Zekariya 11 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 11:1-17

1Tsekula zitseko zako, iwe Lebanoni,

kuti moto unyeketse mikungudza yako!

2Lira mwachisoni, iwe mtengo wa payini, pakuti mkungudza wagwa;

mtengo wamphamvu wawonongeka!

Lirani mwachisoni, inu mitengo ya thundu ya Basani;

nkhalango yowirira yadulidwa!

3Imvani kulira mwachisoni kwa abusa;

msipu wawo wobiriwira wawonongeka!

Imvani kubangula kwa mikango;

nkhalango yowirira ya ku Yorodani yawonongeka!

Abusa Awiri

4Yehova Mulungu wanga akuti, “Dyetsa nkhosa zimene zikukaphedwa. 5Amene amagula nkhosazo amazipha ndipo salangidwa. Amene amazigulitsa amanena kuti, ‘Alemekezeke Yehova, ine ndalemera!’ Abusa ake omwe sazimvera chisoni nkhosazo. 6Pakuti Ine sindidzamveranso chisoni anthu okhala mʼdziko,” akutero Yehova. “Ndidzapereka munthu aliyense mʼmanja mwa mnansi wake ndi mwa mfumu yake. Iwo adzazunza dziko, ndipo Ine sindidzawapulumutsa mʼmanja mwawo.”

7Choncho ine ndinadyetsa nkhosa zokaphedwa, makamaka nkhosa zoponderezedwa. Pamenepo ndinatenga ndodo ziwiri ndipo yoyamba ndinayitcha Kukoma mtima ndipo yachiwiri ndinayitcha Umodzi ndipo ndinadyetsa nkhosazo. 8Pa mwezi umodzi ndinachotsa abusa atatu.

Abusawo anadana nane, ndipo ndinatopa nawo. 9Ndinawuza gulu la nkhosalo kuti, “Sindidzakhalanso mʼbusa wanu. Imene ikufa, ife, ndipo imene ikuwonongeka, iwonongeke, zimene zatsala zizidyana.”

10Kenaka ndinatenga ndodo yanga yotchedwa Kukoma mtima ndi kuyithyola, kuphwanya pangano limene ndinachita ndi mitundu yonse ya anthu. 11Linaphwanyidwa tsiku limenelo ndipo nkhosa zosautsidwa zimene zimandiyangʼanitsitsa zinadziwa kuti anali mawu a Yehova.

12Ndinawawuza kuti, “Ngati mukuganiza kuti zili bwino, patseni malipiro anga; koma ngati si choncho, sungani malipirowo.” Kotero anandipatsa ndalama zasiliva makumi atatu.

13Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ziponye kwa wowumba mbiya,” mtengo woyenera umene anapereka pondigula Ine! Choncho ndinatenga ndalama zasiliva makumi atatu ndi kuziponya mʼnyumba ya Yehova kwa wowumba mbiya.

14Kenaka ndinathyola ndodo yanga yachiwiri yotchedwa Umodzi, kuthetsa ubale pakati pa Yuda ndi Israeli.

15Pamenepo Yehova anayankhula nane kuti, “Tenganso zida za mʼbusa wopusa. 16Pakuti ndidzawutsa mʼbusa mʼdzikomo amene sadzasamalira zotayika, kapena kufunafuna zazingʼono, kapena zovulala, kapena kudyetsa nkhosa zabwino, koma iye adzadya nyama ya nkhosa zonenepa, nʼkumakukuta ndi ziboda zomwe.

17“Tsoka kwa mʼbusa wopandapake,

amene amasiya nkhosa!

Lupanga limukanthe pa mkono wake ndi pa diso lake lakumanja!

Mkono wake ufote kotheratu,

diso lake lamanja lisaonenso.”

King James Version

Zechariah 11:1-17

1Open thy doors, O Lebanon, that the fire may devour thy cedars. 2Howl, fir tree; for the cedar is fallen; because the mighty are spoiled: howl, O ye oaks of Bashan; for the forest of the vintage is come down.11.2 mighty: or, gallants11.2 the forest…: or, the defenced forest

3There is a voice of the howling of the shepherds; for their glory is spoiled: a voice of the roaring of young lions; for the pride of Jordan is spoiled.

4Thus saith the LORD my God; Feed the flock of the slaughter; 5Whose possessors slay them, and hold themselves not guilty: and they that sell them say, Blessed be the LORD; for I am rich: and their own shepherds pity them not. 6For I will no more pity the inhabitants of the land, saith the LORD: but, lo, I will deliver the men every one into his neighbour’s hand, and into the hand of his king: and they shall smite the land, and out of their hand I will not deliver them.11.6 deliver: Heb. make to be found 7And I will feed the flock of slaughter, even you, O poor of the flock. And I took unto me two staves; the one I called Beauty, and the other I called Bands; and I fed the flock.11.7 even…: or, verily the poor11.7 Bands: or, Binders 8Three shepherds also I cut off in one month; and my soul lothed them, and their soul also abhorred me.11.8 lothed…: Heb. was straightened for them 9Then said I, I will not feed you: that that dieth, let it die; and that that is to be cut off, let it be cut off; and let the rest eat every one the flesh of another.11.9 another: Heb. his fellow, or, neighbour

10¶ And I took my staff, even Beauty, and cut it asunder, that I might break my covenant which I had made with all the people. 11And it was broken in that day: and so the poor of the flock that waited upon me knew that it was the word of the LORD.11.11 so…: or, the poor of the flock, etc. certainly knew 12And I said unto them, If ye think good, give me my price; and if not, forbear. So they weighed for my price thirty pieces of silver.11.12 If ye…: Heb. If it be good in your eyes 13And the LORD said unto me, Cast it unto the potter: a goodly price that I was prised at of them. And I took the thirty pieces of silver, and cast them to the potter in the house of the LORD. 14Then I cut asunder mine other staff, even Bands, that I might break the brotherhood between Judah and Israel.11.14 Bands: or, Binders

15¶ And the LORD said unto me, Take unto thee yet the instruments of a foolish shepherd. 16For, lo, I will raise up a shepherd in the land, which shall not visit those that be cut off, neither shall seek the young one, nor heal that that is broken, nor feed that that standeth still: but he shall eat the flesh of the fat, and tear their claws in pieces.11.16 cut off: or, hidden11.16 feed: or, bear 17Woe to the idol shepherd that leaveth the flock! the sword shall be upon his arm, and upon his right eye: his arm shall be clean dried up, and his right eye shall be utterly darkened.