Yohane 6 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 6:1-71

Yesu Adyetsa Anthu 5,000

1Nthawi ina zitatha izi, Yesu anawolokera ku gombe la kutali la nyanja ya Galileya (iyi ndi nyanja ya Tiberiya), 2ndipo gulu lalikulu la anthu linamutsata Iye chifukwa linaona zizindikiro zodabwitsa zimene anazichita pa odwala. 3Kenaka Yesu anakwera pa phiri nakhala pansi ndi ophunzira ake. 4Tsopano phwando la Paska la Ayuda linali pafupi.

5Yesu atakweza maso ndi kuona gulu lalikulu la anthu likubwera kwa Iye, anati kwa Filipo, “Kodi tingagule kuti buledi kuti anthu awa adye?” 6Iye anafunsa izi kumuyesa chabe, pakuti Iye ankadziwa chimene ankayenera kuchita.

7Filipo anamuyankha Iye kuti, “Malipiro a miyezi isanu ndi itatu sangathe kugula buledi okwanira aliyense kuti adye!”

8Mmodzi wa ophunzira ake, Andreya, mʼbale wa Simoni Petro, anati, 9“Pano pali mnyamata amene ali ndi buledi musanu wabarele ndi tinsomba tiwiri, kodi zingakwane onsewa?”

10Yesu anati, “Awuzeni anthuwa akhale pansi.” Pamalo pamenepa panali udzu wambiri ndipo amuna amene anakhala pansi anali osachepera 5,000. 11Kenaka Yesu anatenga bulediyo, atayamika anagawira iwo amene anakhala pansi, chimodzimodzinso nsombazo monga momwe iwo anafunira.

12Ndipo atakhuta, Iye anati kwa ophunzira ake, “Tolani zotsala kuti pasawonongeke kanthu.” 13Choncho iwo anasonkhanitsa makombo nadzaza madengu khumi ndi awiri.

14Pambuyo pake anthu ataona chizindikiro chodabwitsa chimene Yesu anachita, iwo anati, “Zoonadi uyu ndi Mneneri wakudzayo mʼdziko la pansi.” 15Yesu atadziwa kuti iwo amafuna kubwera kudzamuwumiriza kuti akhale mfumu, anachoka napita ku phiri pa yekha.

Yesu Ayenda pa Madzi

16Pofika madzulo, ophunzira ake anatsikira ku nyanja, 17kumene iwo analowa mʼbwato ndi kuyamba kuwoloka nyanja kupita ku Kaperenawo. Tsopano kunali kutada ndipo Yesu anali asanabwerere kwa iwo. 18Mphepo yamphamvu inawomba ndipo nyanja inalusa. 19Iwo atayenda makilomita asanu kapena asanu ndi limodzi, anaona Yesu akuyandikira bwatolo, akuyenda pa madzi; ndipo anachita mantha. 20Koma Iye anawawuza kuti, “Ndine, musaope.” 21Ndipo iwo analola kumutenga mʼbwatomo, nthawi yomweyo bwatolo linafika ku gombe la nyanja kumene ankapita.

22Pa tsiku lotsatira gulu la anthu limene linatsala kumbali ina yanyanjayo linaona kuti panali bwato limodzi lokha, ndipo kuti Yesu sanalowe mʼbwatomo pamodzi ndi ophunzira ake, koma kuti ophunzirawo anapita okha. 23Kenaka mabwato ena ochokera ku Tiberiya anafika pafupi ndi pamalo pamene anthu anadya buledi Ambuye atayamika. 24Nthawi yomwe gulu la anthu linaona kuti Yesu kapena ophunzira ake sanali pamenepo, ilo linalowanso mʼmabwatowo ndi kupita ku Kaperenawo kukamufunafuna Yesu.

Yesu Chakudya Chamoyo

25Atamupeza mbali ina ya nyanjayo, iwo anamufunsa Iye kuti, “Rabi, mwafika nthawi yanji kuno?”

26Yesu anawayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mukundifuna, osati chifukwa munaona zizindikiro zodabwitsa koma chifukwa munadya chakudya ndi kukhuta. 27Gwirani ntchito, osati chifukwa cha chakudya chimene chimawonongeka koma chifukwa cha chakudya chimene sichiwonongeka mpaka ku moyo wosatha, chimene Mwana wa Munthu adzakupatsani. Mulungu Atate anamusindikiza chizindikiro chomuvomereza.”

