Yoswa 10 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 10:1-43

Kuyimitsidwa kwa Dzuwa

1Adoni-Zedeki mfumu ya ku Yerusalemu inamva kuti Yoswa wagonjetsa ndi kuwononga kotheratu mzinda wa Ai pamodzi ndi mfumu yake, monga anachitira ndi Yeriko ndi mfumu yake. Inamvanso kuti anthu a ku Gibiyoni anachita pangano la mtendere ndi Israeli ndipo amakhala pakati pawo. 2Choncho iye ndi anthu ake anachita mantha aakulu, chifukwa Gibiyoni unali mzinda waukulu kwambiri, monga mzinda uliwonse wokhala ndi mfumu. Unali waukulu ndipo ankhondo ake anali olimba mtima. 3Chotsatira chake Adoni-Zedeki mfumu ya Yerusalemu inatuma uthenga kwa Hohamu mfumu ya Hebroni, Piramu mfumu ya Yarimuti, Yafiya mfumu ya Lakisi ndi Debri mfumu ya Egiloni. 4Iye anatumiza mawu kuti, “Bwerani mudzandithandize kumenyana ndi Gibiyoni, chifukwa anthu ake achita pangano la mtendere ndi Yoswa ndi Aisraeli.”

5Mafumu asanu a Aamori aja, mfumu ya Yerusalemu, mfumu ya Hebroni, mfumu ya Yarimuti, mfumu ya Lakisi ndi mfumu ya Egiloni, anagwirizana. Iwo anasonkhanitsa ankhondo awo nazungulira mzinda wa Gibiyoni ndi kuwuthira nkhondo.

6Koma anthu a ku Gibiyoni anatumiza uthenga kwa Yoswa ku misasa ya ku Giligala nati, “Musawataye anthu anu! Bwerani msanga mudzatipulumutse! Dzatithandizeni chifukwa mafumu a Aamori ochokera ku dziko la ku mapiri agwirizana kuti adzatithire nkhondo.”

7Choncho Yoswa ananyamuka kuchoka ku Giligala ndi gulu lake la ankhondo pamodzi ndi anthu ake olimba mtima. 8Yehova anati kwa Yoswa, “Usawaope, Ine ndawapereka mʼdzanja lako. Palibe ndi mmodzi mwa amenewa amene adzalimbe.”

9Atayenda usiku wonse kuchokera ku Giligala, Yoswa anawathira nkhondo mwadzidzidzi. 10Yehova anachititsa mantha adani aja atangoona gulu lankhondo la Israeli. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamori ku Gibiyoni ndipo anawathamangitsa mu msewu wopita ku Beti-Horoni ndi kuwapha njira yonse yopita ku Azeka ndi Makeda. 11Pamene ankathawa pamaso pa Israeli pa njira yochokera ku Beti-Horoni mpaka ku Azeka, Yehova anawagwetsera matalala akuluakulu kuchokera kumwamba ndipo ambiri mwa iwo anafa ndi matalala kuposa amene anaphedwa ndi lupanga la Israeli.

12Pa tsiku limene Yehova anapereka Aamori mʼmanja mwa Israeli, Yoswa ananena kwa Yehova pamaso pa Israeli kuti,

“Iwe dzuwa, ima pamwamba pa Gibiyoni,

mwezi ima pamwamba pa chigwa cha Ayaloni.”

13Choncho dzuwa linayima,

mwezinso unayima,

mpaka dziko la Israeli litagonjetsa adani ake.

Zimenezi zalembedwa mʼbuku la Yasari.

Dzuwa linayima pamodzimodzi pakati pa thambo mlengalenga, osayendanso kwa tsiku lathunthu. 14Sipanakhaleponso tsiku ngati limeneli kuyambira kale, tsiku limene Yehova anamvera munthu. Izi zinatero chifukwa Yehova ankamenyera nkhondo Aisraeli.

15Kenaka Yoswa anabwerera pamodzi ndi Aisraeli onse ku misasa ku Giligala.

Kuphedwa kwa Mafumu Asanu a Aamori

16Mafumu asanu aja anathawa ndi kukabisala ku phanga la Makeda. 17Koma Yoswa anamva kuti mafumu asanu awapeza akubisala ku phanga la Makeda. 18Tsono Yoswa analamula kuti, “Mugubuduzire miyala ikuluikulu pa khomo la phangalo, ndipo muyike anthu ena kuti azilondera. 19Koma inu musakhaleko! Thamangitsani adani anu, muwathire nkhondo kuchokera kumbuyo ndipo musawalole kuti akafike ku mizinda yawo, pakuti Yehova Mulungu wanu wawapereka mʼmanja mwanu.”

