Zekariya 14 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 14:1-21

Yehova Akubwera ndipo Akulamulira

1Taonani tsiku la Yehova likubwera pamene zinthu zimene adani ako anakulanda azidzagawana iwe ukuona.

2Ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse kuti adzathire nkhondo Yerusalemu; mzindawu udzalandidwa, nyumba zidzaphwasulidwa, ndipo akazi adzagwiriridwa. Theka la anthu a mu mzindamu lidzapita ku ukapolo, koma ena onse otsala mu mzindamu sadzachotsedwa.

3Pamenepo Yehova adzabwera kudzamenyana ndi mitundu ya anthu imeneyi, ngati mmene amachitira pa nthawi ya nkhondo. 4Tsiku limenelo adzayimirira pa Phiri la Olivi, kummawa kwa Yerusalemu, ndipo Phiri la Olivilo lidzagawikana pawiri kuyambira kummawa mpaka kumadzulo, kupanga chigwa chachikulu, kuchititsa kuti theka la phiri lisunthire kumpoto ndi linalo kummwera. 5Inu mudzathawa podzera mʼchigwa chapakati pa phirilo, pakuti chidzafika mpaka ku Azeli. Mudzathawa monga munachitira pa tsiku la chivomerezi nthawi ya Uziya mfumu ya Yuda. Kenaka Yehova Mulungu wanga adzabwera, pamodzi ndi oyera ake onse.

6Tsiku limenelo sipadzakhala kuwala, kuzizira kapena chisanu. 7Lidzakhala tsiku lapaderadera, silidzakhala usana kapena usiku; tsiku limeneli akulidziwa ndi Yehova yekha. Ikadzafika nthawi ya madzulo, kudzakhala kukuwalabe.

8Tsiku limenelo madzi amoyo adzatuluka mu Yerusalemu, theka lidzapita ku nyanja ya kummawa ndipo theka lina ku nyanja ya kumadzulo, nthawi yachilimwe ndi nthawi yozizira yomwe.

9Ndipo Yehova adzakhala mfumu pa dziko lonse lapansi. Tsiku limenelo padzakhala Ambuye mmodzi yekha, ndipo dzina lidzakhala limodzi lomwelo.

10Dziko lonse, kuyambira ku Geba mpaka ku Rimoni, kummwera kwa Yerusalemu, lidzakhala ngati Araba. Koma Yerusalemu adzakwezedwa ndipo adzakhala pamalo pakepo, kuyambira ku Chipata cha Benjamini mpaka ku malo amene ali ku Chipata Choyamba, ku Chipata Chapangodya, ndipo kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku malo opsinyira mphesa za mfumu. 11Mʼmenemo mudzakhala anthu; sadzawonongedwanso. Yerusalemu adzakhala pa mtendere.

12Mliri umene Yehova adzakanthire nawo mitundu yonse ya anthu imene inkamenyana ndi Yerusalemu ndi uwu: Matupi awo adzawola iwo eni akuyenda, maso awo adzawola ali mʼmalo mwake, ndipo malilime awo adzawola ali mʼkamwa mwawo. 13Pa tsiku limenelo Yehova adzasokoneza anthu akuluakulu. Munthu aliyense adzagwira dzanja la mnzake, ndi kuyamba kumenyana okhaokha. 14Yuda nayenso adzachita nkhondo ku Yerusalemu. Chuma chonse cha anthu a mitundu yozungulira adzachisonkhanitsa pamodzi; golide, siliva ndi zovala zochuluka kwambiri. 15Mliri womwewo udzapha akavalo ndi nyulu, ngamira ndi abulu, pamodzi ndi nyama zonse zokhala ku misasako.

