Yoweli 2 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoweli 2:1-32

Chilango cha Mulungu

1Lizani lipenga mu Ziyoni.

Chenjezani pa phiri langa loyera.

Onse okhala mʼdziko anjenjemere,

pakuti tsiku la Yehova likubwera,

layandikira;

2tsiku la mdima ndi chisoni,

tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.

Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri,

gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera,

gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo

ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.

3Patsogolo pawo moto ukupsereza,

kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu.

Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni,

kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu,

kulibe kanthu kotsalapo.

4Maonekedwe awo ali ngati akavalo;

akuthamanga ngati akavalo ankhondo.

5Akulumpha pamwamba pa mapiri

ndi phokoso ngati la magaleta,

ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu,

ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.

6Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima;

nkhope iliyonse imagwa.

7Amathamanga ngati ankhondo;

amakwera makoma ngati asilikali.

Onse amayenda pa mizere,

osaphonya njira yawo.

8Iwo sakankhanakankhana,

aliyense amayenda molunjika.

Amadutsa malo otchingidwa

popanda kumwazikana.

9Amakhamukira mu mzinda,

amathamanga mʼmbali mwa khoma.

Amakwera nyumba ndi kulowamo;

amalowera pa zenera ngati mbala.

10Patsogolo pawo dziko limagwedezeka,

thambo limanjenjemera,

dzuwa ndi mwezi zimachita mdima,

ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.

11Yehova amabangula

patsogolo pawo,

gulu lake lankhondo ndi losawerengeka,

ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake.

Tsiku la Yehova ndi lalikulu;

ndi loopsa.

Ndani adzapirira pa tsikulo?

Ngʼambani Mtima Wanu

12“Ngakhale tsopano,

bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse

posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.

13Ngʼambani mtima wanu

osati zovala zanu.

Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu,

pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo,

wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka,

ndipo amaleka kubweretsa mavuto.

14Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni,

nʼkutisiyira madalitso,

a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa

kwa Yehova Mulungu wanu.

15Lizani lipenga mu Ziyoni,

lengezani tsiku losala zakudya,

itanitsani msonkhano wopatulika.

16Sonkhanitsani anthu pamodzi,

muwawuze kuti adziyeretse;

sonkhanitsani akuluakulu,

sonkhanitsani ana,

sonkhanitsani ndi oyamwa omwe.

Mkwati atuluke mʼchipinda chake,

mkwatibwi atuluke mokhala mwake.

17Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova,

alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova.

Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu.

Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka,

kuti anthu a mitundu ina awalamulire.

Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti,

‘Ali kuti Mulungu wawo?’ ”

Yankho la Yehova

18Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake

ndi kuchitira chisoni anthu ake.

19Yehova adzawayankha kuti,

“Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta

ndipo mudzakhuta ndithu;

sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo

kwa anthu a mitundu ina.

20“Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu,

kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu,

gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa

ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo.

Ndipo mitembo yawo idzawola,

fungo lake lidzamveka.”

Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.

21Iwe dziko usachite mantha;

sangalala ndipo kondwera.

Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.

22Inu nyama zakuthengo, musachite mantha,

pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira.

Mitengo ikubala zipatso zake;

mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.

23Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani,

kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu,

pakuti wakupatsani

mvula yoyambirira mwachilungamo chake.

Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka,

mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.

24Pa malo opunthira padzaza tirigu;

mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.

25“Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe,

dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono,

dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka;

gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.

26Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta,

ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu,

amene wakuchitirani zodabwitsa;

ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.

27Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli,

kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu,

ndi kuti palibenso wina;

ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.

Tsiku la Yehova

28“Ndipo patapita nthawi,

ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse.

Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera,

nkhalamba zanu zidzalota maloto,

anyamata anu adzaona masomphenya.

29Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi

ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.

30Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga

ndi pa dziko lapansi,

ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.

31Dzuwa lidzadetsedwa

ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi

lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.

32Ndipo aliyense amene adzayitana

pa dzina la Ambuye adzapulumuka;

pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni

ndi mu Yerusalemu,

monga Yehova wanenera,

pakati pa otsala

amene Yehova wawayitana.

Bibelen på hverdagsdansk

Joels Bog 2:1-27

Græshoppeplagen ses som et tegn på og forvarsel om Guds dom

1Blæs i vædderhornet fra Zion. Lad præsterne sende signal fra Herrens hellige bjerg. Alle mennesker vil skælve, for dommens dag er nær.