20Kotero Yoswa ndi Aisraeli anapha anthu aja, kupatulapo ochepa amene anathawa nakabisala ku mizinda yawo. 21Kenaka gulu lonse la ankhondo linabwerera bwinobwino kwa Yoswa ku misasa ya ku Makeda, palibe aliyense mu mzindamo amene anaputanso Aisraeli.

22Yoswa anati, “Tsekulani khomo la phangalo ndipo muwabweretse kwa ine mafumu asanuwo.” 23Pamenepo mafumu asanu aja anatulutsidwa, mfumu ya ku Yerusalemu, mfumu ya ku Hebroni, mfumu ya ku Yarimuti, mfumu ya ku Lakisi, ndi mfumu ya ku Egiloni. 24Atabwera nawo kwa Yoswa, iye anayitana Aisraeli onse. Ndipo analamula akuluakulu ake amene anapita naye limodzi kuti, “Bwerani kuno ndipo apondeni pakhosi mafumuwa.”

25Yoswa anawawuza kuti, “Musaope kapena kutaya mtima. Khalani amphamvu ndi olimba mtima popeza umo ndi mmene Yehova adzachitire ndi adani anu onse amene mudzamenyana nawo.” 26Kenaka Yoswa anawabaya ndi kuwapha mafumuwo ndipo anawapachika pa mitengo isanu ndipo anakhala pamenepo mpaka madzulo.

27Dzuwa litalowa, Yoswa analamula kuti awachotse pa mitengo ija ndi kuwaponya mʼphanga limene ankabisalamo. Pa khomo pa phangalo anayikapo miyala ikuluikulu imene ilipo mpaka lero.

28Tsiku lomwelo Yoswa analanda mzinda wa Makeda. Iye anapha anthu a mu mzindamo ndi mfumu yake ndipo sanasiye aliyense wamoyo. Yoswa anachita ndi mfumu ya ku Makeda monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.

Agonjetsa Mizinda ya Kummwera

29Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Makeda nakafika ku Libina ndi kuthira nkhondo mzindawo. 30Yehova anaperekanso mzindawo ndi mfumu yake mʼmanja mwa Aisraeli. Ndipo Yoswa anapha onse amene anali mu mzindamo. Palibe amene anatsala wamoyo. Ndipo Yoswa anachita ndi mfumu ya Libina monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.

31Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Libina kupita ku Lakisi. Iye anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo. 32Yehova anapereka Lakisi kwa Israeli; ndipo Yoswa anawulanda pa tsiku lachiwiri. Monga anachita ndi mzinda wa Libina, Yoswa anapha anthu onse okhala mu mzinda wa Lakisi, ndipo palibe amene anatsala ndi moyo. 33Nthawi imeneyi nʼkuti Horamu mfumu ya Gezeri itabwera kudzathandiza Lakisi koma Yoswa anamugonjetsa pamodzi ndi asilikali ake ndipo palibe anatsala wamoyo.

34Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Lakisi nakafika ku Egiloni. Iwo anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo. 35Anawulanda tsiku lomwelo ndipo anapha aliyense amene anali mu mzindawo monga momwe anachitira ku Lakisi.

36Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anachoka ku Egiloni nakafika ku Hebroni ndi kukawuthira nkhondo. 37Iwo analanda mzindawo napha ndi lupanga mfumu yake pamodzi ndi onse amene ankakhala mʼmenemo. Monga anachita ndi mzinda wa Egiloni, kuti sanasiye aliyense ndi moyo, anachitanso chimodzimodzi ndi mzinda wa Hebroni.

38Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anatembenukira mzinda wa Debri ndi kukawuthira nkhondo. 39Iwo analanda mzindawo ndi midzi ndi kupha mfumu yake pamodzi ndi onse okhala mʼmenemo. Anachita ndi mzinda wa Debri pamodzi ndi mfumu yake zofanana ndi zimene anachita ndi mzinda wa Libina ndi wa Hebroni.

40Motero Yoswa anagonjetsa dziko lonselo. Anapha mafumu onse a dera la kumapiri, dera la kummawa, dera la kumadzulo mʼmphepete mwa phiri, ndiponso dera la ku magomo, kummwera. Iye sanasiye wina aliyense wamoyo. Anapha onse amene anali moyo monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli analamulira. 41Yoswa anawagonjetsa iwo kuyambira ku Kadesi Barinea mpaka ku Gaza, ndiponso kuchokera ku chigawo chonse cha Goseni mpaka ku Gibiyoni. 42Yoswa anagonjetsa mafumu onsewa ndi kulanda dziko lawo kamodzinʼkamodzi chifukwa Yehova Mulungu wa Israeli anawamenyera nkhondo.

43Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anabwerera ku misasa yawo ku Giligala.