28Kenaka anamufunsa Iye kuti, “Kodi tichite chiyani kuti tigwire ntchito za Mulungu?”

29Yesu anayankha kuti, “Ntchito ya Mulungu ndi iyi: Kukhulupirira Iye amene anamutuma.”

30Choncho iwo anamufunsa Iye kuti, “Kodi mudzatipatsa chizindikiro chodabwitsa chotani kuti ife tichione ndi kukhulupirira Inu? Kodi mudzachita chiyani? 31Makolo athu akale anadya mana mʼchipululu; monga zalembedwa: ‘anawapatsa buledi wochokera kumwamba kuti adye.’ ”

32Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti si Mose amene ankakupatsani chakudya chochokera kumwamba, koma ndi Atate anga amene ankakupatsani chakudya chenicheni chochokera kumwamba. 33Pakuti chakudya cha Mulungu ndi Iye amene wabwera kuchokera kumwamba ndi kupereka moyo ku dziko la pansi.”

34Iwo anati, “Ambuye, kuyambira tsopano muzitipatsa buledi ameneyu.”

35Kenaka Yesu ananenetsa kuti, “Ine ndine chakudya chamoyo. Iye amene abwera kwa Ine sadzamva njala, ndipo iye amene akhulupirira Ine sadzamva ludzu. 36Monga ndakuwuzani kale, ngakhale kuti mwandiona simukukhulupirirabe. 37Zonse zimene Atate andipatsa zidzabwera kwa Ine, ndipo aliyense amene adzabwera kwa Ine sindidzamutaya kunja. 38Pakuti Ine ndinatsika kuchokera kumwamba osati kudzachita chifuniro changa koma cha Iye amene anandituma Ine. 39Ndipo chifuniro cha Iye amene anandituma Ine nʼchakuti ndisatayepo ngakhale ndi mmodzi yemwe mwa onse amene Iye wandipatsa, koma kuti ndidzawaukitse kwa akufa pa tsiku lomaliza. 40Pakuti chifuniro cha Atate anga ndi chakuti aliyense amene aona Mwanayo namukhulupirira akhale ndi moyo wosatha, ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza.”

41Pamenepo Ayuda anayamba kungʼungʼudza chifukwa anati, “Ine ndine chakudya chotsika kuchokera kumwamba.” 42Iwo anati, “Kodi uyu si Yesu, mwana wa Yosefe, amene abambo ake ndi amayi ake timawadziwa? Nanga Iyeyu akunena bwanji kuti, ‘Ine ndinatsika kuchokera kumwamba?’ ”

43Yesu anayankha kuti, “Musangʼungʼudze pakati panu.” 44Palibe munthu amene angabwere kwa Ine, ngati Atate amene anandituma Ine samubweretsa. Ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza. 45Aneneri analemba kuti, “Onse adzaphunzitsidwa ndi Mulungu! Aliyense amene amamva Atate ndi kuphunzira kwa Iye amabwera kwa Ine. 46Palibe amene anaona Atate koma yekhayo amene achokera kwa Mulungu; yekhayo ndiye anaona Atate. 47Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti Iye amene akhulupirira ali nawo moyo wosatha. 48Ine ndine chakudya chamoyo. 49Makolo anu akale anadya mana mʼchipululu, komabe anafa. 50Koma pano pali chakudya chochokera kumwamba, chimene munthu akadya sangafe. 51Ine ndine chakudya chamoyo chochokera kumwamba. Ngati munthu adya chakudya ichi, adzakhala ndi moyo nthawi zonse. Chakudya chimenechi ndi thupi langa, limene Ine ndidzalipereka kuti anthu pa dziko lapansi akhale ndi moyo.”

52Kenaka Ayuda anayamba kutsutsana kwambiri pakati pawo kuti, “Kodi munthu uyu angathe kutipatsa bwanji thupi lake kuti tidye?”

53Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti ngati simungadye thupi la Mwana wa Munthu ndi kumwa magazi ake, simungakhale ndi moyo mwa inu. 54Aliyense amene adya thupi langa ndi kumwa magazi anga ali ndi moyo wosatha ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza. 55Pakuti thupi langa ndi chakudya chenicheni ndipo magazi anga ndi chakumwa chenicheni. 56Aliyense amene adya thupi langa ndi kumwa magazi anga amakhala mwa Ine, ndi Ine mwa iye. 57Monga Atate amoyo anandituma Ine, ndipo ndili ndi moyo chifukwa cha Atatewo, chomwechonso amene adya thupi langa adzakhala ndi moyo chifukwa cha Ine. 58Ichi ndiye chakudya chimene chinatsika kuchokera kumwamba. Makolo athu akale anadya mana ndi kufa, koma iye amene adya chakudya ichi, adzakhala ndi moyo nthawi yonse.” 59Iye ankanena izi pamene ankaphunzitsa mʼsunagoge mu Kaperenawo.

Ophunzira Ambiri Aleka Kutsata Yesu

60Pakumva izi ambiri a ophunzira ake anati, “Ichi ndi chiphunzitso chovuta. Angachilandire ndani?”

61Pozindikira kuti ophunzira ake ankangʼungʼudza, Yesu anawafunsa kuti, “Kodi izi zikukukhumudwitsani? 62Nanga mutaona Mwana wa Munthu akukwera kupita kumene Iye anali poyamba! 63Mzimu Woyera apereka moyo, thupi silipindula kanthu. Mawu amene ndayankhula kwa inu ndiwo mzimu ndipo ndi moyo. 64Komabe alipo ena mwa inu amene sakukhulupirira.” Pakuti Yesu ankadziwa kuyambira pachiyambi ena mwa iwo amene samakhulupirira ndi amene adzamupereka Iye. 65Iye anapitiriza kunena kuti, “Ichi ndi chifukwa chake ndinakuwuzani kuti palibe wina angabwere kwa Ine pokhapokha Atate atamuthandiza.”

66Kuyambira nthawi imeneyi ophunzira ake ambiri anabwerera ndipo sanamutsatenso Iye.

67Yesu anafunsa khumi ndi awiriwo kuti, “Kodi inu mukufuna kuchokanso?”

68Simoni Petro anamuyankha Iye kuti, “Ambuye, ife tidzapita kwa yani? Inu muli ndi mawu amoyo wosatha. 69Ife tikhulupirira ndi kudziwa kuti Inu ndinu Woyerayo wa Mulungu.”

70Kenaka Yesu anayankha kuti, “Kodi Ine sindinakusankheni inu khumi ndi awiri? Komabe mmodzi wa inu ndi mdierekezi.” 71(Iye amanena Yudasi, mwana wa Simoni Isikarioti amene ngakhale anali mmodzi mwa khumi ndi awiriwo, anali woti adzamupereka).

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Иохан 6:1-71

Насыщение более пяти тысяч человек

(Мат. 14:13-21; Мк. 6:32-44; Лк. 9:10-17)

1После этого Исо переправился на другую сторону Галилейского, или, как его ещё называют, Тивериадского озера. 2За Ним последовало множество людей, потому что они видели знамения, которые Исо творил, исцеляя больных. 3Исо поднялся на склон горы и сел там со Своими учениками. 4Приближалось время иудейского праздника Освобождения.

5Когда Исо поднял глаза и увидел множество людей, идущих к Нему, Он сказал Филиппу:

– Где бы нам купить хлеба, чтобы накормить этих людей?

6Он спросил это для того, чтобы испытать Филиппа, а Сам Он уже знал, что будет делать. 7Филипп ответил:

– Если купить хлеба и на двести серебряных монет6:7 Букв.: «двести динариев». Динарий – римская монета, примерно равная дневному заработку наёмного работника (см. Мат. 20:2)., то этого не хватит даже, чтобы раздать каждому по кусочку!

8Другой Его ученик, Андер, брат Шимона Петруса, сказал:

9– Тут есть мальчик, у которого пять ячменных лепёшек и две рыбки, но разве этого хватит на всех?

10Исо сказал:

– Велите людям возлечь.

