Zekariya 2 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 2:1-13

Munthu ndi Chingwe Choyezera

1Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona munthu atanyamula chingwe choyezera mʼmanja mwake. 2Ndipo ndinafunsa kuti, “Kodi ukupita kuti?”

Anandiyankha kuti, “Akukayeza Yerusalemu kuti ndidziwe mulifupi mwake ndi mulitali mwake.”

3Taonani, mngelo amene amayankhula nane uja akuchoka, mngelo wina anabwera kudzakumana naye 4ndipo anamuwuza kuti, “Thamanga, kamuwuze mnyamatayo kuti, ‘Yerusalemu udzakhala mzinda wopanda malinga chifukwa mudzakhala anthu ambiri ndiponso ziweto zochuluka. 5Ndipo Ine mwini ndidzakhala linga lamoto kuteteza mzindawo,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakhala ulemerero mʼkati mwake.’

6“Tulukani! Tulukani! Thawaniko ku dziko la kumpoto,” akutero Yehova, “pakuti ndinakumwazirani ku mphepo zinayi zamlengalenga,” akutero Yehova.

7“Tuluka, iwe Ziyoni! Thawa, iwe amene umakhala mʼdziko la mwana wamkazi wa Babuloni!” 8Pakuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Atatha kundilemekeza wanditumiza kwa anthu a mitundu ina amene anakufunkhani; pakuti aliyense wokhudza inu wakhudza mwanadiso wanga. 9Ndithu Ine ndidzawamenya anthuwo ndi dzanja langa ndipo amene anali akapolo awo ndiye adzawalande zinthu. Pamenepo mudzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye wandituma.

10“Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, fuwula ndipo sangalala. Pakuti taona ndikubwera, ndipo ndidzakhala pakati pako,” akutero Yehova. 11“Nthawi imeneyo anthu a mitundu yambiri adzabwera kwa Yehova ndipo adzasanduka anthu anga. Ndidzakhala pakati pako ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe. 12Yehova adzachititsa kuti Yuda akhale chuma chake mʼdziko lopatulika ndipo adzasankhanso Yerusalemu. 13Khalani chete pamaso pa Yehova anthu nonse, chifukwa Iye wavumbuluka kuchoka ku malo ake opatulika.”

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Zacarías 2:1-13

El hombre con el cordel de medir

1Alcé la vista, ¡y vi ante mí un hombre que tenía en la mano un cordel de medir! 2Le pregunté: «¿A dónde vas?» Y él me respondió: «Voy a medir Jerusalén. Quiero ver cuánto mide de ancho y cuánto de largo».

3Ya salía el ángel que hablaba conmigo cuando otro ángel vino a su encuentro 4y le dijo: «Corre a decirle a ese joven:

»“Tanta gente habrá en Jerusalén,

y tanto ganado,

que Jerusalén llegará a ser

una ciudad sin muros.

5En torno suyo —afirma el Señor

seré un muro de fuego,

y dentro de ella

seré su gloria”.

6»¡Salid, salid!

¡Huid del país del norte!

—afirma el Señor—.

»¡Fui yo quien os dispersó

por los cuatro vientos del cielo!

—afirma el Señor—.

7»Sión, tú que habitas en Babilonia, ¡sal de allí; escápate!» 8Porque así dice el Señor Todopoderoso, cuya gloria me envió contra las naciones que os saquearon:

«La nación que toca a mi pueblo,

toca la niña de mis ojos.

9Yo agitaré mi mano contra esa nación,

y sus propios esclavos la saquearán.

»Así sabréis que me ha enviado el Señor Todopoderoso.

10»¡Grita de alegría, hija de Sión!

¡Yo vengo a habitar en medio de ti!

—afirma el Señor—.

11»En aquel día,

muchas naciones se unirán al Señor.

Ellas serán mi pueblo,

y yo habitaré entre ellas.

»Así sabréis que el Señor Todopoderoso es quien me ha enviado a vosotros. 12El Señor tomará posesión de Judá, su porción en tierra santa, y de nuevo escogerá a Jerusalén. 13¡Que todo el mundo guarde silencio ante el Señor, que ya avanza desde su santa morada!»