Zekariya 2 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 2:1-13

Munthu ndi Chingwe Choyezera

1Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona munthu atanyamula chingwe choyezera mʼmanja mwake. 2Ndipo ndinafunsa kuti, “Kodi ukupita kuti?”

Anandiyankha kuti, “Akukayeza Yerusalemu kuti ndidziwe mulifupi mwake ndi mulitali mwake.”

3Taonani, mngelo amene amayankhula nane uja akuchoka, mngelo wina anabwera kudzakumana naye 4ndipo anamuwuza kuti, “Thamanga, kamuwuze mnyamatayo kuti, ‘Yerusalemu udzakhala mzinda wopanda malinga chifukwa mudzakhala anthu ambiri ndiponso ziweto zochuluka. 5Ndipo Ine mwini ndidzakhala linga lamoto kuteteza mzindawo,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakhala ulemerero mʼkati mwake.’

6“Tulukani! Tulukani! Thawaniko ku dziko la kumpoto,” akutero Yehova, “pakuti ndinakumwazirani ku mphepo zinayi zamlengalenga,” akutero Yehova.

7“Tuluka, iwe Ziyoni! Thawa, iwe amene umakhala mʼdziko la mwana wamkazi wa Babuloni!” 8Pakuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Atatha kundilemekeza wanditumiza kwa anthu a mitundu ina amene anakufunkhani; pakuti aliyense wokhudza inu wakhudza mwanadiso wanga. 9Ndithu Ine ndidzawamenya anthuwo ndi dzanja langa ndipo amene anali akapolo awo ndiye adzawalande zinthu. Pamenepo mudzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye wandituma.

10“Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, fuwula ndipo sangalala. Pakuti taona ndikubwera, ndipo ndidzakhala pakati pako,” akutero Yehova. 11“Nthawi imeneyo anthu a mitundu yambiri adzabwera kwa Yehova ndipo adzasanduka anthu anga. Ndidzakhala pakati pako ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe. 12Yehova adzachititsa kuti Yuda akhale chuma chake mʼdziko lopatulika ndipo adzasankhanso Yerusalemu. 13Khalani chete pamaso pa Yehova anthu nonse, chifukwa Iye wavumbuluka kuchoka ku malo ake opatulika.”

La Bible du Semeur

Zacharie 2:1-17

Les cornes et les quatre forgerons

1Je levai les yeux et je vis quatre cornes2.1 Voir Dn 7.8.. 2Je demandai à l’ange qui me parlait : Que représentent ces cornes ?

Et il me répondit : Ces cornes représentent les puissances qui ont dispersé les habitants de Juda, d’Israël et de Jérusalem.

3Puis l’Eternel me fit voir quatre forgerons.

4– Que viennent-ils faire ? demandai-je.

Il me répondit : Ils sont venus pour faire trembler les nations qui ont dispersé Juda, de sorte que personne n’osait plus relever la tête. Ils abattront les cornes de ces nations qui ont levé leurs cornes contre Juda pour en disperser la population.

L’arpenteur

5Je regardai et je vis un homme qui portait un cordeau d’arpenteur. 6Je lui demandai : Où vas-tu ?

Il me répondit : Je vais mesurer Jérusalem pour en déterminer la largeur et la longueur.

7Comme l’ange qui me parlait s’en allait, un autre ange vint à sa rencontre 8et lui dit : Cours dire à ce jeune homme là-bas2.8 C’est-à-dire à celui qui voulait mesurer la ville. : « Il y aura un jour tant d’habitants et de bêtes dans Jérusalem que la ville restera ouverte, sans murailles. 9Je serai, moi-même, pour elle comme une muraille de feu tout autour d’elle – l’Eternel le déclare – et je serai sa gloire au milieu d’elle. »

10Allons ! Allons ! Fuyez ! Partez de ce pays du Nord2.10 De la Babylonie (v. 11). – l’Eternel le déclare – car je vous avais dispersés aux quatre vents du ciel2.10 C’est-à-dire aux quatre points cardinaux., l’Eternel le déclare. 11Allons, Sion ! Echappe-toi, toi qui es installée dans la cité de Babylone ! 12Car voici ce que dit le Seigneur des armées célestes, lui qui m’a envoyé avec autorité2.12 lui qui m’a envoyé avec autorité. Autre traduction : après que la gloire m’eut envoyé., au sujet des nations qui vous ont dépouillés : Celui qui touche à vous, c’est comme s’il touchait à la prunelle de mon œil. 13Oui, je lèverai la main contre elles, elles seront pillées par leurs esclaves, et vous saurez que l’Eternel, le Seigneur des armées célestes, m’a envoyé.

14Pousse des cris de joie et sois dans l’allégresse, communauté de Sion, car je viens habiter au milieu de toi, l’Eternel le déclare. 15En ce jour-là, beaucoup de gens des peuples non israélites s’attacheront à l’Eternel et deviendront mon peuple. Et je demeurerai au milieu de vous, et vous saurez que l’Eternel, le Seigneur des armées célestes, m’a envoyé vers vous. 16Et l’Eternel fera de Juda son domaine, son patrimoine, sur la terre sacrée2.16 Autre traduction : du saint., et il choisira de nouveau la ville de Jérusalem. 17Que, devant l’Eternel, toutes les créatures fassent silence, car le voici qui se réveille et sort de sa demeure sainte.