Yoswa 22 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 22:1-34

Mafuko a Kummawa Abwerera Kwawo

1Pambuyo pake Yoswa anayitanitsa fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase, 2ndipo anawawuza kuti, “Inu mwachita zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani, ndipo mwamvera mu zonse zimene ndinakulamulirani. 3Aisraeli anzanu simunawasiye nthawi yayitali yonseyi mpaka lero lino. Inu mwaonetsetsa kuti mwachita zonse zimene Yehova anakulamulani. 4Tsono pakuti Yehova Mulungu wanu wapereka mpumulo kwa abale anu monga anayankhulira nawo, bwererani ku nyumba zanu ku dziko limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani, dziko limene lili pa tsidya la Yorodani kummawa. 5Koma samalitsani kuti mumvere malamulo ndi malangizo amene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani: kukonda Yehova Mulungu wanu, kuchita zimene iye amafuna, kumvera malamulo ake, kukhala okhulupirika kwa Iye ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.”

6Ndipo Yoswa anawadalitsa ndi kuwalola kuti apite ndipo anapitadi ku nyumba zawo. 7Apa nʼkuti Mose atapereka dziko la Basani ku theka lina la fuko la Manase. Koma theka lina la fuko la Manase Yoswa analipatsa dziko la kumadzulo kwa Yorodani pamodzi ndi abale awo onse. Pamene Yoswa ankawatumiza kwawo anthu amenewa, anawadalitsa, 8nawawuza kuti, “Mukubwerera kwanu ndi chuma chambiri. Muli ndi ngʼombe zambiri pamodzi ndi siliva, golide, mkuwa ndi chitsulo, ndiponso zovala zambiri. Izi zimene munafunkha kwa adani anu agawireni abale anu.”

9Choncho mafuko a Rubeni, Gadi, pamodzi ndi theka la fuko la Manase anabwerera kwawo. Aisraeli ena onse anawasiya ku Silo mʼdziko la Kanaani. Tsono anapita ku dziko la Giliyadi, dziko limene linali lawo popeza analilandira potsata malamulo a Yehova kudzera mwa Mose.

10Atafika ku Geliloti, malo amene ali mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani mʼdziko la Kanaani, fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase anamanga guwa lansembe lalikulu pamenepo. 11Ndipo pamene Aisraeli ena onse anawuzidwa kuti anthu a fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase amanga guwa lansembe mʼmalire a Kanaani ku Geliloti, ku tsidya lathu lino la Yorodani, 12gulu lonse la Aisraeli linasonkhana ku Silo kuti lipite kukachita nawo nkhondo.

13Choncho Aisraeli anatumiza Finehasi mwana wa wansembe, Eliezara ku dziko la Giliyadi kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase. 14Pamodzi ndi Finehasiyo anatumiza akuluakulu khumi ochokera ku fuko lililonse la Aisraeli. Aliyense mwa akuluakulu amenewa anali mtsogoleri wa banja limodzi la mafuko a Aisraeli.

15Atafika ku Giliyadi anawuza fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lija la fuko la Manase kuti, 16“Gulu lonse likukufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani mwachita chinthu chonyansa chotere potsutsana ndi Mulungu wa Israeli? Nʼchifukwa chiyani mwapatuka ndi kuleka kutsata Yehova podzimangira nokha guwa lansembe? Mwapandukiratu Yehova! 17Kodi tchimo lija la ku Peori ndi lochepa kwa inu? Paja Yehova analanga gulu lonse ndi mliri chifukwa cha tchimolo, ndipo mpaka lero tchimo limene lija tikanazunzika nalobe. 18Kodi inu tsono mufuna kupatuka kuleka kumutsata Yehova?

“ ‘Ngati lero mumupandukira Yehovayo, ndiye kuti mawamawali Iye adzakwiyira gulu lonse wa Israeli. 19Ngati dziko limene inu mwatenga ndi loyipitsidwa, bwerani ku dziko la Yehova kumene kuli chihema chake kuja, ndipo mukhale nafe limodzi. Koma inu musawukire Yehova kapena kutisandutsa ife kukhala opanduka podzimangira guwa lansembe, kuwonjezera pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu. 20Kumbukirani pamene Akani mwana wa Zera anakana kumvera lamulo la zinthu zoyenera kuwonongedwa, kodi suja mkwiyo wa Yehova unagwera gulu lonse la Israeli? Akaniyo sanafe yekha chifukwa cha tchimo lakelo.’ ”

21Tsono mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawayankha atsogoleri a mabanja a Israeli aja kuti, 22“Wamphamvu uja, Mulungu ndiye Yehova! Wamphamvu uja Mulungu ndiye Yehova. Iyeyu ndiye akudziwa chifukwa chiyani tinachita zimenezi. Tikufunanso kuti inu mudziwe. Ngati tinachita izi mopandukira ndiponso moonetsa kusakhulupirira Yehova, lero lomwe lino musatisiye ndi moyo. 23Ngati tinapandukira Yehova ndi kuleka kumutsata pamene tinadzimangira guwa loti tizipserezerapo nsembe kapena kupereka nsembe zaufa, kapena nsembe za mtendere, Yehova yekha ndiye atilange.

