Yona 2 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yona 2:1-10

Pemphero la Yona

1Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake. 2Iye anati:

“Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova,

ndipo Iye anandiyankha.

Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo,

ndipo Inu munamva kulira kwanga.

3Munandiponya mʼnyanja yozama,

mʼkati mwenimweni mwa nyanja,

ndipo madzi oyenda anandizungulira;

mafunde anu onse ndi mkokomo wake

zinandimiza.

4Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa

pamaso panu;

komabe ndidzayangʼananso

ku Nyumba yanu yopatulika.’

5Madzi wondimiza anandichititsa mantha,

nyanja yozama inandizungulira;

udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.

6Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri;

mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha.

Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo,

Inu Yehova Mulungu wanga.

7“Pamene moyo wanga umachoka mwa ine,

ine ndinakumbukira Inu Yehova,

ndipo pemphero langa linafika kwa inu,

ku Nyumba yanu yopatulika.

8“Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe

amataya chisomo chawo.

9Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe

ndikuyimba nyimbo yamayamiko.

Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa.

Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”

10Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.

Nueva Versión Internacional

Jonás 2:1-10

1Entonces Jonás oró al Señor su Dios desde el vientre del pez. 2Dijo:

«En mi angustia clamé al Señor,

y él me respondió.

Desde lo profundo de los dominios de la muerte2:2 de los dominios de la muerte. Lit. del Seol. pedí auxilio,

y tú escuchaste mi clamor.

3A lo profundo me arrojaste,

al corazón mismo de los mares;

las corrientes me envolvían,

todas tus ondas y tus olas

pasaban sobre mí.

4Y pensé: “He sido expulsado

de tu presencia;

pero volveré a contemplar

tu santo Templo”.2:4 pero … Templo. Alt. ¿Cómo volveré a contemplar tu santo Templo?

5Las aguas me llegaban hasta el cuello,

lo profundo del mar me envolvía;

las algas se me enredaban en la cabeza,

6arrastrándome a los cimientos de las montañas.

Me tragó la tierra y para siempre

sus cerrojos se cerraron tras de mí.

Pero tú, Señor, Dios mío,

rescataste mi vida de la fosa.

7»Al sentir que se me iba la vida,

me acordé del Señor,

y mi oración llegó hasta ti,

hasta tu santo Templo.

8»Los que siguen a ídolos vanos

abandonan el amor de Dios.2:8 abandonan el amor de Dios. Alt. desprecian la misericordia suya.

9Yo, en cambio, te ofreceré sacrificios

y cánticos de gratitud.

Cumpliré las promesas que te hice.

¡La salvación viene del Señor!».

10Entonces el Señor dio una orden y el pez vomitó a Jonás en tierra firme.