Yona 2 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yona 2:1-10

Pemphero la Yona

1Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake. 2Iye anati:

“Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova,

ndipo Iye anandiyankha.

Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo,

ndipo Inu munamva kulira kwanga.

3Munandiponya mʼnyanja yozama,

mʼkati mwenimweni mwa nyanja,

ndipo madzi oyenda anandizungulira;

mafunde anu onse ndi mkokomo wake

zinandimiza.

4Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa

pamaso panu;

komabe ndidzayangʼananso

ku Nyumba yanu yopatulika.’

5Madzi wondimiza anandichititsa mantha,

nyanja yozama inandizungulira;

udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.

6Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri;

mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha.

Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo,

Inu Yehova Mulungu wanga.

7“Pamene moyo wanga umachoka mwa ine,

ine ndinakumbukira Inu Yehova,

ndipo pemphero langa linafika kwa inu,

ku Nyumba yanu yopatulika.

8“Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe

amataya chisomo chawo.

9Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe

ndikuyimba nyimbo yamayamiko.

Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa.

Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”

10Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.

King James Version

Jonah 2:1-10

1Then Jonah prayed unto the LORD his God out of the fish’s belly, 2And said, I cried by reason of mine affliction unto the LORD, and he heard me; out of the belly of hell cried I, and thou heardest my voice.2.2 by…: or, out of mine affliction2.2 hell: or, the grave 3For thou hadst cast me into the deep, in the midst of the seas; and the floods compassed me about: all thy billows and thy waves passed over me.2.3 midst: Heb. heart 4Then I said, I am cast out of thy sight; yet I will look again toward thy holy temple. 5The waters compassed me about, even to the soul: the depth closed me round about, the weeds were wrapped about my head. 6I went down to the bottoms of the mountains; the earth with her bars was about me for ever: yet hast thou brought up my life from corruption, O LORD my God.2.6 bottoms: Heb. cuttings off2.6 corruption: or, the pit 7When my soul fainted within me I remembered the LORD: and my prayer came in unto thee, into thine holy temple. 8They that observe lying vanities forsake their own mercy. 9But I will sacrifice unto thee with the voice of thanksgiving; I will pay that that I have vowed. Salvation is of the LORD.

10¶ And the LORD spake unto the fish, and it vomited out Jonah upon the dry land.