Zekariya 1 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 1:1-21

Yuda Abwerera kwa Yehova

1Mwezi wachisanu ndi chitatu, mʼchaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi mneneri Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido, kuti:

2“Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu. 3Choncho awuze anthuwa kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Bwererani kwa Ine,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. 4Musakhale ngati makolo anu, amene aneneri akale anawalalikira kuti: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Tsopano lekani njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu oyipawo.’ Koma iwo sanamvere kapena kulabadira za Ine, akutero Yehova. 5Kodi makolo anuwo ali kuti tsopano? Nanga aneneri, kodi amakhalapo mpaka muyaya? 6Kodi mawu anga ndi malangizo anga, amene ndinawawuza atumiki anga aneneri, suja anawachitira makolo anu?

“Tsono iwo analapa ndi kunena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse watichitira zomwe zikuyenera njira zathu ndi machitidwe athu, monga anatsimikiza kuti adzachita.’ ”

Munthu Pakati pa Mitengo ya Mchisu

7Tsiku la 24 la mwezi wa 11, mwezi wa Sebati, chaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido.

8Nthawi ya usiku ndinaona masomphenya. Ndinaona munthu atakwera pa kavalo wofiira. Iye anayima pakati pa mitengo ya mchisu mʼchigwa. Kumbuyo kwake kunali akavalo ofiira, akhofi ndi oyera.

9Ine ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, kodi zimenezi ndi chiyani?”

Mngelo amene amayankhula nane anayankha kuti, “Ndidzakuonetsa kuti zimenezi ndi chiyani.”

10Pamenepo munthu amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu anafotokoza kuti, “Amenewa ndiwo amene Yehova wawatuma kuti ayendere dziko lonse lapansi.”

11Ndipo okwera pa akavalo enawo anafotokoza kwa mngelo wa Yehova, amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu kuti, “Ife tayendera dziko lonse lapansi ndipo tapeza kuti dziko lonselo lili pa bata ndi mtendere.”

12Tsono mngelo wa Yehova anati, “Yehova Wamphamvuzonse, kodi mpaka liti mudzakhala osaonetsa chifundo chanu kwa Yerusalemu ndi mizinda ya Yuda, amene mwawakwiyira kwa zaka izi 70?” 13Choncho Yehova anayankhula mawu abwino ndi achitonthozo kwa mngelo amene ankayankhula nane.

14Pamenepo mngelo amene ankayankhula nane anati, “Lengeza mawu awa: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndikuchitira nsanje Yerusalemu ndi Ziyoni, 15koma ndakwiya kwambiri ndi anthu a mitundu ina amene akuganiza kuti ali pa mtendere. Ndinakwiyira anthu anga pangʼono pokha, koma iwo anawonjeza kuzunza anthu angawo.’

16“Choncho, Yehova akuti, ‘Ndidzabwerera ku Yerusalemu ndi mtima wachifundo, nyumba yanga adzayimanganso kumeneko. Ndipo adzatenganso chingwe choyezera kuti amange Yerusalemu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.

17“Lengezanso kuti, Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Mizinda yanga idzakhalanso ndi zokoma zosefukira ndipo Yehova adzatonthoza Ziyoni ndi kusankhanso Yerusalemu.’ ”

Nyanga Zinayi ndi Amisiri Azitsulo Anayi

18Kenaka ndinayangʼananso, ndipo patsogolo panga panali nyanga zinayi. 19Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi ndi chiyani?”

Iye anandiyankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda, Israeli ndi Yerusalemu.”

20Kenaka Yehova anandionetsa amisiri azitsulo anayi. 21Ndinafunsa kuti, “Amisiri a zitsulowa akudzachita chiyani?”

Iye anayankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda kotero kuti panalibe wina amene akanalimbana nazo, koma amisiri a zitsulowa abwera kudzaziopseza ndi kugwetsa nyanga zimenezi za mitundu ya anthu amene analimbana ndi dziko la Yuda ndi kubalalitsa anthu ake.”

Thai New Contemporary Bible

เศคาริยาห์ 1:1-21

เรียกร้องให้กลับมาหาองค์พระผู้เป็นเจ้า

1ในเดือนที่แปดของปีที่สองแห่งรัชกาลดาริอัส พระดำรัสขององค์พระผู้เป็นเจ้ามาถึงผู้เผยพระวจนะเศคาริยาห์บุตรเบเรคิยาห์บุตรอิดโดว่า

2องค์พระผู้เป็นเจ้าทรงพระพิโรธบรรพบุรุษของพวกเจ้ายิ่งนัก 3ฉะนั้นจงบอกเหล่าประชากรดังนี้ว่า พระยาห์เวห์ผู้ทรงฤทธิ์ตรัสว่า ‘จงกลับมาหาเรา’ พระยาห์เวห์ผู้ทรงฤทธิ์ประกาศว่า ‘แล้วเราจะกลับมาหาพวกเจ้า’ พระยาห์เวห์ผู้ทรงฤทธิ์ตรัสดังนั้น 4อย่าเป็นเหมือนบรรพบุรุษของพวกเจ้า ซึ่งบรรดาผู้เผยพระวจนะแต่ก่อนเคยประกาศดังนี้ว่า พระยาห์เวห์ผู้ทรงฤทธิ์ตรัสว่า ‘จงหันจากวิถีและความประพฤติอันชั่วช้าของพวกเจ้า’ แต่พวกเขาไม่ได้ฟังหรือใส่ใจเราเลย องค์พระผู้เป็นเจ้าประกาศดังนั้น 5บัดนี้บรรพบุรุษของพวกเจ้าไปไหนเสียแล้ว? และบรรดาผู้เผยพระวจนะมีชีวิตยืนยงตลอดกาลหรือ? 6แต่ถ้อยคำและกฎหมายซึ่งเราสั่งเหล่าผู้เผยพระวจนะผู้รับใช้ของเราก็เป็นจริงกับบรรพบุรุษของพวกเจ้าไม่ใช่หรือ?