La Bible du Semeur

Josué 10:1-43

La bataille de Gabaon

1Adoni-Tsédeq, roi de Jérusalem, apprit que Josué s’était emparé d’Aï et l’avait totalement détruite pour la vouer à l’Eternel, en faisant subir à cette ville et à son roi le même sort qu’à Jéricho et à son roi. Il entendit également que les habitants de Gabaon avaient fait la paix avec les Israélites et qu’ils vivaient au milieu d’eux. 2Alors il fut saisi d’une grande peur, car Gabaon était une ville importante, comme les villes royales, plus grande qu’Aï, et tous ses hommes étaient des guerriers. 3C’est pourquoi Adoni-Tsédeq, roi de Jérusalem, envoya des messagers à Hoham, roi d’Hébron, à Piream, roi de Yarmouth, à Yaphia, roi de Lakish et à Debir, roi de Eglôn10.3 Toutes ces villes se situaient à quelques kilomètres les unes des autres. Elles constituaient les cinq villes les plus importantes de la région montagneuse du sud du pays., pour leur faire dire : 4Venez me prêter main-forte pour attaquer Gabaon, puisque ses habitants ont conclu la paix avec Josué et les Israélites.

5C’est ainsi que cinq rois des Amoréens, ceux de Jérusalem, d’Hébron, de Yarmouth, de Lakish et de Eglôn formèrent une coalition et marchèrent à la tête de toutes leurs armées contre Gabaon. Ils établirent leur camp devant la ville et engagèrent les hostilités.

6Les habitants de Gabaon envoyèrent des messagers à Josué au camp de Guilgal pour lui faire dire : N’abandonne pas tes serviteurs. Viens vite à notre secours, sauve-nous, car tous les rois amoréens de la région montagneuse se sont ligués contre nous10.6 L’alliance conclue avec Josué (9.11-15) impliquait l’assistance militaire de la nation suzeraine à ses vassaux si ceux-ci étaient attaqués..

7Josué vint depuis Guilgal avec toute son armée et ses plus valeureux guerriers.

8L’Eternel dit à Josué : N’aie pas peur de ces rois, car je te donne la victoire sur eux ; aucun d’eux ne pourra te résister.

9Après avoir marché toute la nuit depuis Guilgal10.9 Parcourant une trentaine de kilomètres pendant la nuit., Josué tomba sur eux à l’improviste. 10L’Eternel les mit en déroute devant Israël et leur fit essuyer une grande défaite devant Gabaon ; les Israélites les battirent en les poursuivant sur la montée de Beth-Horôn10.10 De Gabaon à Beth-Horôn vers le village de Beth-Horôn-la-Haute, le chemin monte pendant deux heures, puis il descend par un sentier abrupt et rocailleux du col de Beth-Horôn-la-Basse. C’est sur ce sentier que Josué poursuivit les fuyards pendant que les grêlons pleuvaient sur eux. et jusqu’à Azéqa et Maqqéda. 11Pendant que les Amoréens s’enfuyaient devant Israël sur la pente qui descend de Beth-Horôn, l’Eternel fit tomber sur eux du ciel d’énormes grêlons qui, jusqu’à Azéqa, firent encore plus de victimes que les épées des Israélites.

12Ce jour-là où l’Eternel donna aux Israélites la victoire sur les Amoréens, Josué s’écria devant tout Israël : Soleil, arrête-toi sur Gabaon ! Et toi, lune, fais halte sur la vallée d’Ayalôn.

13Et le soleil s’arrêta, la lune suspendit son cours jusqu’à ce que le peuple d’Israël eût réglé ses comptes avec ses ennemis. C’est bien ce qui est écrit dans le livre du Juste10.13 Voir 2 S 1.18.. Le soleil s’immobilisa au milieu du ciel et différa son coucher pendant environ un jour entier. 14Jamais auparavant et jamais depuis lors, il n’y eut de jour comparable à celui-là, où l’Eternel a écouté la voix d’un homme. C’est qu’il combattait lui-même pour Israël. 15Après cela, Josué et toute l’armée d’Israël regagnèrent le camp de Guilgal.

La capture et l’exécution des rois vaincus

16Or, pendant la bataille, les cinq rois avaient réussi à s’enfuir et ils s’étaient cachés dans la grotte de Maqqéda. 17On les découvrit cachés dans cette grotte et on vint en informer Josué 18qui donna l’ordre suivant : Roulez de grandes pierres à l’entrée de la grotte et postez-y des hommes pour monter la garde, 19mais ne vous y attardez pas : poursuivez vos ennemis et coupez-leur la retraite ! Ne les laissez pas rentrer dans leurs villes puisque l’Eternel votre Dieu les livre en votre pouvoir !

20Josué et les Israélites leur infligèrent une cuisante défaite et achevèrent de les exterminer tous, à part quelques rescapés qui purent regagner leurs villes fortifiées. 21Puis tout le peuple revint sain et sauf auprès de Josué au camp établi à Maqqéda. Après cela, plus personne dans le pays n’osa parler contre les Israélites.

