Yoweli 3 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoweli 3:1-21

Kuweruzidwa kwa Mitundu ya Anthu

1“Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo,

nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,

2ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse

ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati.

Kumeneko ndidzawaweruza

chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli,

pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu

ndikugawa dziko langa.

3Anagawana anthu anga pochita maere

ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere;

anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo

kuti iwo amwe.

4“Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu. 5Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano. 6Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.

7“Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu. 8Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.

9Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina:

Konzekerani nkhondo!

Dzutsani ankhondo amphamvu!

Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.

10Sulani makasu anu kuti akhale malupanga

ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo.

Munthu wofowoka anene kuti,

“Ndine wamphamvu!”

11Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse,

ndipo musonkhane kumeneko.

Tumizani ankhondo anu Yehova!

12“Mitundu ya anthu idzuke;

ipite ku Chigwa cha Yehosafati,

pakuti kumeneko Ine ndidzakhala

ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.

13Tengani chikwakwa chodulira tirigu,

pakuti mbewu zakhwima.

Bwerani dzapondeni mphesa,

pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza

ndipo mitsuko ikusefukira;

kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”

14Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu,

mʼchigwa cha chiweruzo!

Pakuti tsiku la Yehova layandikira

mʼchigwa cha chiweruzo.

15Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa,

ndipo nyenyezi sizidzawalanso.

16Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni

ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu;

dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka.

Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake,

linga la anthu a ku Israeli.

Madalitso a Anthu a Mulungu

17“Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu,

ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika.

Yerusalemu adzakhala wopatulika;

alendo sadzamuthiranso nkhondo.

18“Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano,

ndipo zitunda zidzayenderera mkaka;

mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi.

Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova

ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.

19Koma Igupto adzasanduka bwinja,

Edomu adzasanduka chipululu,

chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda

mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.

20Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya

ndi Yerusalemu ku mibadomibado.

21Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke

ndidzakhululuka.”

Yehova amakhala mu Ziyoni!

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Иоиль 3:1-21

Суд над народами

1– В те дни, в то самое время,

когда Я восстановлю Иудею и Иерусалим,

2Я соберу все народы

и приведу их в долину Суда3:2 Букв.: «долина Иосафата» – название, которое переводится как: «Вечный судит», то же в ст. 12..

Я буду судить их там

за Мой народ и за Моё наследие – Исраил,

который они рассеяли между народами,

и за Мою землю, которую они разделили.

3Они бросали жребий о Моём народе,

отдавали мальчиков за блудниц

и продавали девочек за вино,

чтобы напиться.

4– Итак, что вы имеете против Меня, народы Тира и Сидона и все жители филистимских округов? Хотите ли воздать Мне возмездие? Если и воздадите Мне, то Я легко и быстро верну возмездие ваше на ваши же головы. 5Вы забрали Моё серебро и золото и внесли лучшие драгоценности в свои капища. 6Вы продавали людей Иудеи и Иерусалима грекам3:6 Букв.: «сыновьям Иавана». для того, чтобы отдалить их от родины.

7Смотрите, Я верну их из тех мест, куда вы продали их, и обращу содеянное вами на ваши же головы. 8Я продам ваших сыновей и дочерей людям из Иудеи, а они продадут их севеянам, отдалённому народу, – так сказал Вечный.

9Провозгласите это между народами:

«Приготовьтесь к войне!

Поднимайте лучших бойцов!

Пусть выступят все воины,

пусть они идут в атаку.

10Перекуйте ваши плуги на мечи

и ваши серпы на копья.

Пусть слабый говорит:

„Я сильный воин!“

11Спешите, все народы, со всех сторон

и собирайтесь в долине».

О Вечный, веди туда Своё воинство!

12– Пусть воспрянут народы,

пусть пойдут в долину Суда,

потому что там Я воссяду,

чтобы судить их всех.

13Взмахните серпами,

потому что созрела жатва,

давите виноград,

потому что давильня наполнена,

и как переливается из сосудов вино,

так велика и злоба их!

14Огромные массы людей толпятся

в долине Приговора,

потому что близок день Вечного

в долине Приговора!

15Померкнут солнце и луна,

и потеряют звёзды свой блеск.

16Прогремит Вечный с Сиона,

воскликнет Он громким голосом из Иерусалима,

и поколеблются земля и небо.

Но Вечный будет убежищем для Своего народа,

крепостью – для народа Исраила.

17– И тогда вы узнаете, что Я – Вечный, ваш Бог,

живущий на Сионе, Моей святой горе.

Иерусалим будет святыней,

и никогда более в него не вступит чужеземцев рать.

18В тот день с гор будет капать молодое вино,

и с холмов потечёт молоко,

и все русла Иудеи наполнятся водою.

В доме Вечного забьёт источник

и напоит безводную долину акаций3:18 Букв.: «долина Шиттим». Акация любит сухую почву и поэтому растёт только в засушливых регионах..

19Египет будет опустошён,

а Эдом станет безлюдной пустыней –

за насилие, которое они причинили народу Иудеи,

и за невинную кровь, пролитую в их земле.

20Иудея будет жить вечно,

и Иерусалим – из поколения в поколение.

21Я отомщу за их кровь,

не оставлю без наказания3:21 Или: «Я смою их кровь, которую ещё не смыл»..

Вечный будет жить на Сионе!