Yuda 1 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yuda 1:1-25

1Ndine Yuda, mtumiki wa Yesu Khristu, komanso mʼbale wake wa Yakobo.

Kwa inu amene Mulungu Atate anakuyitanani, amene amakukondani ndikukusungani mwa Yesu Khristu.

2Chifundo, mtendere ndi chikondi zikhale nanu mochuluka.

Tchimo ndi Kuwonongeka kwa Osapembedza

3Okondedwa, ngakhale ndinkafunitsitsa kukulemberani za chipulumutso cha tonsefe, ndakakamizidwa kuti ndikulembereni ndi kukupemphani kolimba kuti mumenye ndithu nkhondo yotchinjiriza chikhulupiriro chimene Mulungu anachipereka kamodzi kokha kwa anthu onse oyera mtima. 4Pakuti anthu ena amene za chilango chawo zinalembedwa kale, alowa mobisika pakati panu. Amenewa ndi anthu osapembedza Mulungu, amene amapotoza chisomo cha Mulungu wathu kuchisandutsa ufulu ochitira zonyansa ndiponso amakana Yesu Khristu amene Iye ndiye Mbuye ndi Mfumu yathu.

5Ngakhale munazidziwa kale zonsezi, ndafuna kuti ndikukumbutseni kuti Ambuye anapulumutsa anthu ake ndi kuwatulutsa mʼdziko la Igupto, koma pambuyo pake anawononga amene sanakhulupirire. 6Ndipo mukumbukire angelo amene sanakhutire ndi maudindo awo, koma anasiya malo awo. Angelo amenewa Mulungu anawamanga ndi maunyolo osatha, ndipo akuwasunga mʼmalo a mdima mpaka tsiku lalikulu lachiweruzo. 7Musayiwale mizinda ya Sodomu ndi Gomora ija, ndi mizinda yoyandikana nayo. Anthu mʼmenemo anadziperekanso kuchita zadama ndi kuchita zonyansa zachilendo. Mizinda imeneyi yakhala ngati chitsanzo cha amene adzalangidwa ndi moto wosatha.

8Nʼchimodzimodzinso zimene akuchita anthu amenewa potsata maloto awo, amadetsa matupi awo, amakana ulamuliro wa Mulungu ndiponso amachitira chipongwe angelo akumwamba. 9Koma ngakhale mkulu wa angelo Mikayeli, pamene ankalimbana ndi Mdierekezi za mtembo wa Mose, sanamunene kuti wachipongwe, koma anati, “Ambuye akudzudzule iwe!” 10Koma anthu awa amachita chipongwe zinthu zimene sakuzidziwa. Ndipo zinthu zimene amazidziwa ndi nzeru zachibadwa, monga za nyama, ndizo zimene zimawawononga.

11Tsoka kwa iwo chifukwa anatsatira njira ya Kaini. Iwo athamangira phindu, nʼchifukwa chake anagwa mʼtchimo la Baalamu. Iwo anawonongedwa chifukwa chowukira monga anachitira Kora.

12Anthu amenewa ndiwo amayipitsa maphwando anu achikondi. Amadya nanu mopanda manyazi ndipo ali ngati abusa amene amangodzidyetsa okha. Anthuwa ali ngati mitambo yowuluzika ndi mphepo, yopanda mvula. Ali ngati mitengo ya nthawi ya masika, yopanda zipatso, yozuka mizu, mitengo yoferatu. 13Iwowa ali ngati mafunde awukali apanyanja, amene amatulutsa thovu la zonyansa zawo. Amenewa ali ngati nyenyezi zosochera, ndipo Mulungu akuwasungira mdima wandiweyani mpaka muyaya.

14Enoki, wachisanu ndi chiwiri kuyambira pa Adamu, ananeneratu za anthu amenewa kuti, “Onani, Ambuye akubwera ndi oyera ake osawerengeka 15kuti adzaweruze aliyense, ndi kudzagamula kuti onse osapembedza ndi olakwa, chifukwa cha ntchito zawo zosalungama zimene anachita mʼmoyo wawo osaopa Mulungu. Adzawatsutsa chifukwa cha mawu onse achipongwe amene osapembedzawa ananyoza nawo Ambuye.” 16Anthu amenewa amangʼungʼudza ndi kudandaula. Amatsatira zilakolako zawo zoyipa. Amayankhula zodzitamandira ndipo amanamiza ena pofuna kupeza phindu.

Awalimbikitsa kuti Apirire

17Koma okondedwa, kumbukirani zimene atumwi a Ambuye athu Yesu Khristu ananeneratu. 18Iwo anakuwuzani kuti, “Mʼmasiku otsiriza kudzafika anthu onyoza, otsatira zofuna zawo zoyipa.” 19Anthu amenewa ndi amene akubweretsa mipatuko pakati panu, amatsatira nzeru zachibadwa ndipo alibe Mzimu Woyera.