24“Ayi! Ife tinachita izi kuopa kuti tsiku lina zidzukulu zanu zingadzanene kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Kodi inu mukufuna chiyani kwa Yehova Mulungu wa Israeli? 25Yehova anayika mtsinje wa Yorodani kukhala malire pakati pa ife ndi inu, anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi. Inuyo mulibe gawo mwa Yehova.’ Tsono mwina zidzukulu zanuzo nʼkudzaletsa zathu kupembedza Yehova.

26“Nʼchifukwa chake tinaganiza kuti, ‘Tiyeni timange guwa lansembe, koma osati kuti tiziperekapo nsembe zopsereza kapena zopereka.’ 27Koma mosiyana ndi zimenezi, guwali likhale umboni pakati pa ife ndi inu ndiponso mibado imene ikubwerayo, kuti ife timapembedzanso Yehova ndi nsembe zathu zopsereza, zopereka, ndiponso nsembe za mtendere. Motero mʼtsogolo muno zidzukulu zanu sizidzatha kunena kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Inu mulibe gawo mwa Yehova!’

28“Ndipo ife tinati kuti, ‘Ngati iwo adzatiyankhulira kapena kuyankhulira zidzukulu zathu motero mʼtsogolo muno, ife tidzayankha kuti, onani guwa lansembe, lofanana ndi lomwe makolo athu anamanga osati loperekerapo nsembe zopsereza kapena nsembe zina koma ngati umboni pakati pa inu ndi ife.’

29“Sizingatheke konse kuti ife lero nʼkupandukira Yehova. Ife sitingapatuke kuleka kumutsata Yehova ndi kumanga guwa lina la nsembe zopsereza, nsembe za zakudya, ndi nsembe zina zopikisana ndi guwa la Yehova, Mulungu wathu limene lili patsogolo pa Hema ya Yehova mʼmene amakhalamo.”

30Tsono Finehasi wansembe ndi atsogoleri a gululo amene anali naye atamva zimene anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lakummawa la fuko la Manase ananena, anakondwera kwambiri. 31Ndipo Finehasi wansembe, mwana wa Eliezara anati kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi Manase, “Lero tadziwa kuti Yehova ali nafe chifukwa zimene mwachitazi simunawukire nazo Yehova. Inu mwapulumutsa Aisraeli onse ku chilango cha Yehova.”

32Ndipo Finehasi mwana wa wansembe Eliezara, pamodzi ndi atsogoleriwo anachoka ku Giliyadi nasiya anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi nabwerera ku Kanaani kwa Aisraeli anzawo, ndipo anakafotokoza zonsezi. 33Mawu amenewa anakondweretsa Aisraeli onse ndipo anayamika Mulungu. Choncho sanakambenso zopita ku nkhondo kukawononga dziko limene Arubeni ndi Agadi ankakhalamo.

34Arubeni ndi Agadi anatcha guwalo kuti Mboni: Mboni pakati pathu kuti Yehova ndi Mulungu.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Иешуа 22:1-34

Восточные роды возвращаются на свои земли

1Иешуа созвал роды Рувима, Гада и половину рода Манассы 2и сказал им:

– Вы исполнили всё, что повелел вам Муса, раб Вечного, и были послушны мне во всём, что я вам повелевал. 3Долгое время, до этого самого дня, вы не оставляли своих братьев, но несли служение, которое дал вам Вечный, ваш Бог. 4Теперь Вечный, ваш Бог, дал вашим братьям покой, как Он и обещал. Поэтому возвращайтесь домой, в землю, которую Муса, раб Вечного, дал вам на другой стороне Иордана. 5Только прилежно исполняйте повеления и Закон, которые дал вам Муса, раб Вечного: любите Вечного, вашего Бога, ходите всеми Его путями, храните Его повеления, крепко держитесь Его и служите Ему от всего сердца и от всей души.

6Иешуа благословил и отпустил их, и они вернулись в свои шатры. 7(Одной половине рода Манассы Муса дал землю в Башане, а другой половине рода Иешуа дал землю рядом с их братьями на западной стороне Иордана.) Отпуская домой, Иешуа благословил их, 8сказав:

– Возвращайтесь домой со своим великим богатством – большими стадами, серебром, золотом, бронзой, и железом, и великим множеством одежд – и поделитесь со своими братьями добычей, взятой вами у врагов.

