詩篇 143 – JCB & CCL

Japanese Contemporary Bible

詩篇 143:1-12

143

1主よ、私の祈りを聞き、願いに答えてください。

あなたは、約束を決して破らないお方です。

2私を裁判にかけないでください。

あなたほど完全なお方はいないのですから。

3私は敵に追いつめられ、地面にたたきつけられました。

そして、墓のように暗い所に住まわせられたのです。

4いっさいの希望を失った私は、

恐怖に取りつかれ、身震いしています。

5私はあなたがかつてなさった

すばらしい奇跡の数々を思い出しています。

6乾ききった地が雨を慕うように、

私はあなたに両手を差し伸べています。

7主よ、すぐにもこの祈りに答えてください。

悩みはますます深刻になります。

どうか見放さないでください。

そうでなければ、私は死んでしまいます。

8朝になったら、あなたの恵みを見せてください。

あなたを支えとして生きている私に、

どの道を選ぶべきか教えてください。

私は心の底から祈っているのですから。

9主よ、敵からお救いください。

私はあなたのふところに飛び込んで危険を避けます。

10あなたは私の神ですから、

ご意志にそった行動をとらせてください。

恵み深い御霊によって、

私を祝福の道へと導いてください。

11主よ。私をお救いくだされば、

ご威光はひときわ明るく輝くでしょう。

あなたは約束を守ってくださるお方ですから、

どうか、私をいっさいの苦しみから

引き上げてください。

12私を愛してくださる恵み深い神よ。

すべての敵を根絶やしにし、

危害を加えようとする者どもを滅ぼしてください。

私はあなたに仕えるしもべなのですから。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 143:1-12

Salimo 143

Salimo la Davide.

1Yehova imvani pemphero langa,

mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo;

mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu

bwerani kudzandithandiza.

2Musazenge mlandu mtumiki wanu,

pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.

3Mdani akundithamangitsa,

iye wandipondereza pansi;

wachititsa kuti ndikhale mu mdima

ngati munthu amene anafa kale.

4Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga;

mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.

5Ndimakumbukira masiku amakedzana;

ndimalingalira za ntchito yanu yonse,

ndimaganizira zimene manja anu anachita.

6Ndatambalitsa manja anga kwa Inu;

moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma.

Sela

7Yehova ndiyankheni msanga;

mzimu wanga ukufowoka.

Musandibisire nkhope yanu,

mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.

8Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika,

pakuti ine ndimadalira Inu.

Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo,

pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.

9Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova,

pakuti ndimabisala mwa Inu.

10Phunzitseni kuchita chifuniro chanu,

popeza ndinu Mulungu wanga;

Mzimu wanu wabwino unditsogolere

pa njira yanu yosalala.

11Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu;

mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.

12Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga;

wonongani adani anga,

pakuti ndine mtumiki wanu.