16Kenaka opulumuka ochokera mwa mitundu yonse ya anthu amene anathira nkhondo Yerusalemu, azidzapita chaka ndi chaka kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, ndiponso kukachita Chikondwerero cha Misasa. 17Ngati mitundu ina ya anthu pa dziko lapansi sidzapita ku Yerusalemu kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, idzakhala wopanda mvula. 18Ndipo ngati anthu a ku Igupto sadzapita ndi kukakhala nawo kumeneko, adzakhala wopanda mvula. Yehova adzabweretsa pa iwo mliri umene analangira mitundu ina ya anthu imene sinapite ku Chikondwerero cha Misasa. 19Chimenechi chidzakhala chilango cha Igupto ndiponso mitundu ina yonse imene sidzapita ku Chikondwerero cha Misasa.

20Pa tsiku limenelo pa maberu a akavalo padzalembedwa mawu oti wopatulikira Yehova, ndipo miphika ya mʼNyumba ya Yehova idzakhala yopatulika ngati mbale za ku guwa. 21Mʼphika uliwonse ku Yerusalemu ndi ku Yuda udzakhala wopatulikira Yehova Wamphamvuzonse, ndipo onse amene adzabwera kudzapereka nsembe adzatenga miphika ina ndi kuphikiramo. Ndipo nthawi imeneyo simudzakhalanso Akanaani mʼNyumba ya Yehova Wamphamvuzonse.

Thai New Contemporary Bible

เศคาริยาห์ 14:1-21

องค์พระผู้เป็นเจ้า

1วันแห่งองค์พระผู้เป็นเจ้าใกล้จะมาถึงแล้วเมื่อพวกเจ้าแบ่งของที่ริบมาได้ในหมู่พวกเจ้า

2เราจะรวบรวมประชาชาติทั้งมวลมาสู้รบกับเยรูซาเล็ม กรุงนั้นจะถูกยึด บ้านเรือนถูกปล้น ข้าวของถูกริบ พวกผู้หญิงถูกข่มขืน ประชาชนครึ่งเมืองถูกจับไปเป็นเชลย ส่วนที่เหลือจะยังคงอยู่ในกรุงนั้น

3แล้วองค์พระผู้เป็นเจ้าจะเสด็จมาสู้รบกับชนชาติเหล่านั้นเหมือนในยามศึก 4ในวันนั้นพระองค์จะทรงวางพระบาทบนภูเขามะกอกเทศ ทางตะวันออกของกรุงเยรูซาเล็ม และภูเขามะกอกเทศจะแยกออกเป็นสองส่วน จากตะวันออกถึงตะวันตก ทำให้เกิดหุบเขาที่กว้างใหญ่ โดยครึ่งหนึ่งของภูเขาจะเคลื่อนไปทางเหนือ อีกครึ่งหนึ่งเคลื่อนไปทางใต้ 5เจ้าจะหนีไปทางหุบเขาของเรา เพราะมันจะทอดยาวไปถึงอาเซล เจ้าจะหนีเหมือนเมื่อหนีจากแผ่นดินไหว14:5 หรือ 5หุบเขาของเราจะถูกปิดกั้น และจะทอดยาวไปถึงอาเซล มันจะถูกปิดกั้นเหมือนอย่างที่มันเคยถูกปิดกั้นเพราะแผ่นดินไหวในสมัยกษัตริย์อุสซียาห์แห่งยูดาห์ แล้วพระยาห์เวห์พระเจ้าของข้าพเจ้าจะเสด็จมาพร้อมผู้บริสุทธิ์ทั้งปวงซึ่งอยู่กับพระองค์

6ในวันนั้นจะไม่มีความสว่าง ความหนาวเย็น หรือน้ำค้างแข็ง 7จะเป็นวันพิเศษ ไม่มีกลางวันหรือกลางคืน องค์พระผู้เป็นเจ้าเท่านั้นทรงทราบ แม้เมื่อตกเย็นก็จะมีแสงสว่าง

8ในวันนั้นน้ำแห่งชีวิตจะไหลออกมาจากเยรูซาเล็ม ครึ่งหนึ่งไหลลงทะเลตายทางตะวันออก อีกครึ่งหนึ่งไหลลงทะเลเมดิเตอร์เรเนียนทางตะวันตก ไหลตลอดทั้งในฤดูร้อนและฤดูหนาว