Там было много травы, и все возлегли на траву. Одних только мужчин присутствовало около пяти тысяч. 11Исо взял лепёшки, поблагодарил за них Всевышнего и раздал возлежавшим, так что каждый брал, сколько хотел. То же самое Он сделал и с рыбой. 12Когда все наелись, Он сказал Своим ученикам:

– Соберите оставшиеся куски, чтобы ничего не пропало6:12 Иудеям запрещалось оставлять хлеб лежащим на земле. Такой же обычай мы наблюдаем и у жителей Центральной Азии..

13Они собрали и наполнили двенадцать корзин тем, что осталось у тех, кто ел, от пяти ячменных лепёшек. 14Когда люди увидели это знамение, сотворённое Исо, они начали говорить:

– Он точно Тот Пророк, Который должен прийти в мир6:14 См. Втор. 18:15, 18; Ин. 1:45; Деян. 3:18-24..

15Исо понял, что они хотят насильно поставить Его царём6:15 Иудеи неверно понимали роль Масеха. Они надеялись на то, что Масех возглавит вооружённую борьбу против римских оккупантов и свергнет их гнёт, даровав Исроилу процветание и величие. Но Исо пришёл освободить нас от власти греха (см. Мат. 1:21)., и поэтому снова ушёл на гору один.

Хождение Исо Масеха по воде

(Мат. 14:22-33; Мк. 6:45-51)

16Когда наступил вечер, ученики Исо спустились к озеру 17и, сев в лодку, поплыли через озеро в Капернаум. Было уже темно, а Исо всё не было. 18Озеро разбушевалось, так как подул сильный ветер. 19Проплыв пять-шесть километров6:19 Букв.: «двадцать пять или тридцать стадий»., они увидели Исо, идущего по воде и приближающегося к лодке. Ученики испугались.

20– Это Я, не бойтесь, – сказал Исо.

21Они хотели взять Его в лодку, и лодка в тот же миг оказалась у берега, к которому они плыли.

Исо Масех – истинный хлеб с небес

22На следующий день народ, оставшийся на противоположном берегу озера, вспомнил, что там была только одна лодка. Они знали, что Исо не садился в эту лодку вместе со Своими учениками и что ученики отправились одни. 23К берегу подошли потом другие лодки из Тивериады и тоже пристали там, где народ ел хлеб после того, как Повелитель произнёс благодарственную молитву. 24Когда люди обнаружили, что ни Исо, ни Его учеников там нет, они сели в лодки и отправились в Капернаум искать Исо. 25Они нашли Его на противоположном берегу и спросили:

– Учитель, когда Ты сюда пришёл?

26Исо ответил:

– Говорю вам истину, вы ищете Меня не потому, что видели знамения, а потому, что ели хлеб и наелись досыта. 27Заботьтесь не о временной пище, а о пище, дающей жизнь вечную, которую Ниспосланный как Человек даст вам, потому что Его избрал Всевышний, Небесный Отец.

28Они спросили:

– Что же нам делать, чтобы творить дела, угодные Всевышнему?

29Исо ответил:

– Дело, угодное Всевышнему, – это верить в Того, Кого Всевышний послал.

30Они спросили:

– Какое знамение Ты мог бы нам показать, чтобы мы поверили Тебе? Что Ты можешь сделать? 31Например, отцы наши ели манну6:31 Манна (переводится как: «Что это?») – название, данное иудеями тому небесному хлебу, которым Всевышний кормил их в течение 40 лет странствования в пустыне (см. Исх. 16). в пустыне, как об этом написано: «Он дал им хлеб с небес»6:31 Неем. 9:15; см. также Заб. 77:24; 104:40..

32Исо сказал им:

– Говорю вам истину, это не Мусо дал вам хлеб с небес, а Мой Отец даёт вам истинный хлеб с небес. 33Потому что хлеб Всевышнего – это Тот, Кто приходит с небес и даёт миру жизнь.

34Тогда они стали просить Его:

– Господин, давай нам всегда такой хлеб.