20Koma inu okondedwa, muthandizane kuti mukule pa chikhulupiriro chanu choyera, ndipo muzipemphera ndi mphamvu ya Mzimu Woyera. 21Khalani mʼchikondi cha Mulungu pamene mukudikira chifundo cha Ambuye athu Yesu Khristu kuti akubweretsereni moyo wosatha.

22Muwachitire chifundo amene akukayika. 23Ena muwapulumutse powalanditsa ku moto. Enanso muwachitire chifundo, koma mwa mantha, ndipo muzidana ngakhale ndi mwinjiro yomwe yayipitsidwa ndi machimo.

Mawu Olemekeza Mulungu

24Kwa Iye amene angathe kukusungani kuti mungagwe mʼmachimo, ndiponso amene angathenso kukufikitsani pamaso pake pa ulemerero wopanda cholakwa muli okondwa, 25kwa Mulungu yekhayo, Mpulumutsi wathu, kwa Iye kukhale ulemerero, ukulu, mphamvu ndi ulamuliro, mwa Yesu Khristu Ambuye athu, kuyambira isanayambe nthawi, tsopano mpaka muyaya. Ameni.

Thai New Contemporary Bible

ยูดา 1:1-25

1จดหมายฉบับนี้จากข้าพเจ้ายูดาผู้เป็นผู้รับใช้ของพระเยซูคริสต์และเป็นน้องชายของยากอบ

ถึงบรรดาผู้ที่ทรงเรียกซึ่งเป็นที่รักของพระเจ้าพระบิดาและได้รับการปกป้องไว้โดย1:1 หรือเพื่อหรือในพระเยซูคริสต์

2ขอพระเมตตา สันติสุข และความรักมีแก่ท่านทั้งหลายอย่างล้นเหลือ

บาปและความพินาศของคนอธรรม

3เพื่อนที่รักทั้งหลาย แม้ข้าพเจ้ากระตือรือร้นอย่างยิ่งที่จะเขียนถึงท่านเกี่ยวกับความรอดที่เรามีร่วมกัน ข้าพเจ้าก็รู้สึกว่าจำเป็นต้องเขียนมาให้กำลังใจท่านให้ต่อสู้เพื่อความเชื่อซึ่งได้ทรงมอบหมายแก่ประชากรของพระเจ้าเพียงครั้งเดียวเป็นพอ 4เนื่องจากมีบางคนได้แอบแฝงเข้ามาในหมู่พวกท่าน คำพิพากษาของคนพวกนี้ได้ถูกบันทึก1:4 หรือคนพวกนี้ถูกกำหนดให้รับคำพิพากษา ไว้นานแล้ว พวกเขาเป็นคนอธรรมไม่ยำเกรงพระเจ้า พลิกผันพระคุณของพระองค์มาเป็นใบเบิกทางให้ทำผิดศีลธรรม และปฏิเสธพระเยซูคริสต์ผู้ทรงเป็นองค์เจ้าชีวิตและเป็นองค์พระผู้เป็นเจ้าแต่ผู้เดียวของเรา

5แม้ท่านทราบความทั้งสิ้นนี้แล้ว ข้าพเจ้าก็ยังอยากเตือนให้ท่านระลึกว่าองค์พระผู้เป็นเจ้า1:5 สำเนาต้นฉบับบางสำเนาว่าพระเยซู ทรงปลดปล่อยประชากรของพระองค์ออกจากอียิปต์ แต่ต่อมาก็ทรงทำลายบรรดาผู้ที่ไม่เชื่อ 6และเหล่าทูตสวรรค์ที่ไม่พอใจในอำนาจหน้าที่ซึ่งพระเจ้าประทาน แต่ได้ละทิ้งถิ่นที่อยู่ของตนเอง พระองค์ได้ทรงกักขังทูตสวรรค์เหล่านี้ไว้ในที่มืด ล่ามด้วยโซ่อันเป็นนิรันดร์เพื่อรอการพิพากษาในวันอันยิ่งใหญ่นั้น 7เช่นเดียวกัน เมืองโสโดม เมืองโกโมราห์ และเมืองต่างๆ โดยรอบได้ปล่อยตัวมัวเมาทำผิดศีลธรรมทางเพศและกามวิปริต พวกนี้เป็นตัวอย่างของบรรดาผู้ที่จะรับโทษในไฟนิรันดร์

8พวกเพ้อฝันเหล่านี้ก็เป็นแบบเดียวกันไม่มีผิด เขาปล่อยตัวแปดเปื้อน ปฏิเสธสิทธิอำนาจ กล่าวสบประมาทเทพเบื้องบน 9แม้แต่เทพบดีมีคาเอล เมื่อโต้แย้งกับมารเรื่องศพของโมเสสก็ยังไม่กล้าล่วงเกินกล่าวหามารเลย พูดเพียงว่า “ให้องค์พระผู้เป็นเจ้าทรงจัดการกับเจ้า!” 10กระนั้นคนเหล่านี้ก็กล่าวจาบจ้วงล่วงเกินสิ่งที่ตนไม่เข้าใจและสิ่งที่เขาเข้าใจโดยสัญชาตญาณเยี่ยงเดรัจฉานที่ไม่รู้จักใช้เหตุผล สิ่งเหล่านี้เองที่ทำลายล้างพวกเขา