“แล้วเขาเหล่านั้นก็สำนึกผิดและกล่าวว่า ‘พระยาห์เวห์ผู้ทรงฤทธิ์ทรงทำกับเราอย่างสาสมกับวิถีและความประพฤติของเราตามที่พระองค์ทรงตัดสินพระทัยไว้แล้ว’ ”

ชายผู้อยู่ท่ามกลางต้นน้ำมันเขียว

7ในวันที่ยี่สิบสี่เดือนเชบัท คือเดือนที่สิบเอ็ดของปีที่สองแห่งรัชกาลดาริอัส พระดำรัสขององค์พระผู้เป็นเจ้ามาถึงผู้เผยพระวจนะเศคาริยาห์บุตรเบเรคิยาห์บุตรอิดโด

8ยามค่ำคืนข้าพเจ้าเห็นนิมิตตรงหน้าข้าพเจ้า มีชายคนหนึ่งขี่ม้าสีแดง! เขายืนอยู่ในหมู่ต้นน้ำมันเขียวในลำห้วย ข้างหลังเขามีม้าสีแดง ม้าสีน้ำตาล และม้าสีขาว

9ข้าพเจ้าถามว่า “ท่านเจ้าข้า สิ่งเหล่านี้คืออะไร?”

ทูตสวรรค์ที่สนทนากับข้าพเจ้าตอบว่า “เราจะแสดงให้เจ้าเห็นว่าคืออะไร”

10แล้วชายคนที่ยืนในหมู่ต้นน้ำมันเขียวอธิบายว่า “พวกเขาคือผู้ที่องค์พระผู้เป็นเจ้าทรงส่งไปทั่วโลก”

11แล้วพวกเขามารายงานทูตสวรรค์ขององค์พระผู้เป็นเจ้าซึ่งยืนอยู่กลางหมู่ต้นน้ำมันเขียวว่า “เราได้ไปทั่วโลก และพบว่าทั่วโลกก็พักสงบอยู่”

12แล้วทูตขององค์พระผู้เป็นเจ้ากล่าวว่า “ข้าแต่พระยาห์เวห์ผู้ทรงฤทธิ์ พระองค์จะทรงยับยั้งพระเมตตาจากเยรูซาเล็มและหัวเมืองต่างๆ ของยูดาห์ไปนานสักเท่าใด? ทรงพระพิโรธมาเจ็ดสิบปีแล้ว” 13ดังนั้นองค์พระผู้เป็นเจ้าจึงตรัสถ้อยคำที่อ่อนโยนและถ้อยคำปลอบใจกับทูตสวรรค์นั้นซึ่งสนทนากับข้าพเจ้า

14แล้วทูตสวรรค์ที่สนทนากับข้าพเจ้าจึงกล่าวว่า “จงประกาศถ้อยคำเหล่านี้ พระยาห์เวห์ผู้ทรงฤทธิ์ตรัสว่า ‘เราหวงแหนเยรูซาเล็มและศิโยน 15แต่เราโกรธยิ่งนักที่ชนชาติต่างๆ รู้สึกมั่นคงปลอดภัย เราโกรธนิดเดียว แต่พวกเขาทำให้ย่อยยับเกินขนาด’

16“ฉะนั้นองค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสว่า ‘เราจะหันกลับมาหาเยรูซาเล็มด้วยความเมตตา และพระนิเวศของเราจะถูกสร้างขึ้นมาใหม่ที่นั่น และสายวัดจะถูกดึงออกวัดทั่วเยรูซาเล็ม’ พระยาห์เวห์ผู้ทรงฤทธิ์ประกาศดังนั้น

17“จงประกาศต่อไปว่า พระยาห์เวห์ผู้ทรงฤทธิ์ตรัสว่า ‘เมืองต่างๆ ของเราจะเจริญรุ่งเรืองอย่างล้นเหลืออีกครั้ง และองค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงปลอบโยนศิโยนและเลือกสรรเยรูซาเล็มอีกครั้ง’ ”

เขาสัตว์สี่อันและช่างฝีมือสี่คน

18แล้วข้าพเจ้าเงยหน้า เห็นเขาสัตว์สี่อันอยู่ตรงหน้า! 19ข้าพเจ้าจึงถามทูตสวรรค์ที่สนทนากับข้าพเจ้าว่า “สิ่งเหล่านี้คืออะไร?”

เขาตอบว่า “สิ่งเหล่านี้คือเขาสัตว์ซึ่งทำให้ยูดาห์ อิสราเอล และเยรูซาเล็มกระจัดกระจาย”

20แล้วองค์พระผู้เป็นเจ้าทรงสำแดงให้ข้าพเจ้าเห็นช่างฝีมือสี่คน 21ข้าพเจ้าจึงถามว่า “คนเหล่านี้มาทำอะไร?”

เขาตอบว่า “สิ่งเหล่านี้คือเขาสัตว์ซึ่งทำให้ยูดาห์กระจัดกระจายจนไม่มีใครโงหัวขึ้นมาได้ แต่ช่างฝีมือเหล่านี้มาเพื่อทำให้เขาสัตว์ทั้งหลายหวาดกลัว และทำลายเขาสัตว์ของประชาชาติทั้งหลายที่ได้ชูเขาของตนขึ้น ทำให้ประชากรยูดาห์กระจัดกระจายไป”