되지 않았다.

48그것은 여호와께서 모세에게 이렇게 말씀하셨기 때문이다.

49“레위 지파는 한 사람도 징집 명단에 포함시키지 말고

501:50 또는 ‘증거막’성막과 그 모든 비품을 관리하게 하라. 그들은 성막과 그 모든 기구를 운반하고 성막 주변에 살면서 봉사하게 하라.

51성막을 다른 곳으로 옮길 때에는 레위인들이 그것을 걷고 세워야 한다. 그 외에 다른 사람이 이 성막에 접근하면 처형시켜라.

52그리고 이스라엘의 각 지파는 자기 지파의 기를 가지고 지파별로 지역을 정하여 천막을 쳐야 한다.

53그러나 레위인들은 성막 주위에 천막을 쳐서 이스라엘 백성에게 나 여호와의 진노가 내리지 않게 하라. 이와 같이 레위인들은 성막을 지키는 책임을 져야 한다.”

54그래서 이스라엘 백성은 여호와께서 모세에게 명령하신 대로 하였다.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 1:1-54

Kalembera

1Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti, 2“Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi. 3Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali. 4Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi. 5Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa:

Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,

6Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,

7Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,

8Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,

9Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,

10Mwa ana a Yosefe:

kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi;

kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;

11Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,

12Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,

13Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,

14Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,

15Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”

16Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.

17Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa, 18ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi 19monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:

20Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 21Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.

22Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 23Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.

24Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 25Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.

26Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 27Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.

28Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 29Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.

30Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 31Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.

32Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe:

Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 33Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.

34Kuchokera mwa zidzukulu za Manase:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 35Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.

36Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 37Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.

38Kuchokera mwa zidzukulu za Dani:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 39Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.

40Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 41Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.

42Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali:

Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 43Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.

44Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake. 45Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo. 46Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.

47Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena. 48Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, 49“Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli. 50Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo. 51Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa. 52Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake. 53Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”

54Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.