9И роды Рувима, Гада и половина рода Манассы оставили исраильтян в Шило, что в Ханаане, чтобы вернуться в Галаад, в свою землю, которой они завладели по повелению Вечного, данному через Мусу.

Жертвенник «Свидетель»

10Придя в Гелилот, что рядом с Иорданом, в земле Ханаана, роды Рувима, Гада и половина рода Манассы соорудили у Иордана огромный жертвенник. 11Когда исраильтяне услышали, что те соорудили на границе Ханаана в Гелилоте, что рядом с Иорданом на исраильской стороне, жертвенник, 12весь народ Исраила собрался в Шило, чтобы идти на них войной.

13Исраильтяне послали в землю Галаада, к родам Рувима, Гада и половине рода Манассы, Пинхаса, сына священнослужителя Элеазара. 14С ним отправилось десять вождей, по одному от каждого из исраильских родов, каждый из них был главой семейства среди исраильских кланов.

15Когда они пришли в Галаад – к родам Рувима, Гада и половине рода Манассы, – они сказали им:

16– Всё общество Вечного говорит: «Как вы могли совершить такое предательство против Бога Исраила? Как вы могли отступить от Вечного и соорудить себе жертвенник, восстав ныне против Вечного? 17Разве не было с нас довольно греха Пеора?22:17 См. Чис. 25:1-9. До этого самого дня мы ещё не очистились от того греха, за который весь народ Вечного поразил мор! 18А сегодня вы собираетесь отступить от Вечного? Если сегодня вы восстанете против Вечного, то завтра Он разгневается на весь народ Исраила. 19Если ваша земля нечиста, то перейдите в землю Вечного, где стоит священный шатёр Вечного, и разделите землю с нами. Только не восставайте против Вечного и против нас22:19 Или: «и не делайте мятежниками и нас»., сооружая себе иной жертвенник, нежели жертвенник Вечного, нашего Бога. 20Разве, когда Ахан, правнук Зераха, нечестно поступил с подлежащими уничтожению вещами, не обрушился гнев на весь народ Исраила? А за тот грех умер не он один».

21Рувимиты, гадиты и половина рода Манассы ответили главам исраильских кланов:

22– Вечный – Бог богов! Вечный – Бог богов! Он знает, и Исраил пусть знает, – если это было восстание или предательство против Вечного, то не щадите22:22 Или: «пусть Он не пощадит». нас сегодня. 23Если мы построили свой собственный жертвенник, чтобы, отступив от Вечного, приносить на нём всесожжения и хлебные приношения или совершать жертвы примирения, то пусть Сам Вечный призовёт нас к ответу. 24Нет! Мы сделали это из страха, что однажды ваши потомки могут сказать нашим: «Что вам до Вечного, Бога Исраила? 25Вечный сделал Иордан границей между нами и вами, рувимиты и гадиты! Нет у вас доли в Вечном». Так ваши потомки могут заставить наших перестать чтить Вечного.

26Вот почему мы сказали: «Приготовимся и соорудим жертвенник, но не для всесожжений или жертвоприношений». 27Напротив, пусть он будет свидетелем между нами и вами и грядущими поколениями, что мы чтим Вечного в Его святилище своими всесожжениями, приношениями и жертвами примирения. Тогда в будущем ваши потомки не смогут сказать нашим: «Нет у вас доли в Вечном». 28Мы решили, что если они когда-нибудь скажут это нам или нашим потомкам, то мы ответим: «Посмотрите на жертвенник, который соорудили наши отцы по образу жертвенника Вечного не для всесожжений или приношений, но для свидетельства между нами и вами».

29Да не будет того, чтобы нам сегодня восстать против Вечного и отступить от Него, соорудив иной жертвенник для всесожжений, хлебных приношений и жертв примирения, нежели тот жертвенник Вечного, нашего Бога, что находится перед Его священным шатром.

30Когда священнослужитель Пинхас и вожди народа, главы исраильских кланов, услышали, что сказали рувимиты, гадиты и половина рода Манассы, они были удовлетворены. 31И священнослужитель Пинхас, сын Элеазара, сказал рувимитам, гадитам и половине рода Манассы:

– Сегодня мы узнали, что Вечный с нами, что вы не совершили против Вечного этого предательства. Теперь вы избавили исраильтян от руки Вечного.

32И священнослужитель Пинхас, сын Элеазара, возвратился вместе с вождями от рувимитов и гадитов в Галааде и принёс от них ответ в Ханаан, к исраильтянам. 33Те были рады услышать эту весть и возблагодарили Аллаха. И больше они не говорили о том, чтобы пойти войной на страну, где живут рувимиты и гадиты, и опустошить её.

34А рувимиты и гадиты назвали жертвенник «Свидетель», потому что они говорили: «Это свидетель между нами, что Вечный – наш Бог».