雅歌 5 – JCB & CCL

Japanese Contemporary Bible

雅歌 5:1-16

5

ソロモン王

1いとしい花嫁よ。さあ私は、自分の庭園にやって来た。

私は没薬と香料を集め、

はちの巣からみつを取って食べ、

ぶどう酒とミルクを飲んでいる。」

エルサレムの娘たち

「愛する方たちよ、食べて飲んでください。

十分に飲んでください。」

おとめ

2ある夜のことです。眠っているとき、

夢の中で愛する方の声が聞こえました。

あの方は、私の寝室のドアをたたいていました。

『いとしい人、私の恋人、私のかわいい鳩よ、

開けておくれ。

夜通し外にいたので、すっかり露にぬれてしまった。』

3私は答えました。

『もう寝間着を着てしまったのに、

また着替えるのですか。

足も洗ったので汚したくありません。』

4それでも、愛する方が

鍵を開けようとするのを見て気の毒になり、

5私は跳び起きて、ドアを開けました。

かんぬきの取っ手を引いたとき、

私の手から香水が、指からかぐわしい没薬の液が

したたり落ちました。

6ところが、せっかくお開けしたのに、

もうあの方の姿は見えません。

私は心臓の止まる思いでした。

どんなにあちこち捜しても、

あの方は見当たらないのです。

必死にお呼びしても返事はありません。

7私は警備の人に見つかり、たたかれました。

城壁の見張りにはベールをはぎ取られました。

8エルサレムの娘さん、どうか誓ってください。

私の愛する方を見かけたら、

私が恋の病をわずらっていると伝えてほしいのです。」

エルサレムの娘たち

9女性の中で一番美しい人よ。

私たちにそれほどまでに頼み込む

だれよりもすてきな人とはどんなお方ですか。」

おとめ

10私の愛する方は日焼けして魅力的で、

ほかのどの男の方よりすてきです。

11頭は純金、

黒い髪はウェーブがかかっています。

12目は流れのほとりにいる鳩のようで、

穏やかに輝き、深く澄んでいます。

13頬はかぐわしい香料の花壇、

くちびるはゆりの花、息は没薬のようです。

14腕はトパーズをはめ込んだ丸い金の棒。

体は宝石をちりばめた光沢のある象牙。

15足は純金の台座にすえられた大理石のようで、

レバノン杉のようにたくましいのです。

あの方にまさる人はいません。

16あの方のことばは、うっとりするほどです。

あの方のすべてがすてきなのです。

エルサレムの娘さん。

これが私の愛する方、私の恋人です。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 5:1-16

Mwamuna

1Ndalowa mʼmunda mwanga, iwe mlongo wanga, iwe mkwatibwi wanga;

ndasonkhanitsa mure wanga ndi zokometsera zakudya zanga.

Ndadya uchi wanga pamodzi ndi zisa zake zomwe;

ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga.

Abwenzi

Idyani abwenzi anga, imwani;

Inu okondana, imwani kwambiri.

Mkazi

2Ndinagona tulo koma mtima wanga unali maso.

Tamverani, bwenzi langa akugogoda:

“Nditsekulire, mlongo wanga, bwenzi langa,

nkhunda yanga, wangwiro wanga.

Mutu wanga wanyowa ndi mame,

tsitsi langa lanyowa chifukwa cha nkhungu ya usiku.”

3Ndavula kale zovala zanga,

kodi ndizivalenso?

Ndasamba kale mapazi anga

kodi ndiwadetsenso?

4Bwenzi langa anapisa dzanja lake pa chibowo cha pa chitseko;

mtima wanga unagunda chifukwa cha iye.

5Ndinanyamuka kukamutsekulira wachikondi wangayo,

ndipo manja anga anali noninoni ndi mure,

zala zanga zinali mure chuchuchu,

pa zogwirira za chotsekera.

6Ndinamutsekulira wachikondi wanga,

koma nʼkuti wachikondi wangayo atachoka; iye anali atapita.

Mtima wanga unafumuka chifukwa cha kuchoka kwake.

Ndinamuyangʼanayangʼana koma sindinamupeze.

Ndinamuyitana koma sanandiyankhe.

7Alonda anandipeza

pamene ankayendera mzindawo.

Anandimenya ndipo anandipweteka;

iwo anandilanda mwinjiro wanga,

alonda a pa khoma aja!

8Inu akazi a ku Yerusalemu ndithu ndikukupemphani,

mukapeza wokondedwa wangayo,

kodi mudzamuwuza chiyani?

Muwuzeni kuti ine ndadwala nacho chikondi.

Abwenzi

9Iwe wokongola kuposa akazi onsewa,

kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana wina aliyense bwanji?

Kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana ena onse chotani

kuti uzichita kutipempha motere?

Mkazi

10Wokondedwa wangayo ndi wowala kwambiri ndi wathanzi

pakati pa anthu 1,000.

11Mutu wake ndi golide woyengeka bwino;

tsitsi lake ndi lopotanapotana,

ndiponso lakuda bwino ngati khwangwala.

12Maso ake ali ngati nkhunda

mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,

ngati nkhunda zitasamba mu mkaka,

zitayima ngati miyala yamtengowapatali.

13Masaya ake ali ngati timinda ta mbewu zokometsera zakudya

zopatsa fungo lokoma.

Milomo yake ili ngati maluwa okongola

amene akuchucha mure.

14Manja ake ali ngati ndodo zagolide

zokongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali.

Thupi lake ndi losalala ngati mnyanga wanjovu

woyikamo miyala ya safiro.

15Miyendo yake ili ngati mizati yamwala,

yokhazikika pa maziko a golide.

Maonekedwe ake ali ngati Lebanoni,

abwino kwambiri ngati mkungudza.

16Milomo yake ndi yosangalatsa kwambiri;

munthuyo ndi wokongola kwambiri!

Uyu ndiye wachikondi wanga ndi bwenzi langa,

inu akazi a ku Yerusalemu.