Yoweli 2 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoweli 2:1-32

Chilango cha Mulungu

1Lizani lipenga mu Ziyoni.

Chenjezani pa phiri langa loyera.

Onse okhala mʼdziko anjenjemere,

pakuti tsiku la Yehova likubwera,

layandikira;

2tsiku la mdima ndi chisoni,

tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.

Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri,

gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera,

gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo

ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.

3Patsogolo pawo moto ukupsereza,

kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu.

Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni,

kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu,

kulibe kanthu kotsalapo.

4Maonekedwe awo ali ngati akavalo;

akuthamanga ngati akavalo ankhondo.

5Akulumpha pamwamba pa mapiri

ndi phokoso ngati la magaleta,

ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu,

ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.

6Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima;

nkhope iliyonse imagwa.

7Amathamanga ngati ankhondo;

amakwera makoma ngati asilikali.

Onse amayenda pa mizere,

osaphonya njira yawo.

8Iwo sakankhanakankhana,

aliyense amayenda molunjika.

Amadutsa malo otchingidwa

popanda kumwazikana.

9Amakhamukira mu mzinda,

amathamanga mʼmbali mwa khoma.

Amakwera nyumba ndi kulowamo;

amalowera pa zenera ngati mbala.

10Patsogolo pawo dziko limagwedezeka,

thambo limanjenjemera,

dzuwa ndi mwezi zimachita mdima,

ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.

11Yehova amabangula

patsogolo pawo,

gulu lake lankhondo ndi losawerengeka,

ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake.

Tsiku la Yehova ndi lalikulu;

ndi loopsa.

Ndani adzapirira pa tsikulo?

Ngʼambani Mtima Wanu

12“Ngakhale tsopano,

bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse

posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.

13Ngʼambani mtima wanu

osati zovala zanu.

Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu,

pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo,

wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka,

ndipo amaleka kubweretsa mavuto.

14Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni,

nʼkutisiyira madalitso,

a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa

kwa Yehova Mulungu wanu.

15Lizani lipenga mu Ziyoni,

lengezani tsiku losala zakudya,

itanitsani msonkhano wopatulika.

16Sonkhanitsani anthu pamodzi,

muwawuze kuti adziyeretse;

sonkhanitsani akuluakulu,

sonkhanitsani ana,

sonkhanitsani ndi oyamwa omwe.

Mkwati atuluke mʼchipinda chake,

mkwatibwi atuluke mokhala mwake.

17Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova,

alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova.

Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu.

Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka,

kuti anthu a mitundu ina awalamulire.

Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti,

‘Ali kuti Mulungu wawo?’ ”

Yankho la Yehova

18Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake

ndi kuchitira chisoni anthu ake.

19Yehova adzawayankha kuti,

“Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta

ndipo mudzakhuta ndithu;

sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo

kwa anthu a mitundu ina.

20“Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu,

kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu,

gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa

ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo.

Ndipo mitembo yawo idzawola,

fungo lake lidzamveka.”

Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.

21Iwe dziko usachite mantha;

sangalala ndipo kondwera.

Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.

22Inu nyama zakuthengo, musachite mantha,

pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira.

Mitengo ikubala zipatso zake;

mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.

23Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani,

kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu,

pakuti wakupatsani

mvula yoyambirira mwachilungamo chake.

Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka,

mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.

24Pa malo opunthira padzaza tirigu;

mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.

25“Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe,

dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono,

dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka;

gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.

26Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta,

ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu,

amene wakuchitirani zodabwitsa;

ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.

27Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli,

kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu,

ndi kuti palibenso wina;

ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.

Tsiku la Yehova

28“Ndipo patapita nthawi,

ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse.

Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera,

nkhalamba zanu zidzalota maloto,

anyamata anu adzaona masomphenya.

29Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi

ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.

30Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga

ndi pa dziko lapansi,

ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.

31Dzuwa lidzadetsedwa

ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi

lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.

32Ndipo aliyense amene adzayitana

pa dzina la Ambuye adzapulumuka;

pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni

ndi mu Yerusalemu,

monga Yehova wanenera,

pakati pa otsala

amene Yehova wawayitana.

Nueva Versión Internacional

Joel 2:1-32

Un ejército de langostas

1¡Toquen la trompeta en Sión;

den la voz de alarma en mi santo monte!

¡Tiemblen todos los habitantes del país!

Ya viene el día del Señor;

en realidad, ya está cerca.

2Día de tinieblas y oscuridad,

día de nubes y densos nubarrones.

Como la aurora que se extiende sobre los montes,

así avanza un pueblo fuerte y numeroso,

pueblo como nunca lo hubo en la antigüedad

ni lo habrá en las generaciones futuras.

3El fuego devora delante de ellos;

detrás, las llamas arden.

Antes de su llegada, el país se parece al jardín del Edén;

después, queda un desolado desierto.

¡Nada escapa de su poder!

4Tienen aspecto de caballos;

galopan como corceles.