11วิบัติแก่พวกเขา! เขาได้ดำเนินตามแนวทางของคาอิน เขาได้ทุ่มตัวเข้าสู่ความผิดพลาดของบาลาอัมเพราะเห็นแก่ได้ เขาจะถูกทำลายล้างไปเหมือนอย่างการกบฏของโคราห์

12คนเหล่านี้เป็นรอยด่างพร้อยในงานเลี้ยงแห่งความรักของท่าน พวกเขาร่วมกินดื่มกับท่านอย่างตะกละตะกลามโดยไม่เกรงกลัวแม้แต่น้อย เป็นเหมือนคนเลี้ยงแกะที่เลี้ยงแต่ตัวเอง เขาเป็นเมฆไร้ฝนที่ลอยไปตามลม เป็นต้นไม้ที่ไม่ให้ผลตามฤดูกาลและถูกถอนรากถอนโคนตายซ้ำสอง 13เขาเป็นคลื่นคะนองในทะเลที่ซัดความน่าอับอายของตนเป็นฟองฟู่ เขาเป็นดาวที่เตลิดจากวงโคจร ความมืดมิดได้ถูกสงวนไว้ให้เขาตลอดกาล

14เอโนคซึ่งเป็นคนในชั่วอายุที่เจ็ดนับจากอาดัมได้พยากรณ์เกี่ยวกับคนเหล่านี้ไว้ว่า “ดูเถิด องค์พระผู้เป็นเจ้ากำลังเสด็จมาพร้อมด้วยผู้บริสุทธิ์นับแสนนับล้านของพระองค์ 15เพื่อพิพากษาทุกคนและเพื่อให้คนอธรรมทั้งปวงสำนึกในการอธรรมทั้งสิ้นที่ได้ทำไปตามแนวทางอธรรม และสำนึกในคำจาบจ้วงที่คนบาปคนอธรรมได้กล่าวร้ายพระองค์” 16คนเหล่านี้มักพร่ำบ่นและชอบจับผิด เขาทำตามตัณหาชั่วของตน เขายกตนเองและประจบสอพลอคนอื่นเพื่อหาประโยชน์ใส่ตัว

เรียกร้องให้มานะอดทน

17แต่เพื่อนที่รักทั้งหลาย จงระลึกถึงสิ่งที่เหล่าอัครทูตขององค์พระเยซูคริสต์เจ้าของเราได้บอกไว้ล่วงหน้า 18พวกเขากล่าวกับท่านว่า “ในยุคสุดท้ายจะมีคนชอบเยาะเย้ยซึ่งทำตามตัณหาชั่วของตนเอง” 19คนเหล่านี้ทำให้พวกท่านแตกแยกกัน เขาทำตามสัญชาตญาณเท่านั้นและไม่มีพระวิญญาณ

20ส่วนท่านเพื่อนที่รักทั้งหลาย จงเสริมสร้างกันขึ้นในความเชื่ออันบริสุทธิ์ที่ท่านมีอยู่ และจงอธิษฐานในพระวิญญาณบริสุทธิ์ 21จงรักษาตัวไว้ในความรักของพระเจ้าขณะที่ท่านรอคอยพระเมตตาของพระเยซูคริสต์เจ้าของเราให้นำท่านไปสู่ชีวิตนิรันดร์

22จงสำแดงความเมตตาแก่ผู้ที่สงสัย 23จงฉุดผู้อื่นออกมาจากไฟและช่วยพวกเขาให้รอด จงสำแดงความเมตตาแก่ผู้อื่น แต่จงกลัวที่จะเป็นมลทิน คือจงรังเกียจแม้แต่เสื้อผ้าที่แปดเปื้อนด้วยโลกีย์

บทสดุดี

24แด่พระองค์ผู้ทรงสามารถคุ้มครองไม่ให้ท่านล้มลง และนำท่านเข้าสู่เบื้องพระพักตร์อันเปี่ยมด้วยพระเกียรติสิริอย่างปราศจากตำหนิและด้วยความชื่นชมยินดีอย่างใหญ่หลวง 25คือแด่พระเจ้าองค์เดียวผู้ทรงเป็นพระผู้ช่วยให้รอดของเรา ขอพระเกียรติสิริ พระบารมี เดชานุภาพ และอำนาจมีแด่พระองค์โดยทางพระเยซูคริสต์องค์พระผู้เป็นเจ้าของเรา แด่พระเจ้าผู้ทรงดำรงตลอดมาทุกยุค ในอดีต ในปัจจุบัน และสืบๆ ไปเป็นนิตย์! อาเมน