Yoswa 5 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 5:1-15

Mwambo wa Mdulidwe pa Giligala

1Mafumu onse a Aamori, a kummawa kwa Yorodani ndi mafumu onse a Akanaani a mʼmbali mwa Nyanja anamva momwe Yehova anawumitsira Yorodani pamene Aisraeli ankawoloka. Choncho anachita mantha ndi kutayiratu mtima chifukwa cha Aisraeliwo.

2Tsono Yehova anati kwa Yoswa, “Panga mipeni ya miyala ndipo uchitenso mwambo wa mdulidwe pa Aisraeli.” 3Choncho Yoswa anapanga mipeni ya miyala ndi kuchita mdulidwe Aisraeli ku Gibeyati Haaraloti.

4Chifukwa chimene Yoswa anachitira izi ndi ichi: Onse amene anatuluka mʼdziko la Igupto, amuna onse amene anali oyenera kumenya nkhondo anatha kufa mʼchipululu atatuluka mʼdziko la Igupto. 5Anthu onse amene anatuluka mʼdziko la Igupto anali atachita mwambo wa mdulidwe, koma onse amene anabadwira mʼchipululu, pa ulendo wochoka ku Igupto, sanachite. 6Aisraeli anakhala akuyenda mʼchipululu kwa zaka makumi anayi mpaka amuna onse amene potuluka mʼdziko la Igupto anali a msinkhu woyenera kupita ku nkhondo anamwalira. Iwo anafa chifukwa sanamvere mawu a Yehova. Yehova anawalumbirira kuti sadzalowa konse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi limene analonjeza kwa makolo awo kuti adzatipatsa. 7Koma ana awo amene analowa mʼmalo mwawo ndiwo amene Yoswa anawachita mdulidwe popeza sanachite pamene anali pa ulendo wawo mʼchipululu muja. 8Atamaliza kuchita mdulidwe uja, anthu onse anakakhala ku misasa yawo kudikira kuti zilonda zipole.

9Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Kuyambira tsopano anthu a ku Igupto sadzakunyozaninso.” Nʼchifukwa chake malowa anatchedwa Giligala mpaka lero.

10Akupumulabe ku Giligala kuja mʼchigwa cha Yeriko, Aisraeli anachita chikondwerero cha Paska madzulo pa tsiku la 14 la mwezi woyamba womwewo. 11Mmawa mwake ndi pamene anayamba kudya zakudya za mʼdziko la Kanaani. Anaphika buledi wopanda yisiti ndi kukazinga tirigu tsiku lomwelo. 12Atangodya chakudya cha mʼdzikomo, mana anasiya kugwa, ndipo sanapezekenso. Kuyambira nthawi imeneyo Aisraeli anayamba kudya chakudya cha mʼdziko la Kanaani.

Kugwa kwa Makoma a Yeriko

13Tsiku lina pamene Yoswa anali pafupi ndi Yeriko, anakweza maso ake ndipo mwadzidzidzi anaona munthu atayima patsogolo pake ndi lupanga losolola mʼdzanja lake. Yoswa anapita pamene panali munthuyo ndipo anamufunsa kuti, “Kodi uli mbali yathu kapena ya adani athu?”

14Iye anayankha kuti “Sindili mbali iliyonse. Ndabwera monga mkulu wa asilikali a Yehova.” Pomwepo Yoswa anadzigwetsa chafufumimba kupereka ulemu, ndipo anamufunsa, “Kodi mbuye wanga muli ndi uthenga wotani kwa mtumiki wanu?”

15Mkulu wa asilikali a Yehova uja anayankha kuti, “Vula nsapato zako, pakuti wayima pa malo wopatulika.” Ndipo Yoswa anachitadi zimene anawuzidwazo.

La Bible du Semeur

Josué 5:1-15

1Tous les rois des Amoréens établis sur la rive occidentale du Jourdain et tous les rois des Cananéens établis sur le littoral de la mer Méditerranée apprirent que l’Eternel avait asséché le Jourdain devant les Israélites jusqu’à ce qu’ils l’aient traversé. Alors le courage leur manqua et ils perdirent tous leurs moyens en face des Israélites.

La circoncision de la nouvelle génération

2A cette même époque, l’Eternel dit à Josué : Fais-toi des couteaux de silex et circoncis cette deuxième génération d’Israélites.

3Josué se munit de couteaux de silex et circoncit les Israélites sur la colline d’Araloth.

4Voici pourquoi Josué les circoncit : tous les hommes en âge de porter les armes qui étaient sortis d’Egypte étaient morts en chemin dans le désert après avoir quitté l’Egypte. 5Ils étaient tous circoncis. Mais les garçons nés pendant la traversée du désert, après la sortie d’Egypte, ne l’avaient pas été. 6Pendant quarante ans, les Israélites avaient marché dans le désert jusqu’à l’extinction de toute la génération des hommes en âge de porter les armes au moment de la sortie d’Egypte. En effet, parce qu’ils n’avaient pas obéi à l’Eternel, l’Eternel avait juré de ne pas leur laisser voir le pays qu’il avait promis par serment à leurs ancêtres de nous donner, ce pays ruisselant de lait et de miel. 7Mais il leur substitua leurs fils : ce sont eux que Josué circoncit puisqu’ils ne l’avaient pas été pendant la marche dans le désert.

8Après que tout le peuple eut été circoncis, ils restèrent sur place dans le camp jusqu’à leur guérison. 9Puis l’Eternel dit à Josué : Aujourd’hui, j’ai fait rouler loin de vous l’opprobre de l’Egypte.

C’est pourquoi cet endroit fut appelé Guilgal (Le roulement), nom qu’il a conservé jusqu’à ce jour.

La célébration de la Pâque – fin de la manne

10Pendant que les Israélites campaient à Guilgal, ils célébrèrent la Pâque le soir du quatorzième jour du mois, dans les plaines de Jéricho. 11Le lendemain, ils mangèrent des produits du pays : des pains sans levain et des épis grillés. 12A partir du lendemain de ce jour-là, la manne5.12 Voir Ex 16.13-35. cessa de tomber puisqu’ils pouvaient se nourrir des produits du pays ; il n’y eut plus de manne pour les Israélites qui vécurent des productions du pays de Canaan cette année-là.

L’arrivée du chef de l’armée de l’Eternel

13Un jour où Josué se trouvait près de Jéricho, il vit soudain un individu qui se tenait debout devant lui, avec son épée dégainée à la main. Josué s’avança vers lui et lui demanda : Es-tu des nôtres ou de nos ennemis ?

14– Non, répondit l’homme. Je suis le chef de l’armée de l’Eternel et je viens maintenant.

Alors Josué se prosterna, le visage contre terre, et lui dit : Seigneur, je suis ton serviteur, quels sont tes ordres ?

15Le chef de l’armée de l’Eternel lui répondit : Ote tes sandales de tes pieds, car l’endroit où tu te tiens est un lieu saint.

Et Josué obéit.