Yoweli 1 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoweli 1:1-20

1Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.

Kubwera kwa Dzombe

2Inu akuluakulu, imvani izi;

mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko.

Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu,

kapena mʼnthawi ya makolo anu?

3Muwafotokozere ana anu,

ndipo ana anuwo afotokozere ana awo,

ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.

4Chimene dzombe losamera mapiko lasiya

dzombe lowuluka ladya;

chimene dzombe lowuluka lasiya

dzombe lalingʼono ladya;

chimene dzombe lalingʼono lasiya

chilimamine wadya.

5Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire!

Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo;

lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano,

pakuti wachotsedwa pakamwa panu.

6Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa,

wamphamvu ndi wosawerengeka;

uli ndi mano a mkango,

zibwano za mkango waukazi.

7Wawononga mphesa zanga

ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu.

Wakungunula makungwa ake

ndi kuwataya,

kusiya nthambi zake zili mbee.

8Lirani ngati namwali wovala chiguduli,

chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.

9Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa

sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova.

Ansembe akulira,

amene amatumikira pamaso pa Yehova.

10Minda yaguga,

nthaka yauma;

tirigu wawonongeka,

vinyo watsopano watha,

mitengo ya mafuta yauma.

11Khalani ndi nkhawa, inu alimi,

lirani mofuwula inu alimi a mphesa;

imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele,

pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.

12Mpesa wauma

ndipo mtengo wamkuyu wafota;

makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi,

mitengo yonse ya mʼmunda yauma.

Ndithudi chimwemwe cha anthu

chatheratu.

Mulungu Ayitana Anthu kuti Atembenuke

13Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani;

lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe.

Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse,

inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga;

pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa

sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.

14Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya,

itanani msonkhano wopatulika.

Sonkhanitsani akuluakulu

ndi anthu onse okhala mʼdziko

ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu

ndipo alirire Yehova.

15Kalanga ine tsikulo!

Pakuti tsiku la Yehova layandikira;

lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.

16Kodi chakudya chathu sichachotsedwa

ife tikuona?

Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu

simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?

17Mbewu zikunyala

poti pansi ndi powuma.

Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka;

nkhokwe zapasuka

popeza tirigu wauma.

18Taonani mmene zikulirira ziweto;

ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku

chifukwa zilibe msipu;

ngakhalenso nkhosa zikusauka.

19Kwa Inu Yehova ndilirira,

pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo,

malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.

20Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu;

timitsinje tonse taphwa

ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Yoeli 1:1-20

11:1 2Pet 1:21; Ebr 1:1; Yer 1:2; Mdo 2:16Neno la Bwana ambalo lilimjia Yoeli mwana wa Pethueli.

Uvamizi Wa Nzige

21:2 Yoe 2:2, 16; Hos 4:1; 5:1; Isa 7:17; Kum 4:32; Dan 12:1; Mt 24:21Sikilizeni hili, enyi wazee;

sikilizeni, ninyi nyote mnaoishi katika nchi.

Je, jambo kama hili lilishawahi kutokea

katika siku zenu au katika siku za babu zenu?

31:3 Kut 10:2; Za 78:4Waelezeni watoto wenu,

na watoto wenu wawaambie watoto wao,

na watoto wao kwa kizazi kitakachofuata.

41:4 Kut 10:4, 14-15; Amo 7:1; Neh 3:15; Kum 28:39Kilichosazwa na kundi la tunutu

nzige wakubwa wamekula,

kilichosazwa na nzige wakubwa

parare wamekula,

kilichosazwa na parare

madumadu wamekula.

51:5 Isa 24:7; 32:10; Yoe 3:3Amkeni, enyi walevi, mlie!

Pigeni yowe enyi wanywaji wote wa mvinyo,

pigeni yowe kwa sababu ya mvinyo mpya,

kwa kuwa mmenyangʼanywa

kutoka midomoni mwenu.