2Det bliver en mørk og dyster dag med kulsorte skyer på himlen. Som morgenlyset breder sig over bjergene, bevæger en mægtig fjendehær sig frem. Aldrig før har man set så vældig en hær, og aldrig siden skal man se dens lige. 3Den stormer frem som en steppebrand. Foran den ligger landet grønt og frugtbart som Edens have, bagved den er landet øde som en ørken. Intet undslipper. 4Det ligner en hær af heste, som stormer frem til angreb. 5De springer hen over bjergene med en larm som stridsvogne i fuld fart. Man hører en knitren som en stubmark, der brænder. De rykker frem som en mægtig hær i kampformation. 6Folkeslag gribes af frygt for dem, og alle ansigter bliver ligblege.

7De stormer frem som veltrænede soldater og forcerer enhver forhindring. De styrer lige mod målet uden at komme ud af kurs. 8De går ikke i vejen for hinanden, men holder retningen. De trænger frem gennem en regn af spyd, og lader sig ikke standse. 9De kaster sig over byen. De løber oven på bymuren. De trænger ind i husene. De klatrer gennem vinduerne, som var de tyve. 10Jorden skælver foran dem, og himlens kræfter rystes. Solen og månen formørkes, og stjernerne holder op med at skinne.

11Herren fører an med et højt kommandoråb, for det er hans mægtige, talløse hær. En enorm skare står parat til at udføre hans ordrer. Det bliver en frygtelig dag, når Herren fælder sin dom. Hvem kan udholde den dag?

Et kald til omvendelse

12Herren siger: „Vend om til mig, mens der endnu er tid! Søg mig af hele jeres hjerte med anger, gråd og faste. 13Sønderriv jeres hjerter, ikke jeres tøj.”2,13 Det var skik dengang at sønderrive sin yderkjortel som tegn på sorg og fortvivlelse.

Vend om til Herren, jeres Gud, for han er nådig og barmhjertig. Der skal meget til, før han bliver vred, og han omslutter jer med sin trofaste kærlighed. Han er parat til at eftergive straffen. 14Hvem ved? Det kan være, han standser straffen og velsigner jer i stedet, så der igen kan bringes afgrødeofre og drikofre til Herren, jeres Gud.

15Blæs nu I vædderhornet fra Zions bjerg! Kald folket sammen til faste og bod. 16Alle skal samles, både gamle og børn, ja selv spædbørn. Lad brudepar afbryde deres fest for at komme herhen.

17Guds tjenere, præsterne, skal stille sig op mellem indgangen til templet og alteret, så de grædende kan gå i forbøn for landet. „Herre, skån dit folk,” skal de bede. „Lad ikke de andre folkeslag håne os og sige: ‚Hvor er jeres Gud, som skulle hjælpe jer?’ ”

Herren griber ind

18Da de havde gjort det, fik Herren medlidenhed med sit folk, og viste sin nidkærhed for det land, han havde givet dem. 19Han svarede på sit folks bøn og sagde: „Jeg vil give jer korn, olivenolie og vin, så der er rigeligt til alle. I skal ikke længere hånes af de andre folkeslag. 20Jeg vil fjerne hæren af græshopper fra nord. Størsteparten drives ud i ørkenen, mens fortropperne drukner i Det Døde Hav og bagtropperne i Middelhavet. Der bliver en voldsom stank af død.”

Herren har gjort store ting! 21Nu skal alle glæde og fryde sig, for Herren har gjort store ting for os. 22Dyrene glæder sig, for græsset bliver grønt, og træerne bærer frugt. Figentræer og vinstokke giver igen en rigelig høst.

23Jerusalem, fryd dig over Herren, din Gud, for regnen, han sender, er et tegn på hans godhed. Han sender rigeligt med efterårsregn og forårsregn som før. 24Tærskepladsen skal fyldes med korn, persekarret flyde over med druesaft og olivenpressen med olie.

25Herren siger: „Jeg vil erstatte det, I mistede i de år, da græshopperne åd jeres afgrøder. Det var mig, der sendte den store hær imod jer. 26-27Men nu skal I spise og blive mætte, og I skal takke og lovprise mig for den store nåde, jeg har vist jer. Aldrig igen skal mit folk opleve en lignende katastrofe. I skal få at se, at jeg er midt iblandt mit folk, Israel, og at jeg alene er Herren, jeres Gud.