22Josué ordonna de dégager l’entrée de la grotte et d’en faire sortir les cinq rois pour les lui amener. 23On fit ainsi et on lui amena les cinq rois qui se trouvaient dans la caverne, les rois de Jérusalem, d’Hébron, de Yarmouth, de Lakish et de Eglôn. 24Pendant qu’on les faisait sortir pour les lui amener, Josué convoqua tous les hommes d’Israël et dit aux chefs des soldats qui avaient combattu avec lui : Approchez-vous et posez vos pieds sur la nuque de ces rois.

Les chefs s’avancèrent et firent ainsi. 25Josué reprit : N’ayez pas peur, ne vous laissez pas effrayer ! Prenez courage et tenez bon ! Car c’est ainsi que l’Eternel traitera tous vos ennemis contre lesquels vous combattrez.

26Après cela, Josué les mit à mort et les fit pendre à cinq arbres. Ils y restèrent pendus jusqu’au soir. 27Au moment du coucher du soleil, il ordonna de descendre leurs corps et de les jeter dans la grotte où les rois s’étaient cachés. Ensuite, on en boucha l’entrée avec de grandes pierres qui s’y trouvent encore aujourd’hui10.27 Voir Dt 21.22-23..

La conquête de la partie sud du pays

28Le même jour, Josué s’empara de Maqqéda, il la frappa du tranchant de l’épée, il exécuta son roi et extermina tous les êtres vivants qui s’y trouvaient sans laisser aucun survivant pour les vouer à l’Eternel. Il traita le roi de Maqqéda comme il avait traité celui de Jéricho.

29De Maqqéda, Josué et tout Israël avec lui passèrent à Libna qu’ils attaquèrent. 30L’Eternel la livra aussi, elle et son roi, au pouvoir des Israélites, ils tuèrent tous les êtres vivants qui s’y trouvaient sans laisser aucun survivant. Josué traita son roi comme il avait traité celui de Jéricho.

31De Libna, Josué et tout Israël avec lui passèrent à Lakish. Ils établirent leur camp devant la ville et l’attaquèrent. 32L’Eternel la livra en leur pouvoir et ils s’en emparèrent le second jour ; ils la frappèrent du tranchant de l’épée et tuèrent tous les êtres vivants qui s’y trouvaient comme ils l’avaient fait à Libna. 33Horam, le roi de Guézer, vint au secours de Lakish, mais Josué le battit, lui et son armée, sans lui laisser aucun survivant.

34De Lakish, Josué et tout Israël avec lui se dirigèrent vers Eglôn, ils établirent leur camp devant la ville et l’attaquèrent. 35Ils s’en emparèrent le même jour et la frappèrent du tranchant de l’épée, ils exécutèrent tous les êtres vivants qui s’y trouvaient pour les vouer à l’Eternel, comme ils l’avaient fait à Lakish.

36De Eglôn, Josué et tout Israël avec lui se rendirent à Hébron et l’attaquèrent10.36 Située dans la vallée et occupée par des Hittites (voir note 1.4).. 37Ils s’en emparèrent et tuèrent son roi, et tous les êtres vivants qui s’y trouvaient ainsi que dans les villes qui en dépendaient. Il n’y resta aucun survivant, comme ils l’avaient fait à Eglôn. Josué détruisit la ville et extermina tous les êtres vivants qui s’y trouvaient pour les vouer à l’Eternel. 38Après cela, Josué et tout Israël avec lui revinrent sur Debir et l’attaquèrent. 39Ils s’emparèrent de la ville, capturèrent son roi et prirent toutes les villes qui en dépendaient. Ils exterminèrent tous les êtres vivants qui s’y trouvaient pour les vouer à l’Eternel et n’y laissèrent aucun survivant, comme à Hébron. Josué traita Debir et son roi comme il avait traité Libna et son roi.

40Josué conquit tout le pays, il battit tous les rois de la région montagneuse, ceux du Néguev, de la plaine côtière et des contreforts des montagnes. Il extermina tous les êtres vivants sans épargner personne, pour les vouer à l’Eternel, comme l’Eternel, le Dieu d’Israël, l’avait ordonné. 41Il soumit toute la région de Qadesh-Barnéa jusqu’à Gaza, et le district de Goshen10.41 Ville de la montagne (11.16 ; 15.51), à ne pas confondre avec la région égyptienne du delta du Nil (Gn 45.10). jusqu’à Gabaon. 42En une seule campagne, il vainquit tous les rois et s’empara de leurs territoires, car l’Eternel, le Dieu d’Israël, combattait pour son peuple. 43Ensuite, Josué et tout Israël avec lui regagnèrent le camp de Guilgal.