35Исо сказал:

– Я Сам и есть хлеб жизни. Кто приходит ко Мне, тот никогда не останется голодным, и кто верит Мне, тот не будет испытывать жажды. 36Но как Я уже говорил вам, вы видели Меня и всё равно не верите. 37Все, кого Отец дал Мне, непременно придут ко Мне, и кто придёт ко Мне, того Я никогда не прогоню. 38Ведь Я пришёл с небес не для того, чтобы делать то, что Сам хочу, но чтобы исполнять волю Того, Кто послал Меня. 39А воля Пославшего Меня заключается в том, чтобы Я не потерял никого из тех, кого Он Мне дал, но чтобы в Последний день Я воскресил их. 40Воля Моего Отца заключается в том, чтобы каждый, кто видит Сына и верит в Него, имел жизнь вечную, и Я воскрешу его в Последний день.

41Бывших там иудеев разозлило то, что Исо сказал: «Я хлеб, пришедший с небес». 42Они говорили:

– Разве Он не Исо, сын Юсуфа?6:42 См. сноску на 1:45. Мы же знаем и отца Его, и мать! Как Он может говорить: «Я пришёл с небес»?

43Исо сказал:

– Не возмущайтесь. 44Никто не может прийти ко Мне, если Отец, Который послал Меня, не привлечёт его, и Я воскрешу его в Последний день. 45В Книге Пророков записано: «Они будут все научены Всевышним»6:45 Ис. 54:13.. Каждый, кто слушает Отца и учится у Него, приходит ко Мне. 46Но никто не видел Отца, кроме Пришедшего от Всевышнего, только Он видел Отца6:46 См. сноску на 1:18.. 47Говорю вам истину: тот, кто верит в Меня, имеет жизнь вечную. 48Я – хлеб жизни. 49Ваши праотцы ели манну в пустыне и всё же умерли. 50Но этот хлеб, сходящий с небес, таков, что человек, который ест его, не умрёт. 51Я – живой хлеб, пришедший с небес. Кто ест этот хлеб, тот будет жить вечно. Этот хлеб – тело Моё, которое Я отдаю ради жизни мира.

52Тогда между иудеями начался спор:

– Как это Он может дать нам Своё тело, чтобы мы его ели?!

53Исо сказал им:

– Говорю вам истину: если вы не будете есть тела Ниспосланного как Человек и не будете пить Его крови, то в вас не будет и жизни. 54Каждый, кто ест тело Моё и пьёт кровь Мою, имеет жизнь вечную, и Я воскрешу его в Последний день, 55потому что тело Моё – это истинная пища, и кровь Моя – это истинное питьё. 56Тот, кто ест тело Моё и кто пьёт кровь Мою, тот находится во Мне, и Я в нём. 57Как живой Отец послал Меня и как Я живу благодаря Отцу, так и тот, кто питается Мной, будет жить благодаря Мне. 58Хлеб этот пришёл с небес, и он не таков, как тот, который ели ваши праотцы, – они все умерли. Но тот, кто питается этим хлебом, будет жить вечно.

59Исо сказал это, когда учил в молитвенном доме в Капернауме.

Многие из учеников Исо Масеха оставляют Его

60Многие из Его учеников, услышав это, говорили:

– Это какое-то ужасное учение, и кто только может его слушать?

61Исо понял, что Его ученики остались недовольны Его словами, и сказал им:

– Вас это задевает? 62А что, если вы увидите Ниспосланного как Человек поднимающимся туда, где был раньше? 63Только Дух даёт жизнь, человеку это не под силу. В словах, которые Я вам говорил, есть Дух, дающий жизнь. 64Но некоторые из вас не верят (Исо ведь с самого начала знал, кто не верит и кто предаст Его), – 65и Он продолжал: – Поэтому Я говорил вам, что никто не сможет прийти ко Мне, если ему это не будет дано Небесным Отцом.

66Тогда многие из Его учеников оставили Его и больше не ходили с Ним.

67– Не хотите ли и вы Меня оставить? – спросил Он у двенадцати Своих посланников. 68Шимон Петрус ответил:

– Повелитель, к кому нам ещё идти? У Тебя слова вечной жизни. 69Мы верим и знаем, что Ты – Святой Всевышнего.

70Исо ответил:

– Не Я ли избрал вас, всех двенадцать? И всё же один из вас – дьявол!

71Он имел в виду Иуду, сына Шимона Искариота, который, хоть и был одним из двенадцати, в будущем предал Его.