61:6 Yoe 2:2, 11, 25; Ufu 9:8; Mit 30:25; Za 105:35Taifa limevamia nchi yangu,

lenye nguvu tena lisilo na idadi;

lina meno ya simba,

magego ya simba jike.

71:7 Isa 5:8; Amo 4:9Limeharibu mizabibu yangu

na kuangamiza mitini yangu.

Limebambua magome yake

na kuyatupilia mbali,

likayaacha matawi yake yakiwa meupe.

81:8 Isa 22:2; Amo 8:10; Mit 2:17Omboleza kama bikira aliyevaa nguo ya gunia

anayehuzunika kwa ajili ya mume wa ujana wake.

91:9 Yoe 2:14; Hos 9:4; Isa 22:12Sadaka za nafaka na sadaka za kinywaji

zimekatiliwa mbali kutoka nyumba ya Bwana.

Makuhani wanaomboleza,

wale wanaohudumu mbele za Bwana.

101:10 Isa 5:6; 24:4; Yer 3:3; Hos 9:2; Hes 18:12; Yer 12:11Mashamba yameharibiwa,

ardhi imekauka;

nafaka imeharibiwa,

mvinyo mpya umekauka,

mafuta yamekoma.

111:11 Yer 14:3; Ay 6:20; Amo 5:16; Kut 9:31; Isa 17:11Kateni tamaa, enyi wakulima,

lieni, enyi mlimao mizabibu;

huzunikeni kwa ajili ya ngano na shayiri,

kwa sababu mavuno ya shambani yameharibiwa.

121:12 Isa 15:6; Kut 28:33; Isa 16:8; Hos 9:1-2; Hag 2:19; Yer 48:33Mzabibu umekauka

na mtini umenyauka;

mkomamanga, mtende na mtofaa,

miti yote shambani, imekauka.

Hakika furaha yote ya mwanadamu

imeondoka.

Wito Wa Toba

131:13 Mwa 37:34; Yer 4:8; 2:17; Hos 9:4; Yoe 2:14Vaeni nguo ya gunia, enyi makuhani, muomboleze;

pigeni yowe, enyi mnaohudumu madhabahuni.

Njooni, vaeni nguo ya gunia usiku kucha,

enyi mnaohudumu mbele za Mungu wangu;

kwa kuwa sadaka za nafaka na sadaka za kinywaji

zimezuiliwa kufika katika nyumba ya Mungu wenu.

141:14 2Nya 20:3-4; Yon 3:8; Hos 4:1Tangazeni saumu takatifu;

liiteni kusanyiko takatifu.

Iteni wazee

na wote waishio katika nchi

waende katika nyumba ya Bwana Mungu wenu,

wakamlilie Bwana.

151:15 Yer 30:7; 46:10; Isa 2:12; Eze 30:3; Amo 5:8Ole kwa siku hiyo!

Kwa kuwa siku ya Bwana iko karibu;

itakuja kama uharibifu

kutoka kwa Mwenyezi.1:15 Mwenyezi hapa ina maana ya Shaddai kwa Kiebrania.

16Je, chakula hakikukatiliwa mbali

mbele ya macho yetu:

furaha na shangwe

kutoka nyumba ya Mungu wetu?

17Mbegu zinakauka

chini ya mabonge ya udongo.

Ghala zimeachwa katika uharibifu,

ghala za nafaka zimebomolewa,

kwa maana hakuna nafaka.

18Jinsi gani ngʼombe wanavyolia!

Makundi ya mifugo yanahangaika

kwa sababu hawana malisho;

hata makundi ya kondoo yanateseka.

19Kwako, Ee Bwana, naita,

kwa kuwa moto umeteketeza

malisho ya mbugani

na miali ya moto imeunguza

miti yote shambani.

20Hata wanyama wa porini wanakuonea shauku;

vijito vya maji vimekauka,

na moto umeteketeza

malisho yote ya mbugani.