5Al saltar sobre las cumbres de los montes,

producen un estruendo como el de carros de guerra,

como el crepitar del fuego al consumir la hojarasca.

¡Son como un ejército poderoso en formación de batalla!

6Ante él se estremecen las naciones;

todo rostro palidece.

7Atacan como guerreros,

escalan muros como soldados.

Cada uno mantiene la marcha

sin romper la formación.

8No se atropellan entre sí;

cada uno marcha en línea.

Se lanzan entre las flechas

sin romper filas.

9Se abalanzan contra la ciudad,

escalan los muros,

trepan por las casas,

se meten por las ventanas como ladrones.

10Ante este ejército tiembla la tierra

y se estremece el cielo,

el sol y la luna se oscurecen

y las estrellas dejan de brillar.

11Truena la voz del Señor

al frente de su ejército;

son innumerables sus tropas

y poderosos los que ejecutan su palabra.

El día del Señor es grande y terrible.

¿Quién lo podrá resistir?

Exhortación al arrepentimiento

12«Ahora bien», afirma el Señor,

«vuélvanse a mí de todo corazón,

con ayuno, llantos y lamentos».

13Rásguense el corazón

y no las vestiduras.

Vuélvanse al Señor su Dios,

porque él es misericordioso y compasivo,

lento para la ira y lleno de amor,

cambia de parecer y no castiga.

14Tal vez Dios reconsidere y cambie de parecer,

y deje tras de sí una bendición.

Las ofrendas de cereales y las ofrendas líquidas

son del Señor su Dios.

15¡Toquen la trompeta en Sión!

¡Proclamen el ayuno!

¡Convoquen a una asamblea sagrada!

16¡Congreguen al pueblo;

consagren la asamblea!

¡Junten a los ancianos del pueblo,

reúnan a los pequeños

y a los niños de pecho!

¡Que salga de su alcoba el recién casado

y la recién casada, de su cámara nupcial!

17Lloren, sacerdotes, ministros del Señor,

entre la entrada y el altar;

y digan: «Compadécete, Señor, de tu pueblo.

No entregues tu propiedad como objeto de burla,

para que las naciones no se burlen de ella.2:17 no se burlen de ella. Alt. no la sometan.

¿Por qué habrán de decir entre los pueblos:

“Dónde está su Dios?”».

La respuesta del Señor

18Entonces el Señor se llenó de celos por su tierra

y mostró piedad a su pueblo.

19Y respondió el Señor:

«Miren, enviaré cereales, vino nuevo y aceite,

hasta dejarlos plenamente satisfechos;

y nunca más los haré

objeto de burla de las naciones.

20»Alejaré de ustedes al que viene del norte,

arrojándolo hacia una tierra seca y desolada:

lanzaré su vanguardia hacia el mar oriental,

y su retaguardia hacia el mar occidental.2:20 el mar oriental … el mar occidental. Es decir, el mar Muerto y el Mediterráneo.

Subirá su hedor

y se elevará su fetidez».

¡El Señor ha hecho grandes cosas!

21No temas, tierra,

sino alégrate y regocíjate,

porque el Señor ha hecho grandes cosas.

22No teman, animales del campo,

porque los pastizales de la estepa ya reverdecen;

los árboles producen su fruto

y la higuera y la vid dan su riqueza.

23Alégrense, habitantes de Sión,

regocíjense en el Señor su Dios,

porque les ha dado las lluvias de otoño.

Él envía la lluvia,

la de otoño y la de primavera,

como en tiempos pasados.

24Las parcelas se llenarán de grano;

los lagares rebosarán de vino nuevo y de aceite.

25«Yo los compensaré a ustedes

por los años en que todo lo devoró

ese gran ejército de langostas

que envié contra ustedes:

las grandes, las pequeñas,

las jóvenes y los saltamontes.2:25 Véase nota en 1:4.

26Ustedes comerán en abundancia, hasta saciarse,

y alabarán el nombre del Señor su Dios,

que hará maravillas por ustedes.

¡Nunca más será avergonzado mi pueblo!

27Entonces sabrán que yo estoy en medio de Israel,

que yo soy el Señor su Dios,

y no hay otro fuera de mí.

¡Nunca más será avergonzado mi pueblo!

El día del Señor

28»Después de esto,

derramaré mi Espíritu sobre todo ser humano.

Los hijos y las hijas de ustedes profetizarán,

tendrán sueños los ancianos

y los jóvenes recibirán visiones.

29En esos días derramaré mi Espíritu

aun sobre los siervos y las siervas.

30En el cielo y en la tierra mostraré prodigios:

sangre, fuego y columnas de humo.

31El sol se convertirá en tinieblas

y la luna en sangre

antes que llegue el día del Señor,

día grande y terrible.

32Y todo el que invoque el nombre del Señor será salvo,

porque en el monte Sión y en Jerusalén

habrá salvación,

como lo ha dicho el Señor.

Y entre los sobrevivientes

estarán los llamados del Señor.