9องค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงเป็นกษัตริย์ครองทั้งโลก ในวันนั้นจะมีองค์พระผู้เป็นเจ้าเพียงพระองค์เดียวและมีพระนามของพระองค์เพียงพระนามเดียวเท่านั้น

10ทั่วทั้งแผ่นดินจากเกบาถึงริมโมนทางใต้ของเยรูซาเล็มจะเป็นเหมือนอาราบาห์ ส่วนเยรูซาเล็มจะสูงเด่น มันจะคงอยู่ในที่ของมัน จากประตูเบนยามินถึงบริเวณประตูที่หนึ่งถึงประตูมุม และจากหอคอยฮานันเอลถึงบ่อย่ำองุ่นหลวง 11เยรูซาเล็มจะมีผู้คนอาศัยอยู่ มันจะมั่นคงปลอดภัยและไม่ถูกทำลายล้างอีกต่อไป

12ภัยพิบัติที่องค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงให้เกิดแก่บรรดาประชาชาติที่มาสู้รบกับเยรูซาเล็มมีดังนี้คือ เนื้อของเขาจะเปื่อยเน่าทั้งที่ยังยืนอยู่ ตาของเขาเน่าคากระบอกตา และลิ้นเปื่อยเน่าอยู่ในปาก 13ในวันนั้นองค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงบันดาลให้ผู้คนโกลาหลอลหม่าน แต่ละคนจะจับมือของอีกคนแล้วสู้กัน 14ชาวยูดาห์ก็จะไปสู้รบที่เยรูซาเล็มด้วย พวกเขาจะเก็บรวบรวมทรัพย์สมบัติของทุกชนชาติที่อยู่รายรอบ ได้ทั้งเงินทองและเสื้อผ้ามากมาย 15ภัยพิบัติคล้ายคลึงกันจะเกิดกับม้า ล่อ อูฐ ลา และสัตว์ทั้งปวงในค่ายเหล่านั้น

16แล้วบรรดาผู้รอดชีวิตจากประชาชาติทั้งปวงที่มาโจมตีเยรูซาเล็มจะขึ้นไปเยรูซาเล็มทุกปี เพื่อนมัสการองค์กษัตริย์พระยาห์เวห์ผู้ทรงฤทธิ์ และเพื่อฉลองเทศกาลอยู่เพิง 17ชนชาติใดๆ ทั่วโลกที่ไม่ไปนมัสการองค์กษัตริย์พระยาห์เวห์ผู้ทรงฤทธิ์ พวกเขาจะไม่ได้รับฝน 18หากชาวอียิปต์ไม่ยอมขึ้นมาร่วม เขาจะไม่ได้รับฝน องค์พระผู้เป็นเจ้า14:18 หรือมาร่วม แล้วองค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงบันดาลภัยพิบัติให้เกิดแก่อียิปต์ เป็นภัยพิบัติอย่างเดียวกับที่ทรงให้เกิดแก่ประชาชาติที่ไม่ขึ้นไปร่วมฉลองเทศกาลอยู่เพิง 19นี่เป็นการลงโทษอียิปต์และประชาชาติทั้งปวงซึ่งไม่ขึ้นไปร่วมฉลองเทศกาลอยู่เพิง

20ในวันนั้นลูกพรวนที่ตัวม้าจะมีข้อความจารึกว่า “บริสุทธิ์แด่องค์พระผู้เป็นเจ้า” และหม้อหุงต้มในพระวิหารขององค์พระผู้เป็นเจ้าจะเป็นเหมือนภาชนะศักดิ์สิทธิ์หน้าแท่นบูชา 21หม้อทุกใบในเยรูซาเล็มและยูดาห์จะบริสุทธิ์แด่พระยาห์เวห์ผู้ทรงฤทธิ์ และคนทั้งปวงที่มาถวายเครื่องบูชาจะหยิบหม้อบางใบไปใช้ในการต้มเครื่องบูชาได้ และในวันนั้นจะไม่มีชาวคานาอัน14:21 หรือพ่อค้าในพระนิเวศของพระยาห์เวห์ผู้ทรงฤทธิ์อีกต่อไป