詩篇 141 – JCB & CCL

Japanese Contemporary Bible

詩篇 141:1-10

141

1主よ、どうか早く、私の祈りに答えてください。

助けを呼び求める声を聞いてください。

2私の祈りが、夕方の供え物となり、

あなたの前に立ち上る香となりますように。

3主よ、どうか、この口を堅く閉じ、

くちびるに封をさせてください。

4悪に走る汚れた心を取り除いてください。

罪人の仲間入りをして、

彼らのごちそうにありつこうなどと

思うことのないようにしてください。

5神を敬う人からのきびしい忠告は、

私を思う心から出たものです。

非難されたように感じても、

私にとって薬となるのです。

私が彼らの非難を拒絶することがありませんように。

私は、悪者どもには警戒を怠らず、

彼らの悪行に対抗して絶えず祈ります。

6-7悪者どもの指導者たちが罰を受け、

その骨が地にばらまかれるなら、

彼らは初めて私のことばに注意をはらい、

今まで、私が彼らを助けようとしていたことに

気づくでしょう。

8私の主よ。私はあなたを見つめ、

いつ助けてくださるかと待っています。

あなたは私の隠れ家ですから、

彼らに手出しをさせないでください。

9彼らの罠に近づけないでください。

10その罠には彼ら自身がかかり、

私は難を免れることができますように。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 141:1-10

Salimo 141

Salimo la Davide.

1Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine.

Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.

2Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani;

kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.

3Yehova ikani mlonda pakamwa panga;

londerani khomo la pa milomo yanga.

4Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa;

kuchita ntchito zonyansa

pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa;

musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.

5Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo;

andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga.

Mutu wanga sudzakana zimenezi.

Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.

6Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri,

ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.

7Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza,

ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.”

8Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse;

ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.

9Mundipulumutse ku misampha imene anditchera,

ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.

10Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo,

mpaka ine nditadutsa mwamtendere.