Yoweli 3 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoweli 3:1-21

Kuweruzidwa kwa Mitundu ya Anthu

1“Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo,

nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,

2ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse

ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati.

Kumeneko ndidzawaweruza

chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli,

pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu

ndikugawa dziko langa.

3Anagawana anthu anga pochita maere

ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere;

anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo

kuti iwo amwe.

4“Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu. 5Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano. 6Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.

7“Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu. 8Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.

9Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina:

Konzekerani nkhondo!

Dzutsani ankhondo amphamvu!

Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.

10Sulani makasu anu kuti akhale malupanga

ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo.

Munthu wofowoka anene kuti,

“Ndine wamphamvu!”

11Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse,

ndipo musonkhane kumeneko.

Tumizani ankhondo anu Yehova!

12“Mitundu ya anthu idzuke;

ipite ku Chigwa cha Yehosafati,

pakuti kumeneko Ine ndidzakhala

ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.

13Tengani chikwakwa chodulira tirigu,

pakuti mbewu zakhwima.

Bwerani dzapondeni mphesa,

pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza

ndipo mitsuko ikusefukira;

kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”

14Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu,

mʼchigwa cha chiweruzo!

Pakuti tsiku la Yehova layandikira

mʼchigwa cha chiweruzo.

15Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa,

ndipo nyenyezi sizidzawalanso.

16Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni

ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu;

dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka.

Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake,

linga la anthu a ku Israeli.

Madalitso a Anthu a Mulungu

17“Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu,

ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika.

Yerusalemu adzakhala wopatulika;

alendo sadzamuthiranso nkhondo.

18“Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano,

ndipo zitunda zidzayenderera mkaka;

mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi.

Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova

ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.

19Koma Igupto adzasanduka bwinja,

Edomu adzasanduka chipululu,

chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda

mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.

20Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya

ndi Yerusalemu ku mibadomibado.

21Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke

ndidzakhululuka.”

Yehova amakhala mu Ziyoni!

Nova Versão Internacional

Joel 3:1-21

O Julgamento das Nações

1“Sim, naqueles dias e naquele tempo,

quando eu restaurar a sorte de Judá e de Jerusalém,

2reunirei todos os povos

e os farei descer ao vale de Josafá3.2 Josafá significa o Senhor julga; também no versículo 12..

Ali os julgarei por causa da minha herança

Israel, o meu povo—, pois o espalharam entre as nações

e repartiram entre si a minha terra.

3Lançaram sortes sobre o meu povo

e deram meninos em troca de prostitutas;

venderam meninas por vinho,

para se embriagarem.

4“O que vocês têm contra mim, Tiro, Sidom,

e todas as regiões da Filístia?

Vocês estão me retribuindo algo que eu fiz a vocês?

Se estão querendo vingar-se de mim,

ágil e veloz me vingarei do que vocês têm feito.

5Pois roubaram a minha prata e o meu ouro

e levaram para os seus templos os meus tesouros mais valiosos.

6Vocês venderam o povo de Judá

e o de Jerusalém aos gregos,

mandando-os para longe

da sua terra natal.

7“Vou tirá-los dos lugares para onde os venderam

e sobre vocês farei recair o que fizeram:

8venderei os filhos e as filhas de vocês ao povo de Judá,

e eles os venderão à distante nação dos sabeus”.

Assim disse o Senhor.

9Proclamem isto entre as nações:

Preparem-se para a guerra!

Despertem os guerreiros!

Todos os homens de guerra aproximem-se e ataquem.

10Forjem os seus arados,

fazendo deles espadas;

e de suas foices façam lanças.

Diga o fraco: “Sou um guerreiro!”

11Venham depressa, vocês, nações vizinhas,

e reúnam-se ali.

Faze descer os teus guerreiros, ó Senhor!

12“Despertem, nações;

avancem para o vale de Josafá,

pois ali me assentarei

para julgar todas as nações vizinhas.

13Lancem a foice,

pois a colheita está madura.

Venham, pisem com força as uvas,

pois o lagar está cheio

e os tonéis transbordam,

tão grande é a maldade dessas nações!”

14Multidões, multidões

no vale da Decisão!

Pois o dia do Senhor está próximo,

no vale da Decisão.

15O sol e a lua escurecerão,

e as estrelas já não brilharão.

16O Senhor rugirá de Sião,

e de Jerusalém levantará a sua voz;

a terra e o céu tremerão.

Mas o Senhor será um refúgio para o seu povo,

uma fortaleza para Israel.

Bênçãos para o Povo de Deus

17“Então vocês saberão que eu sou o Senhor, o seu Deus,

que habito em Sião, o meu santo monte.

Jerusalém será santa;

e estrangeiros jamais a conquistarão.

18“Naquele dia, os montes gotejarão vinho novo;

das colinas manará leite;

todos os ribeiros de Judá terão água corrente.

Uma fonte fluirá do templo do Senhor

e regará o vale das Acácias.

19Mas o Egito ficará desolado,

Edom será um deserto arrasado,

por causa da violência feita ao povo de Judá,

em cuja terra derramaram sangue inocente.

20Judá será habitada para sempre

e Jerusalém por todas as gerações.

21Sua culpa de sangue, ainda não perdoada,

eu a perdoarei.”

O Senhor habita em Sião!